< Deuteronomo 2 >

1 Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
Saa vendte vi om og brød op til Ørkenen i Retning af det røde Hav, saaledes som HERREN havde paalagt mig, og i lang Tid vandrede vi rundt om Se'irs Bjerge.
2 Ndipo Yehova anati kwa ine,
Da sagde HERREN til mig:
3 “Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
»Nu har I længe nok vandret rundt om Bjergene her; vend eder nu mod Nord!
4 Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
Men byd Folket og sig: Naar I nu drager igennem eders Brødres, Esaus Sønners, Landemærker, de, som bor i Se'ir, og de bliver bange for eder, saa skal I tage eder vel i Vare
5 Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
for at indlade eder i Krig med dem; thi jeg vil ikke give eder saa meget som en Fodsbred af deres Land; thi Esau har jeg givet Se'irs Bjerge i Arv og Eje.
6 Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
Fødevarer at spise skal I købe af dem for Penge, ogsaa Vand at drikke skal I købe af dem for Penge;
7 Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
thi HERREN din Gud har velsignet dig i alt, hvad du har taget dig for, han har sørget for dig paa din Vandring gennem denne store Ørken; i fyrretyve Aar har HERREN din Gud nu været med dig, du har ikke manglet noget.«
8 Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
Derpaa drog vi fra Elat og Ezjongeber ad Arabavejen gennem vore Brødres, Esaus Sønners Land, de, som bor i Se'ir; saa drejede vi af og drog videre ad Vejen til Moabs Ørken.
9 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
Og HERREN sagde til mig: »Du maa ikke angribe Moab eller indlade dig i Krig med dem, thi jeg vil ikke give dig noget af deres Land i Eje; thi Lots Sønner har jeg givet Ar i Eje.
10 (Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
(Fordum beboedes det af Emiterne, et stort og talrigt Folk, kæmpestore som Anakiterne;
11 Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
ogsaa de henregnes ligesom Anakiterne til Refaiterne, men Moabiterne kalder dem Emiter.
12 Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
I Se'ir boede derimod fordum Horiterne, som Esaus Sønner drev bort og udryddede foran sig, hvorefter de bosatte sig der i deres Sted, ligesom Israel gjorde ved sit Ejendomsland, som HERREN gav dem.)
13 Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
Bryd nu op og gaa over Zeredbækken!« Saa gik vi over Zeredbækken.
14 Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
Der var gaaet otte og tredive Aar fra vort Opbrud fra Kadesj-Barnea, til vi gik over Zeredbækken, til hele din Slægt af vaabenføre Mænd var uddød af Lejren, saaledes som HERREN havde svoret dem;
15 Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
ogsaa HERRENS Haand havde været imod dem, saa de blev udryddet af Lejren til sidste Mand.
16 Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
Men da alle vaabenføre Mænd var uddøde af Folket,
17 Yehova anati kwa ine,
talede HERREN til mig og sagde:
18 “Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
Naar du nu drager gennem Moabs Landemærker, gennem Ar,
19 Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
og saaledes naar hen til Ammoniterne, saa maa du ikke angribe dem eller indlade dig i Krig med dem, thi jeg vil ikke give dig noget af Ammoniternes Land i Eje; thi det har jeg givet Lots Børn i Eje.
20 (Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
(Ogsaa det henregnes til Refaiternes Land; det beboedes fordum af Refaiter, men Ammoniterne kalder dem Zamzummiter.
21 Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
Det var et stort og talrigt Folk, kæmpestore som Anakiterne. Men HERREN udryddede dem foran dem, saa de drev dem bort og bosatte sig der i deres Sted,
22 Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
ligesom han gjorde for Esaus Sønner, der bor i Se'ir, for hvem han udryddede Horiterne, saa de drev dem bort og bosatte sig der i deres Sted, og de bor der den Dag i Dag.
23 Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
Men Avvijiterne, der boede i Landsbyer i Egnene henimod Gaza, dem drev Kaftorerne, der var udvandret fra Kaftor, bort og bosatte sig der i deres Sted).
24 “Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
Bryd nu op og gaa over Arnonfloden! Se, jeg har givet Hesjbons Konge, Amoriten Sihon, og hans Land i din Haand; giv dig kun til at drive ham bort og føre Krig med ham!
25 Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
Fra i Dag af begynder jeg at vække Frygt og Rædsel for dig hos alle Folkeslag under Himmelen; blot de hører om dig, skal de ryste og bæve for dig!
26 Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
Da udsendte jeg Sendebud fra Kedemots Ørken til Kong Sihon af Hesjbon med følgende fredelige Tilbud:
27 “Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
»Lad mig drage gennem dit Land; jeg skal holde mig til Vejen uden at bøje af til højre eller venstre.
28 Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
Fødevarer at spise skal du sælge mig for Penge, og Vand at drikke skal du give mig for Penge, jeg beder kun om at maatte drage igennem til Fods,
29 monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
saaledes som Esaus Sønner, der bor i Se'ir, og Moabiterne, der bor i Ar, tillod mig, indtil jeg kommer over Jordan ind i det Land, HERREN vor Gud vil give os!«
30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
Men Kong Sihon i Hesjbon vilde ikke tillade os at drage igennem; thi HERREN din Gud forhærdede hans Aand og gjorde hans Hjerte haardt for at give ham i din Haand, som det nu er sket.
31 Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
Derpaa sagde HERREN til mig: »Se, jeg har allerede begyndt at give Sihon og hans Land i din Magt; giv dig kun til at drive ham bort for at tage hans Land i Besiddelse!«
32 Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
Saa rykkede Sihon med alle sine Krigere ud imod os til Kamp ved Jaza;
33 Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
og HERREN vor Gud gav ham i vor Magt, og vi slog ham og hans Sønner og alle hans Krigere.
34 Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
Og vi indtog dengang alle hans Byer og lagde i enhver By Band paa Mænd, Kvinder og Børn uden at lade en eneste undslippe;
35 Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
kun Kvæget tog vi selv som Bytte, tillige med hvad vi røvede i de erobrede Byer.
36 Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
Fra Aroer ved Arnonflodens Bred og Byen, der ligger i Dalen, og til Gilead var der ikke en By, som var os uindtagelig; HERREN vor Gud gav dem alle i vor Magt.
37 Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.
Men paa Ammoniternes Land forgreb du dig ikke, hverken det, der ligger langs Jabbokfloden, eller Byerne i Bjergene, saaledes som HERREN vor Gud havde paabudt.

< Deuteronomo 2 >