< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
Haupaswi kumtolea dhabihu Yahwe Mungu wako ng'ombe au kondoo aliye na kasoro au kitu chochote kibaya, kwa kuwa hiyo itakuwa chukizo kwa Yahwe Mungu wako.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
Kama kunapatikana miongoni mwenu, ndani ya malango ya mji wowote ambao Yahwe Mungu wenu anawapatia, mwanaume yoyote au mwanamke ambaye anafanya uovu mbele ya Yahwe Mungu wenu kuiharibu agano lake -
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
yoyote ambaye ameenda na kuabudu miungu mingine na kuisujudia, wala jua, mwezi, au kati ya jeshi la mbinguni- hakuna chochote nimekuamuru,
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
na kama ungeambiwa kuhusu hiki, au kama una mifugo- basi unapaswa kufanya uchunguzi wa makini. Kama ni kweli na hakika kwamba chukizo kama hilo limefanyika Israeli-
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
-basi utamleta huyo mwanaume au mwanamke, aliyefanya uovu huu, katika malango ya mji, kwamba mwanaume kabisa au mwanamke, na umponde huyo mtu mpaka kufa.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
Kwa kinywa cha mashahidi wawili, au mashahidi watatu, itakuwa yeye anayepaswa kuuwawa; lakini kwa kinywa cha shahidi mmoja peke hatauwawa.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Mkono wa mashahidi unapaswa kuwa wa kwanza kumuuwa, na badae mkono wa watu wote; na mtamuondoa muovu miongoni mwenu.
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Kama jambo linatokea ambalo ni gumu kwenu kufanya maamuzi- pengine swali la mauaji au kifo cha ajali, haki ya mtu mmoja na haki ya mtu mwingine, au swali moja la aina ya kuzulu kufanyika, au aina nyingine ya jambo-mambo ya utata ndani ya malango yenu, basi utapaswa kwenda kwenye eneo ambalo Yahwe Mungu wako atachagua kama patakatifu pake.
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
Utapaswa kwenda kwa makuhani, wazao wa Lawi, na kwa mwamuzi atakayetumika kwa wakati huo; mtatafuta ushauri wao, na watawapa ninyi maamuzi.
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
Mnapaswa kufuata sheria mliyopewa, katika eneo Yahwe atachagua kama patakatifu pake. Mtakuwa makini kufanya kila kitu ambacho wanawaelekeza kufanya.
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
Fuata sheria wanayowafundisha, na kufanya kulingana na maamuzi wanawapa. Msigeuke kutoka kwa kile wanawambia, kwa kulia au kushoto.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
Yeyote anayefanya kwa kiburi, kwa kutomsikiliza kuhani anayesimama kutumika mbele ya Yahwe Mungu wako, au kwa kutomsikiliza mwamuzi- huyu mtu atakufa; mtaweka mbali uovu kutoka Israeli.
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
Watu wote wanapaswa kusikia na kuogopa, na kutofanya kwa kiburi tena.
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
Wakati mlipokuja kwenye nchi ambayo Yahwe Mungu anawapa, na wakati mnamiliki na kuanza kuishi ndani yake, na halafu unasema, 'Nitajiwekea mfalme juu yangu, kama mataifa yote yanayonizunguka mimi,'
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
basi unapaswa kwa hakika kujiwekea mfalme juu yako mtu yeyote ambaye Yahwe atachagua. Unapaswa kujiweka kama mfalme juu yako mtu yeyote kutoka miongoni mwa ndugu zenu. Haupaswi kuweka mgeni, ambaye si ndugu yenu, juu yenu.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Lakini hapaswi kuzidisha farasi kwa ajili yake, wala kusababisha watu kurudi Misri ili kwamba aweze kuzidisha farasi, kwa kuwa Yahwe alikwisha sema kwako, 'Unapaswa kuanzia sasa usirudi njia hiyo tena.'
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
Na hapaswi kuzidisha wake kwa ajili yake, ili kwamba moyo wake usigeuke kotoka kwa Yahwe; wala hapaswi sana kuzidisha kwa ajili yake fedha au dhahabu.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
Wakati aketipo kwenye kiti cha enzi cha ufalme wake, anapaswa kuandika kwenye kitabu kwa ajili yake nakala ya sheria hii, kutoka kwenye sheria ambayo iko mbele ya makuhani, ambao ni Walawi.
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
Kitabu kinapaswa kuwa na yeye, na anapaswa kusoma ndani yake kwa siku zake zote, ili kwamba aweze kujifunza kumheshimu Yahwe Mungu wako, ili kwamba ashike maneno yote ya sheria hii na amri hizi, kuzishika.
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
Anapaswa kufanya hivi ili kwamba moyo wake usiinuliwe zaidi ya ndugu zake, na ili kwamba asigeuke mbali na amri, kwa kulia au kwa kushoto' kwa kusudi kwamba aweze kuzidisha siku zake katika ufalme wake, yeye na watoto wake, miongoni mwa Israel.

< Deuteronomo 17 >