< Deuteronomo 19 >

1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
Wakati Yahwe Mungu wenu anayafutilia mbali mataifa, yale ambayo Yahwe Mungu wenu anawapa nchi yao, na wakati mnakuja kwao na kuishi katika miji yao na nyumba,
2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
mnapaswa kuchagua miji mitatu kwa ajili yenu katikati mwa nchi yenu ambayo Yahwe Mungu anawapa kuimiliki.
3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
Mnapaswa kujenga barabara na kugawa mipaka ya nchi yenu katika maeneo matatu, nchi ambayo Yahwe Mungu wenu anafanya kuimiliki, ili kwamba kila mmoja anayeua mtu mwingine apate kukimbia hapo.
4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
Hii ni sheria kwa ajili ya mtu anayeua mwingine na anayekimbilia huko kuishi: yeyote auae jirani yake bila kujua, na hapo awali hakumchukia-
5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
kama wakati mtu aingiapo katika msitu pamoja na jirani yake kukata kuni, na mkono wake ukata mti chini kwa shoka, na kichwa uteleza kutoka kwenye mpini na kumpiga jirani yake mpaka akafa- basi mtu huyu anapaswa kukimbilia katika moja ya miji hii na kuishi.
6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
Vinginevyo damu ya mlipiza kisasi atamfuata yeye aliyetoa uhai, na kwa hasira kali anampita kwa sababu ilikuwa safari ndefu. Na anampiga na kumuua, ijapokuwa mtu huyo akustahili kufa; na hata akustahili adhabu ya kifo kwa sababu hakumchukia jirani yake kabla hili halijatokea.
7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
Basi sasa ninakuamuru kuchagua miji mitatu kwa ajili yako.
8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
Kama Yahwe Mungu wenu apanua mipaka yenu, kama alivyoapa kwa mababu zenu kufanya, na kuwapa nchi yote ambayo amewaahadia kuwapa mababu zenu;
9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
kama mnazishika amri hizi zote kuzifanya, ambazo ninakuamuru leo- amri za kumpenda Yahwe Mungu wenu na daima kutembea katika njia zake, basi mnapaswa kuongeza miji mitatu zaidi kwa ajili yenu, isipokuwa ile mitatu.
10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
Fanya hivi ili kwamba damu isiyo na hatia isimwangwe katikati ya nchi ambayo Yahwe Mungu wenu anawapa kwa ajili ya urithi, ili kwamba pasiwepo hatia ya damu kwenu.
11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
Lakini kama yeyote anamchukia jirani yake, uongo unamsubiri, uinuka dhidi yake, na majeraha ya kufa kwake ili kwamba anakufa, na kama basi anakimbia katika moja ya miji hii-
12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
basi wazee wa mji wake wanapaswa kumtoa na kumrudisha toka huko, na kumkabizi katika mkono wa ndugu mhusika, ili kwamba amuue.
13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
Jicho lako halipaswi kumuonea huruma; badala yake; unapaswa kuondoa hatia ya damu kutoka Israel, ili kwamba iwe vizuri kwako.
14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Haupaswi kuondoa alama ya jirani yako ambayo wameweka katika eneo muda mrefu, katika urithi wako ambao utarithi, katika nchi ambayo Yahwe Mungu wako anakupa kumiliki.
15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
Shahidi moja peke hapaswi kuinuka dhidi ya mtu kwa ajili ya uovu wowote, au kwa ajili ya dhambi yoyote, katika jambo lolote ambalo amefanya dhambi; kwa kinywa cha mashahidi wawili, au kwa kinywa cha mashahidi watatu, kunapaswa jambo lolote lilithibitishwe.
16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
Kama ushuhuda wa mtu asiye na haki anainua dhidi ya mtu yeyote kushuhudia dhidi yake kwa mambo mabaya.
17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
Basi watu wote wawili, mmoja kati ya yule utata upo, anapaswa kusimama mbele ya Yahwe, mbele ya makuhani na waamuzi ambao wanatumika siku hizo.
18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
Waamuzi wanapaswa kuchunguza kwa uangalifu; ona, kama ushahidi ni ushahidi wa uongo na umeshuhudiwa kwa uongo dhidi ya ndugu yake,
19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
basi unapaswa kufanya kwake, kama alivyokusudia kufanya kwa ndugu yake, na utaondoa uovu kutoka miongoni mwenu.
20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
Basi wale wanaobaki watasikia na kuogopa, na kuanzia hapo na kuendelea hawatafanya tena aina ya ouvu miongoni mwao.
21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.
Macho yako hapaswi kuona huruma; maisha yatalipa kwa maisha, jicho kwa jicho, jino kwa jino, mkono kwa mkono, mguu kwa mguu.

< Deuteronomo 19 >