< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
Dilia Hina Godema gobele salimusa: , wadela: i o bahoi bulamagau o sibi mae ima. Hina Gode da amo hou higasa.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
Dilia moilai amo ganodini dunu o uda afae da Hina Godema wadela: le hamosea amola Ea gousa: su gugunufinisisia,
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
e da eno ogogosu ‘gode’ liligi o eso o oubi o gasumuni, Gode Ea sia: wadela: musa: ilima nodone sia: ne gadosea,
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
amo sia: nabasea, dilia bai dawa: ma: ne noga: le hogoma. Amo wadela: i hou da dafawane Isala: ili soge ganodini hamoi dagoi ba: sea,
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
amo dunu moilai gadili oule asili, igiga gala: le, medole legema.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
Be hedolo mae medole legema. Ba: su dunu aduna o aduna baligi da ea wadela: i hou dafawane ba: i dagoiba: le fawane, medole legema. Be dunu afae fawane da ba: su dunu esalea, mae medole legema.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Ba: su dunu da degabo amo dunu medole legema: ne, igiga gala: ma: ma. Amasea, dunu huluane da amo igiga medomu. Amasea, dilia da wadela: i hou Isala: ili amo ganodini fadegale fasimu.
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Be moilai fofada: su dunu da fofada: su eno da ilima hamedei agoane ba: sea - amo da medole legesu o sogega gegesu o fasu - dilia da amo dunu dilia Hina Gode Ea ilegei sogebi amoga oule masa.
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
Dilia gobele salasu dunu (Lifai dunu) amola fofada: su dunu bagade amoga adole ba: musa: masa. Ilia da fofada: lalu, sia: dilima olelemu.
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
Ilia da Hina Gode Ea ilegei sogebi amogawi dilima hou olelemu. Dawa: ma! Dilia ilia sia: huluane defele hamoma.
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
Ilia da sema amola hou huluane dilima olelemu. Ilia olelei defele, noga: le hamoma. Lobodafa la: ididili o lobo fofadi la: ididili amoga mae masa be moloidafa gusuba: i masa.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
Be nowa dunu da fofada: su bagade dunu o gobele salasu dunu (amo da Godema hawa: hamonana) amo higasea, amo dunu dilia medole legema. Amo wadela: i hou Isala: ili fi ganodini diala, dilia fadegale fasima.
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
Dunu huluane da amo hou nababeba: le, beda: mu. Amasea, ilia da amo higasu hou bu hame hamomu.
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
Dilia da soge amo dilia Hina Gode da dilima iaha amo ganodini fi dagosea, dilia da na: iyado fi dilima gadenene esala defele hina bagade dunu ilegemusa: dawa: mu.
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
Be dilia hina bagade ilegemusa: dawa: sea, noga: le dawa: ma! Hina Gode Ea ilegei dunu fawane lama. Dilia fidafa dunu fawane lama. Ga fi dunu amo maedafa ilegema.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Amo hina bagade dunu da hosi bagohame hame gagumu. Amola e da ea fi dunu hosi bidi lama: ne Idibidi sogega hame asunasimu. Bai Hina Gode da Ea fi dunu da Idibidi sogega hamedafa buhagima: ne sia: i dagoi.
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
Hina bagade dunu da uda bagohame, amo hame lama: mu. Bai e da Hina Gode Ea hou fisisa: besa: le, uda eno hame lama: mu. E da silifa, gouli amola muni bagade hame lama: mu.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
E da hina bagade hawa: hamosu lalegagusia, e da Gode Ea sema amola Ea olelesu (amo Lifai gobele salasu dunu ilia gagusa) amo huluane dedene gaguma: mu.
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
E da amo buga lalegaguli, eso huluane idilalumu. Amasea, e da amo dawa: le Hina Godema nodone dawa: mu amola mae yolesili, Gode Ea sia: defele lalumu.
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
Amasea, e da gasa fi hou mae hamone, ea hou da ea na: iyado Isala: ili fi amo baligisa e da hame dawa: mu. E da Gode Ea sia: amo giadofamu da hamedei ba: mu. E da hina bagade ouligisu hou ode bagohame hamoma: mu. Amola ea mano da Isala: ili dunu ilima hina bagade ouligisu dunu ode bagohame esalumu.

< Deuteronomo 17 >