< Deuteronomo 2 >

1 Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
Then we turned, and took our journey into the wilderness by the way to the Red Sea, as Jehovah spoke to me. And we encompassed mount Seir many days.
2 Ndipo Yehova anati kwa ine,
And Jehovah spoke to me, saying,
3 “Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
Ye have encompassed this mountain long enough, turn northward.
4 Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
And command thou the people, saying, Ye are to pass through the border of your brothers the sons of Esau, who dwell in Seir, and they will be afraid of you. Take ye good heed to yourselves therefore.
5 Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
Do not contend with them, for I will not give you of their land, no, not so much as for the sole of the foot to tread on, because I have given mount Seir to Esau for a possession.
6 Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
Ye shall purchase food from them for money, that ye may eat, and ye shall also buy water from them for money, that ye may drink.
7 Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
For Jehovah thy God has blessed thee in all the work of thy hand. He has known thy walking through this great wilderness. These forty years Jehovah thy God has been with thee; thou have lacked nothing.
8 Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
So we passed by from our brothers the sons of Esau, who dwell in Seir, from the way of the Arabah from Elath and from Ezion-geber. And we turned and passed by the way of the wilderness of Moab.
9 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
And Jehovah said to me, Do not vex Moab, neither contend with them in battle, for I will not give thee of his land for a possession, because I have given Ar to the sons of Lot for a possession.
10 (Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
(The Emim dwelt in it formerly, a people great, and many, and tall, as the Anakim.
11 Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
These also are accounted Rephaim, as the Anakim, but the Moabites call them Emim.
12 Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
The Horites also dwelt in Seir formerly, but the sons of Esau succeeded them. And they destroyed them from before them, and dwelt in their stead, as Israel did to the land of his possession, which Jehovah gave to them.)
13 Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
Now rise up, and get you over the brook Zered. And we went over the brook Zered.
14 Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
And the days in which we came from Kadesh-barnea, until we came over the brook Zered, were thirty-eight years; until all the generation of the men of war were consumed from the midst of the camp, as Jehovah swore to them.
15 Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
Moreover the hand of Jehovah was against them, to destroy them from the midst of the camp, until they were consumed.
16 Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
So it came to pass, when all the men of war were consumed and dead from among the people,
17 Yehova anati kwa ine,
that Jehovah spoke to me, saying,
18 “Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
Thou are this day to pass over Ar, the border of Moab.
19 Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
And when thou come near opposite the sons of Ammon, do not vex them, nor contend with them, for I will not give thee of the land of the sons of Ammon for a possession, because I have given it to the sons of Lot for a possession.
20 (Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
(That also is accounted a land of Rephaim. Rephaim dwelt in it formerly, but the Ammonites call them Zamzummim,
21 Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
a people great, and many, and tall, as the Anakim. But Jehovah destroyed them before them, and they succeeded them, and dwelt in their stead,
22 Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
as he did for the sons of Esau, who dwell in Seir, when he destroyed the Horites from before them. And they succeeded them, and dwelt in their stead even to this day.
23 Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
And the Avvim, who dwelt in villages as far as Gaza, the Caphtorim, who came forth out of Caphtor, destroyed them, and dwelt in their stead.)
24 “Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
Rise ye up, take your journey, and pass over the valley of the Arnon. Behold, I have given into thy hand Sihon the Amorite, king of Heshbon, and his land. Begin to possess it, and contend with him in battle.
25 Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
This day I will begin to put the dread of thee and the fear of thee upon the peoples who are under the whole heaven, who shall hear the report of thee, and shall tremble, and be in anguish because of thee.
26 Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
And I sent messengers out of the wilderness of Kedemoth to Sihon king of Heshbon with words of peace, saying,
27 “Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
Let me pass through thy land. I will go along by the highway, I will turn neither to the right hand nor to the left.
28 Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
Thou shall sell me food for money, that I may eat, and give me water for money, that I may drink. Only let me pass through on my feet,
29 monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
as the sons of Esau who dwell in Seir, and the Moabites who dwell in Ar, did to me, until I shall pass over the Jordan into the land which Jehovah our God gives us.
30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
But Sihon king of Heshbon would not let us pass by him, for Jehovah thy God hardened his spirit, and made his heart obstinate, that he might deliver him into thy hand, as at this day.
31 Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
And Jehovah said to me, Behold, I have begun to deliver up Sihon and his land before thee. Begin to possess, that thou may inherit his land.
32 Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
Then Sihon came out against us, he and all his people, to battle at Jahaz.
33 Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
And Jehovah our God delivered him up before us. And we smote him, and his sons, and all his people.
34 Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
And we took all his cities at that time, and utterly destroyed every inhabited city, with the women and the little ones; we left none remaining.
35 Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
We only took the cattle for a prey to ourselves, with the spoil of the cities which we had taken.
36 Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
From Aroer, which is on the edge of the valley of the Arnon, and from the city that is in the valley, even to Gilead, there was not a city too high for us. Jehovah our God delivered up all before us.
37 Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
Only to the land of the sons of Ammon thou did not come near, all the side of the river Jabbok, and the cities of the hill-country, and wherever Jehovah our God forbad us.

< Deuteronomo 2 >