< Deuteronomo 16 >

1 Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
Tag Vare på Abib Måned og hold Påske for HERREN din Gud; thi i Abib Måned førte HERREN din Gud dig ved Nattetide ud af Ægypten.
2 Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
Og som Påskeoffer til HERREN din Gud skal du slagte Småkvæg og Hornkvæg på det Sted, HERREN din Gud udvælger fil Bolig for sit Navn.
3 Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
Du må ikke spise syret Brød dertil. I syv Dage skal du spise usyret Brød dertil, Trængselsbrød thi i største Hast drog du ud af Ægypten for at du kan ihukomme den Dag, du drog ud af Ægypten, så længe du lever.
4 Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
Hele syv dage må der ikke findes Surdej nogetsteds inden for dine Landemærker. Af Kødet, som du slagter om Aftenen den første Dag må intet ligge Natten over til næste Morgen.
5 Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
Du har ingensteds Lov at slagte Påskeofferet inden dine Porte, som HERREN din Gud giver dig;
6 koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
men på det Sted, HERREN din Gud udvælger til Bolig for sit Navn, der skal du slagte Påskeofferet om Aftenen ved Solnedgang, på det Tidspunkt du drog ud af Ægypten.
7 Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
Og du skal koge det og spise det på det Sted, HERREN din Gud udvælger, og næste Morgen skal du vende hjemad og drage til dine Boliger.
8 Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
I seks dage skal du spise usyrede Brød, og på den syvende skal der være festlig Samling for HERREN din Gud, du må intet Arbejde udføre.
9 Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
Syv Uger skal du tælle frem; den Dag du sætter Seglen til Hornet, skal du begynde at tælle.
10 Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
Så skal du fejre Ugefesten for HERREN din Gud med så mange frivillige Gaver, du vil give, efter som HERREN din Gud velsigner dig.
11 Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
Og du skal være glad for HERREN din Guds Åsyn på det Sted, HERREN din Gud udvælger til Bolig for sit Navn, sammen med din Søn og Datter, din Træl og Trælkvinde, Leviten inden dine Porte, den fremmede, den faderløse og Enken, som bor hos dig.
12 Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
Og du skal komme i Hu, at du var Træl i Ægypten, og omhyggeligt holde disse Anordninger.
13 Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
Løvhyttefesten skal du fejre i syv Dage, når du har indsamlet Udbyttet fra din Tærskeplads og din Perse;
14 Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
og du skal være glad på din Højtid sammen med din Søn og Datter, din Træl og Trælkvinde, Leviten, den fremmede, den faderløse og Enken inden dine Porte.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Syv Dage skal du holde Højtid for HERREN din Gud, på det Sted HERREN udvælger, thi HERREN din Gud vil velsigne dig i alt, hvad du avler, og alt, hvad du arbejder med; derfor skal du kun være glad.
16 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
Tre Gange om Året skal alle af Mandkøn hos dig stedes for HERREN din Guds Åsyn, på det Sted han udvælger, på de usyrede Brøds Fest, Ugefesten og Løvhyttefesten; og man må ikke stedes for HERRENs Åsyn med tomme Hænder;
17 Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
men enhver skal komme med, hvad han kan give efter den Velsignelse, HERREN din Gud giver dig.
18 Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
Dommere og Tilsynsmænd skal du indsætte dig overalt inden dine Porte, som HERREN din Gud vil give dig, rundt om i dine Stammer, og de skal dømme Folket på retfærdig Vis.
19 Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Du må ikke bøje Retten, ikke vise Personsanseelse og ikke tage imod Bestikkelse; thi Bestikkelse gør Vismænd kolde og forplumrer de retfærdiges Sag.
20 Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Ret, kun Ret skal du stræbe efter, for at du kan leve og beholde det Land, som HERREN din Gud vil give dig.
21 Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
Du må ikke plante dig nogen Asjerastøtte, noget som helst Træ ved Siden af det Alter, du rejser for HERREN din Gud.
22 ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.
Heller ikke må du rejse dig nogen Stenstøtte; dem hader HERREN din Gud.

< Deuteronomo 16 >