< Deuteronomo 16 >
1 Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
Observe le mois d'Abib et célèbre la Pâque en l'honneur de Yahvé ton Dieu, car c'est au mois d'Abib que Yahvé ton Dieu t'a fait sortir d'Égypte de nuit.
2 Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
Tu sacrifieras la Pâque à l'Éternel, ton Dieu, du menu et du gros bétail, dans le lieu que l'Éternel choisira pour y faire résider son nom.
3 Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
Tu ne mangeras pas de pain levé avec elle. Tu mangeras avec lui des pains sans levain pendant sept jours, des pains d'affliction (car tu es sorti du pays d'Égypte en hâte), afin de te souvenir du jour où tu es sorti du pays d'Égypte, tous les jours de ta vie.
4 Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
Il n'y aura pas de levure avec vous dans tout votre territoire pendant sept jours; et aucune des viandes que vous sacrifierez le premier jour, le soir, ne restera toute la nuit jusqu'au matin.
5 Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
Tu ne sacrifieras pas la Pâque dans l'une des portes que l'Éternel, ton Dieu, te donne;
6 koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
mais au lieu que l'Éternel, ton Dieu, choisira pour y faire résider son nom, là tu sacrifieras la Pâque le soir, au coucher du soleil, à l'époque où tu es sorti d'Égypte.
7 Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
Tu la feras rôtir et tu la mangeras dans le lieu que choisira Yahvé ton Dieu. Le matin, tu retourneras dans tes tentes.
8 Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Pendant six jours, tu mangeras des pains sans levain. Le septième jour, il y aura une assemblée solennelle en l'honneur de Yahvé, ton Dieu. Tu ne feras aucun travail.
9 Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
Vous compterez pour vous-mêmes sept semaines. A partir du moment où vous commencerez à mettre la faucille sur le grain sur pied, vous commencerez à compter sept semaines.
10 Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
Vous célébrerez la fête des semaines devant l'Éternel, votre Dieu, avec le tribut d'une offrande volontaire de votre main, que vous donnerez selon la manière dont l'Éternel, votre Dieu, vous bénira.
11 Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
Tu te réjouiras devant l'Éternel, ton Dieu, toi, ton fils, ta fille, ton serviteur, ta servante, le Lévite qui est dans tes portes, l'étranger, l'orphelin et la veuve qui sont parmi toi, dans le lieu que l'Éternel, ton Dieu, choisira pour y faire résider son nom.
12 Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
Tu te souviendras que tu as été esclave en Égypte. Tu observeras et tu mettras en pratique ces lois.
13 Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
Tu célébreras la fête des cabanes pendant sept jours, après avoir ramassé ce qui vient de ton aire et de ta cuve.
14 Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
Tu te réjouiras de ta fête, toi, ton fils, ta fille, ton serviteur, ta servante, le lévite, l'étranger, l'orphelin et la veuve qui sont dans tes portes.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Tu feras une fête à l'Éternel, ton Dieu, pendant sept jours, dans le lieu que l'Éternel choisira, car l'Éternel, ton Dieu, te bénira dans tout ton produit et dans tout le travail de tes mains, et tu seras tout entier dans la joie.
16 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
Trois fois par an, tous tes mâles se présenteront devant l'Éternel, ton Dieu, dans le lieu qu'il choisira: à la fête des pains sans levain, à la fête des semaines et à la fête des kiosques. Ils ne se présenteront pas devant l'Éternel à vide.
17 Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Chacun donnera selon ses moyens, en fonction de la bénédiction que l'Éternel, ton Dieu, t'a accordée.
18 Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
Tu établiras des juges et des officiers dans toutes tes portes, celles que l'Éternel, ton Dieu, te donne, selon tes tribus, et ils jugeront le peuple avec droiture.
19 Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Tu ne pervertiras pas la justice. Tu ne feras pas preuve de partialité. Tu ne prendras pas de pot-de-vin, car le pot-de-vin aveugle les yeux des sages et pervertit les paroles des justes.
20 Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Tu suivras ce qui est tout à fait juste, afin de vivre et d'hériter du pays que l'Éternel, ton Dieu, te donne.
21 Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
Tu ne planteras pas d'ashère d'un arbre quelconque à côté de l'autel de Yahvé ton Dieu, que tu te feras toi-même.
22 ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.
Tu ne te dresseras pas non plus une pierre sacrée que Yahvé ton Dieu déteste.