< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
Thou shalt not sacrifice unto the Lord thy God any bullock, or lamb, whereon there is a blemish, any thing evil; for it is an abomination unto the Lord thy God.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
If there be found in the midst of thee, within any one of thy gates, which the Lord thy God giveth thee. a man or a woman, that doth the wickedness in the eyes of the Lord thy God, to transgress his covenant,
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
And he hath gone and served other gods, and worshipped them, either the sun, or the moon, or any of the host of heaven, which I have prohibited;
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
And it be told thee, and thou hearest of it: then shalt thou inquire diligently; and, behold, if it be true, the thing is certain, such abomination hath been wrought in Israel:
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
Then shalt thou bring forth that man or that woman, who have committed this wicked thing, unto thy gates, the man or the woman, and thou shalt stone them with stones till they die.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
Upon the evidence of two witnesses, or of three witnesses, shall he that is worthy of death be put to death; he shall not be put to death upon the evidence of one witness.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
The hand of the witnesses shall be first upon him to put him to death, and the hand of all the people at the last; and thou shalt put the evil away from the midst of thee.
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
If a matter be unknown to thee for decision, between blood and blood, between plea and plea, and between bodily injury and injury, [or] matters of controversy within thy gates: then shalt thou arise, and get thee up unto the place which the Lord thy God will choose;
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
And thou shalt come unto the priests, the Levites, and unto the judge that may be in those days, and thou shalt inquire, and they shall inform thee of the sentence of the case;
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
And thou shalt do according to the sentence, which they may tell thee from that place which the Lord will choose, and thou shalt observe to do according to all that they may instruct thee;
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
In accordance with the instruction which they may instruct thee, and according to the decision which they may say unto thee, shalt thou do: thou shalt not depart from the sentence which they may tell thee, to the right, or to the left.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
And the man that will act presumptuously, so as not to hearken unto the priest that standeth to minister there before the Lord thy God, or unto the judge, even that man shall die; and thou shalt put away the evil from Israel.
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
And all the people shall hear, and be afraid, and not act presumptuously any more.
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
When thou art come unto the land which the Lord thy God giveth thee, and thou hast taken possession of it, and dwellest therein, and thou sayest, I wish to set a king over me, like all the nations that are round about me:
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
Then mayest thou indeed set a king over thee, the one whom the Lord thy God will choose; [but] from the midst of thy brethren shalt thou set a king over thee; thou mayest not set over thee a stranger, who is not thy brother.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Only he shall not acquire for himself many horses; so that he may not cause the people to return to Egypt, in order to acquire many horses; whereas the Lord hath said unto you, Ye shall henceforth not return on that way any more.
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
Neither shall he take to himself many wives, that his heart may not turn away; nor shall he acquire for himself too much silver and gold.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
And it shall be, when he sitteth upon the throne of his kingdom, that he shall write for himself a copy of this law in a book out of [that which is] before the priests, the Levites;
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
And it shall be with him, and he shall read therein all the days of his life: in order that he may learn to fear the Lord his God, to keep all the words of this law and these statutes, to do them.
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
So that his heart be not lifted up above his brethren, and so that he turn not aside from the commandment, to the right, or to the left: in order that he may live many days in his kingdom, he, and his children, in the midst of Israel.

< Deuteronomo 17 >