< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
“Lingenzi umhlatshelo kuThixo uNkulunkulu wenu ngenkabi loba imvu elesici lesolekayo, ngoba lokho kuyisinengiso kuye.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
Nxa kulendoda loba owesifazane ohlala phakathi kwenu kwelinye lamadolobho eliwaphiwa nguThixo uNkulunkulu wenu limfumana esona emehlweni kaThixo uNkulunkulu wenu esephula isivumelwano,
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
njalo ngokwephula imilayo yami esezikhonzela abanye onkulunkulu, ebakhothamela loba ekhonza ilanga loba inyanga loba izinkanyezi zezulu,
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
kube kanti lokhu sekubikiwe kini, kutsho ukuthi kuzamele likuchwayisise ngokupheleleyo. Nxa kuliqiniso njalo sekubonakele ukuthi kuliqiniso lokhu okuyisinengiso okwenzakele ko-Israyeli,
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
thathani leyondoda loba owesifazane lowo owenze lesi senzo esibi limuse esangweni ledolobho lenu limkhande ngamatshe aze afe.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
Ngobufakazi bababili loba abathathu indoda izabulawa, kodwa kakho ozabulawa ngobufakazi bomuntu oyedwa kuphela.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Akuthi ofakazi labo kube yibo abaqalisayo ukumkhanda, besekulandela bonke abanye abantu. Kumele lisuse ububi phakathi kwenu.”
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
“Nxa amacala eza phambi kwemithethwandaba yenu enzima ukuwahlulela, loba awokuchitha igazi, ukwephula imithetho loba awokuhlaselwa, athatheni liye lawo endaweni uThixo uNkulunkulu wenu azayikhetha.
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
Hambani kubaphristi, abangabaLevi, kanye lakumahluleli osesikhundleni okwalesosikhathi. Buzani kibo bona bazalinika isigwebo esifaneleyo.
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
Lina-ke kumele lenze njengokucebisa kwabo endaweni uThixo azayikhetha. Linanzelele ukuthi lenza lokho kanye abaliqondisa ukuba likwenze.
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
Yenzani ngokomthetho njengalokho abalifundisa ngakho lezinqumo abalipha zona. Lingaphambuki kulokho abalitshela khona, liye kwesokudla loba kwesenxele.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
Indoda etshengisela ukudelela iseyisa umahluleli loba umphristi owenza umsebenzi wokukhonza khonapho uThixo uNkulunkulu wenu kumele ibulawe. Kumele lisuse bonke ububi phakathi kuka-Israyeli.
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
Bonke abantu bazakuzwa besabe, bangabe besadelela futhi.”
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
“Ekungeneni kwenu elizweni uThixo uNkulunkulu wenu alinika lona selilithethe laba ngelenu njalo selihlezi kulo, njalo selisithi, ‘Asibekeni inkosi isibuse ukuze sifanane lezinye izizwe esakhelene lazo,’
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
wobani leqiniso lokuthi libeka inkosi ekhethwe nguThixo uNkulunkulu wenu. Kumele abe ngomunye wabafowenu. Lingafaki umuntu wezizweni ukuba alibuse, ongasiye wakini ko-Israyeli.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Inkosi njalo akumelanga izifuyele amabhiza amanengi loba ithume abantu babuyele eGibhithe ukuyazuza amanye khona ngoba uThixo ulitshelile wathi, ‘Lingaphindi liyihambe njalo leyondlela.’
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
Kayingathathi abafazi abanengi funa inhliziyo yayo idukiswe. Kayingazinothisi ngesiliva langegolide elinengi kakhulu.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
Nxa isithatha isihlalo sobukhosi bombuso wayo kayithathe umqulu izilobele kulo umthetho lo iwuthatha encwadini yabaphristi abangabaLevi.
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
Umqulu lowo kawuhlale ukuyo, ihlale iwubala zonke insuku zokuphila kwayo ukuze ifunde ukwesaba uThixo uNkulunkulu wayo, ilandele ngokunanzelela wonke amazwi omthetho lo lalezi izimiso,
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
njalo ukuze ingazenzi ongcono kulabanye abakibo, ingaphambuki emthethweni iye ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo. Ngakho yona kanye lezizukulwane zayo bazabusa isikhathi eside embusweni wayo ko-Israyeli.”

< Deuteronomo 17 >