< Deuteronomo 19 >

1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
Kad Jahve, Bog tvoj, istrijebi narode čiju zemlju tebi daje te kad ih istjeraš i nastaniš se u njihovim gradovima i domovima,
2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
u zemlji koju ti Jahve, Bog tvoj, daje u baštinu, odvoji tri grada.
3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
Načini put onamo, a onda područje zemlje koju ti Jahve, Bog tvoj, daje u baštinu podijeli natroje, tako da svaki ubojica može onamo uteći.
4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
Ovo je slučaj u kojemu ubojica može onamo pobjeći i spasiti svoj život: kad tko ubije svoga bližnjega nehotice, a da ga prije nije mrzio;
5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
primjerice, kad ode sa svojim bližnjim u šumu da siječe drva, zamahne sjekirom u ruci da obori drvo, gvožđe odleti s držalice i pogodi njegova druga te on pogine: takav ubojica neka uteče u jedan od tih gradova i spasit će život.
6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
Inače bi krvni osvetnik, progoneći u svom bijesu ubojicu - kad bi put bio predug - mogao gonjenoga stići i pogubiti ga, iako taj nije zaslužio smrt budući da ubijenoga nije otprije mrzio.
7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
Stoga ti nalažem: tri grada odvoji!
8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
A kad Jahve, Bog tvoj, proširi tvoje područje, kao što se zakleo ocima tvojim, i dadne ti svu zemlju koju je obećao tvojim ocima,
9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
budeš li držao i vršio sve ove zapovijedi što ti ih danas nalažem i ljubio Jahvu, Boga svoga, te hodio njegovim putovima sve vrijeme - onda ovim gradovima dodaj još tri grada:
10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
tako se neće prolijevati nedužna krv u tvojoj zemlji koju ti Jahve daje u baštinu i nećeš se krvlju okaljati.
11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
Ali ako tko mrzi svoga bližnjega i vreba ga, skoči na nj i ubije ga, a zatim pobjegne u jedan od tih gradova,
12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
onda neka starješine onoga grada izvedu ubojicu i predaju ga u ruke krvnom osvetniku da ga pogubi.
13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
Neka ga oko tvoje ne sažaljuje! Tako ćeš u Izraelu iskorijeniti prolijevanje nedužne krvi i bit ćeš sretan.
14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Nemoj pomicati susjedova međaša kojim su stari razmeđašili tvoj posjed što ćeš ga naslijediti u zemlji koju ti Jahve, Bog tvoj, daje u baštinu.
15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
Neka ne ustaje jedan jedini svjedok protiv čovjeka ni za koju krivnju i ni za kakav zločin. Kakav god bio prekršaj, neka presuda počiva na iskazu dvojice ili trojice svjedoka.
16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
Ako kakav krivi svjedok ustane protiv koga optužujući ga za pobunu,
17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
onda obojica koja se parbe neka stupe pred Jahvu, pred svećenika i suce koji budu vršili službu u to vrijeme.
18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
Neka suci provedu temeljitu istragu. Bude li se pokazalo da je svjedok lažan i da je lažno svjedočio protiv svoga brata,
19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
učinite mu onako kako je on kanio svome bratu. Iskorijeni zlo iz svoje sredine!
20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
Drugi će, kad o tome čuju, pobojati se te više neće činiti takva zla u tvojoj sredini.
21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.
Neka ti se oko ne sažaljuje! Život za život; oko za oko; zub za zub; ruka za ruku; noga za nogu.

< Deuteronomo 19 >