< Deuteronomo 19 >
1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
Lorsque le Seigneur ton Dieu aura détruit les nations dont il va te livrer la terre, et que tu la posséderas, et que tu habiteras dans les villes et dans les maisons,
2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
Tu sépareras trois villes au milieu de la terre que le Seigneur ton Dieu te donnera en possession,
3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
Aplanissant soigneusement la voie; et tu partageras en trois parties égales toute l’étendue de ta terre, afin que le fugitif pour cause d’homicide ait dans le voisinage où pouvoir se réfugier.
4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
Voici la loi de l’homicide fuyant, dont la vie doit être conservée: Celui qui a frappé son prochain, sans s’en apercevoir, et qui est reconnu pour n’avoir eu hier et avant-hier aucune haine contre lui,
5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
Mais pour être allé simplement avec lui dans la forêt couper du bois, si en coupant le bois la cognée est échappée de sa main, et que le fer sortant du manche ait frappé son ami et l’ait tué, celui-là se réfugiera dans une des susdites villes, et vivra;
6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
De peur que le plus proche parent de celui dont le sang a été versé, excité par sa douleur, ne le poursuive et ne l’atteigne, si le chemin est trop long, et ne frappe l’âme de celui qui ne mérite point la mort, parce qu’il est démontré qu’il n’a eu auparavant aucune haine contre celui qui a été tué.
7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
C’est pourquoi je t’ordonne de placer les trois villes dans une égale distance entre elles.
8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
Mais lorsque le Seigneur ton Dieu aura étendu tes limites, comme il l’a juré à tes pères, et qu’il t’aura donné toute la terre qu’il leur a promise,
9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
(Si cependant tu gardes ses commandements, et que tu fasses ce qu’aujourd’hui je te prescris: que tu aimes le Seigneur ton Dieu et que tu marches dans ses voies en tout temps) tu ajouteras trois autres villes, et tu doubleras ainsi le nombre des trois susdites villes,
10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
Afin qu’un sang innocent ne soit pas versé au milieu de la terre que le Seigneur ton Dieu te donnera pour la posséder, afin que tu ne sois pas coupable de sang.
11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
Mais si quelqu’un, haïssant son prochain, tend des pièges à sa vie, et que, se levant, il le frappe, et que, celui-ci étant mort, il s’enfuie dans une des susdites villes,
12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
Les anciens de sa ville enverront, et l’enlèveront du lieu de refuge et le livreront à la main du parent de celui dont le sang a été versé, et il mourra.
13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
Tu n’auras pas pitié de lui, et tu ôteras d’Israël le sang innocent, afin que bien t’arrive.
14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Tu n’enlèveras, et tu ne déplaceras point les bornes de ton prochain, que des prédécesseurs ont posées dans ta possession que le Seigneur ton Dieu te donnera dans la terre que tu recevras pour la posséder.
15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
Il ne se présentera point un seul témoin contre quelqu’un, quel que soit son péché et son crime; mais c’est sur la parole de deux ou trois témoins que tout sera avéré.
16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
S’il s’élève un témoin menteur contre un homme, l’accusant de prévarication,
17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
Les deux qui sont en cause viendront devant le Seigneur en la présence des prêtres et des juges qu’il y aura en ces jours-là.
18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
Et lorsqu’après avoir fait la plus exacte perquisition, ils auront trouvé que le faux témoin a dit contre son frère un mensonge,
19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Ils lui rendront ce qu’il avait eu dessein de faire à son frère, et tu ôteras le mal d’au milieu de toi,
20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
Afin que tous les autres entendant, éprouvent de la crainte, et qu’ils n’osent nullement faire de telles choses.
21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.
Tu n’auras point pitié de lui; mais tu exigeras âme pour âme, œil pour œil, dent pour dent, main pour main, pied pour pied.