< Deuteronomo 18 >
1 Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
“Abaphristi abangabaLevi ngempela, isizwana sonke sabaLevi kabangabi lesabelo loba ilifa ndawonye labako-Israyeli. Bazaphila ngemihlatshelo yokudla enikelwa kuThixo, ngoba leli yilo ilifa labo.
2 Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
Abayikuba lelifa phakathi kwabafowabo; uThixo uyilifa labo, njengokuthembisa kwakhe.
3 Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
Le yiyo ingxenye yabaphristi ezavela emihlatshelweni yabantu eyenkunzi loba eyemvu: umkhono, inhloko kanye lezangaphakathi.
4 Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
Kufanele libaphe izithelo zakuqala zamabele enu, iwayini elitsha lamafutha, uboya bakuqala ekugundweni kwezimvu zenu,
5 pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
ngoba uThixo uNkulunkulu wenu ubakhethile bona kanye lezizukulwane zabo phakathi kwazo zonke izizwana zenu ukuze kube yibo abazakwenza umsebenzi wokukhonza ebizweni likaThixo ngezikhathi zonke.
6 Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
Nxa umLevi angasuka kwelinye lamadolobho enu loba kungaphi kwelabako-Israyeli lapho abehlala khona, abeseziletha ngokuzimisela endaweni ezakhethwa nguThixo,
7 kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
angenza umsebenzi wokukhonza ebizweni likaThixo uNkulunkulu wakhe njengabo bonke abafowabo abangabaLevi abasebenzela khonapho phambi kukaThixo.
8 Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
Uzakwabelana labanye bakhe ngokulinganayo kulokho abakuzuzayo, lanxa yena esezuze imali ekuthengisweni kwempahla yakwabo.”
9 Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
“Lapho selingena elizweni uThixo uNkulunkulu wenu alinika lona, lingabozifundisa ukulingisa izenzo ezinengekayo zezinye izizwe khonale.
10 Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
Akungabi lamuntu phakathi kwenu ozakwenza umhlatshelo ngendodana yakhe loba indodakazi yakhe ngomlilo, kangabi ovumisayo loba ochasisa ngemibono, ochasisa imilingo njalo oyenza okuphathelane lobuthakathi,
11 wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
ophosayo, loba isanuse loba isangoma loba obuza kwabafileyo.
12 Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
Loba ngubani owenza lezizinto uyisinengiso kuThixo, kanti njalo ngenxa yezenzo lezi ezinengekayo uThixo uNkulunkulu wenu azazixotsha phambi kwenu lezizizwe.
13 Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Kumele libemsulwa phambi kukaThixo uNkulunkulu wenu.”
14 Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
“Izizwe elizazithathela ilizwe zilalela okwalabo abathakathayo labavumisayo. Kodwa lina, uThixo uNkulunkulu wenu kalivumeli ukukwenza lokho.
15 Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
UThixo uNkulunkulu wenu uzalivusela umphrofethi phakathi kwabafowenu njengami. Libomlalela.
16 Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
Lokhu yikho elakucela kuThixo uNkulunkulu wenu eHorebhi mhla wosuku lokuhlangana lapho elathi, ‘Asingalizwa ilizwi likaThixo uNkulunkulu wethu njalo singaboni umlilo omkhulu futhi, ngoba singafa.’
17 Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
UThixo wathi kimi: ‘Lokho abakutshoyo kuhle.
18 Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
Ngizabavezela umphrofethi onjengawe phakathi kwabafowabo; ngizamfunza amazwi ami, yena nguye ozabatshela konke engizamlaya ngakho.
19 Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
Nxa loba ngubani ongayikulalela amazwi ami azakhulunywa ngumphrofethi ngebizo lami, mina ngokwami yimi engizamelana laye.
20 Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
Kodwa-ke umphrofethi ozenza okhuluma amazwi ami wona kungesiwo engimlaye ngawo ukuba awatsho, loba umphrofethi okhuluma ngebizo labanye onkulunkulu, kumele abulawe.’
21 Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
Lingazitshela lokhu lithi, ‘Singakwazi njani ukuthi lelilizwi kaliveli kuThixo na?’
22 Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.
Nxa lokho okumenyezelwa ngumphrofethi ngebizo likaThixo kungenzakali loba kungagcwaliseki, lokho kuyilizwi eliyabe lingaveli kuThixo. Lowo mphrofethi uyabe ekhuluma ize. Lingamesabi.”