< Deuteronomo 16 >

1 Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
Observe le mois des blés nouveaux, et tu feras la Pâque du Seigneur ton Dieu, parce que dans le mois des blés nouveaux, tu es sorti nuitamment de l'Egypte.
2 Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
Tu sacrifieras, pour la Pâque du Seigneur ton Dieu, des bœufs, des brebis et des chèvres, au lieu seul que le Seigneur ton Dieu aura choisi afin que son nom y soit invoqué.
3 Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
Avec la victime, tu ne mangeras pas de pain levé; pendant sept jours, avec ses chairs, tu mangeras des azymes, pain de la mortification, parce qu'à la hâte vous êtes sortis de l'Egypte, et parce qu'il faut vous souvenir du jour de votre sortie d'Egypte, tous les jours de votre vie.
4 Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
On ne verra pas chez toi de pain levé, en tout ton territoire, pendant sept jours; rien ne restera des chairs des victimes que tu auras sacrifiées sur le soir du premier jour.
5 Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
Tu ne pourras sacrifier la Pâque dans aucune des villes que le Seigneur ton Dieu te donne;
6 koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
Mais au lieu seul que le Seigneur ton Dieu aura choisi pour que son nom y soit invoqué; tu sacrifieras la Pâque sur le soir, au coucher du soleil, vers l'heure où tu es sorti de l'Egypte.
7 Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
Tu feras bouillir ou rôtir les chairs, et tu les mangeras au lieu seul qu'aura choisi le Seigneur ton Dieu, et, le lendemain matin, pars, retourne en tes demeures.
8 Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Tu mangeras des azymes pendant six jours; le septième jour, pour finir, sera la fête du Seigneur ton Dieu; tu ne feras ce jour-là aucune œuvre, sauf toutes les choses que l'on fait à cause d'un mort.
9 Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
Tu compteras en toi-même sept semaines, à partir du jour ou ta faux commencera la moisson.
10 Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
Tu célèbreras ensuite la fête des semaines du Seigneur ton Dieu, selon tes facultés, selon ce que t'aura donné le Seigneur ton Dieu.
11 Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
Tu te réjouiras devant le Seigneur ton Dieu, toi et ton fils, et ta fille, et ton serviteur, et la servante, et le lévite, et le prosélyte, et l'orphelin, et la veuve, qui se trouvent parmi vous, au lieu seul que le Seigneur aura choisi pour que son nom y soit invoqué.
12 Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
Et tu te souviendras que tu as été esclave en la terre d'Egypte, et tu observeras et exécuteras les commandements.
13 Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
Tu célèbreras la fête des tabernacles pendant sept jours, lorsque tu auras recueilli, tant sur l'aire que dans le pressoir, les fruits de tes champs.
14 Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
Tu te réjouiras, en cette fête, toi, et ton fils, et ta fille, et ton serviteur, et ta servante, et le lévite, et le prosélyte, et l'orphelin, et la veuve, qui se trouveront dans tes villes.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Tu célèbreras cette fête pendant sept jours en l'honneur du Seigneur ton Dieu, au lieu seul qu'aura choisi le Seigneur, et le Seigneur te bénira en toutes tes récoltes, en toutes œuvres de tes mains, et tu seras plein de joie.
16 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
Trois fois par an, tout mâle parmi vous se présentera devant le Seigneur votre Dieu, au lieu seul qu'aura choisi le Seigneur, pour la fête des azymes, pour la tête des semaines et pour la fête des tabernacles; nul ne se présentera les mains vides devant le Seigneur.
17 Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Chacun de vous offrira selon ses facultés, et selon que le Seigneur l'aura béni.
18 Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
Tu institueras pour toi des juges et des scribes dans les villes que le Seigneur te donne par tribus; ils jugeront le peuple, et rendront des jugements équitables.
19 Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Ils ne feront point pencher la justice, ils ne feront point acception des personnes, ils n'accepteront point de présents; car les présents aveuglent le sage, et ôtent aux justes leur intelligence.
20 Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Vous vous efforcerez de rendre justice selon l'équité, afin que vous viviez et que vous entriez en la terre que le Seigneur vous donne, pour qu'elle soit votre héritage.
21 Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
Tu ne planteras point de bois sacré; tu ne planteras aucun autre arbre auprès de l'autel de ton Dieu.
22 ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.
Tu ne t'érigeras point de colonnes; le Seigneur ton Dieu les exècre.

< Deuteronomo 16 >