< Deuteronomo 19 >

1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
When the Lord thy God shall have cut off the nations, whose land the Lord thy God giveth thee, and thou hast driven them out, and dwellest in their cities, and in their houses:
2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
Then shalt thou set apart three cities for thyself, in the midst of thy land, which the Lord thy God giveth thee to possess it.
3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
Thou shalt put in order for thyself the [way to them], and divide into three parts the territory of thy land, which the Lord thy God will give thee to inherit, and it shall serve, that every man-slayer may flee thither.
4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
And this is the case of the man-slayer, who shall flee thither, that he may live: Whoso smiteth his neighbor without knowledge, when he hath not been an enemy to him in time past;
5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
And he that goeth into the forest with his neighbor to hew wood, and his hand fetcheth a stroke with the axe to cut down the tree, and the iron slippeth from the helve, and striketh his neighbor, that he die: this one shall flee unto one of these cities, and live;
6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
That the avenger of the blood pursue not the manslayer, while his heart is hot, and overtake him, because the way is long, and smite him dead; whereas he deserveth not a judgment of death, inasmuch as he was not an enemy to him in time past.
7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
Therefore do I command thee, saying, Three cities shalt thou set apart for thyself.
8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
And if the Lord thy God enlarge thy boundary, as he hath sworn unto thy fathers, and give thee all the land which he hath spoken to give unto thy fathers;
9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
Because thou dost keep all this commandment to do it, which I command thee this day, to love the Lord thy God, and to walk in his ways all the days: then shalt thou add for thyself three cities more, unto these three;
10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
That innocent blood be not shed in the midst of thy land, which the Lord thy God giveth thee for an inheritance, and blood-guiltiness be brought upon thee.
11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
But if any man be an enemy to his neighbor, and he lie in wait for him, and rise up against him, and smite him mortally so that he die, and he flee unto one of these cities:
12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
Then shall the elders of his city send and fetch him thence, and they shall deliver him into the hand of the avenger of the blood, that he may die.
13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
Thy eye shall not look with pity on him; but thou shalt put away the [shedding of] innocent blood from Israel, that it may go well with thee.
14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Thou shalt not remove the landmark of thy neighbor, which they of old time have set, in thy inheritance which thou shalt inherit, in the land that the Lord thy God giveth thee to possess it.
15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
There shall not rise up one single witness against a man for any iniquity, or for any sin, in any sin that he sinneth: upon the evidence of two witnesses, or upon the evidence of three witnesses, must a case be established.
16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
If a witness of violence rise up against any man to testify against him for any wrong:
17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
Then shall both the men, who have the controversy, stand before the Lord, before the priests and the judges, who shall be in those days;
18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
And the judges shall inquire diligently; and, behold, if the witness be a false witness, he hath testified a falsehood against his brother:
19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Then shall ye do unto him, as he had purposed to do unto his brother; and thou shalt put away the evil from the midst of thee.
20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
And those who remain shall hear, and be afraid, and shall henceforth commit no more any such evil thing in the midst of thee.
21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.
And thy eye shall have no pity; but life [shall go] for life, eye for eye, tooth for tooth, hand for hand, foot for foot.

< Deuteronomo 19 >