< Deuteronomo 16 >
1 Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
Ostříhej měsíce Abib, abys slavil Fáze Hospodinu Bohu svému, nebo toho měsíce Abib vyvedl tě Hospodin Bůh tvůj z Egypta v noci.
2 Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
A obětovati budeš Fáze Hospodinu Bohu svému z bravů i skotů na místě, kteréž by vyvolil Hospodin, aby tam přebývalo jméno jeho.
3 Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
Nebudeš v něm jísti nic kvašeného. Za sedm dní jísti budeš přesnice, chléb trápení, (nebo s chvátáním vyšel jsi z země Egyptské), abys pamatoval na den, v kterémž jsi vyšel z země Egyptské, po všecky dny života svého.
4 Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
Aniž spatřín bude u tebe kvas ve všech končinách tvých za sedm dní, a nezůstane nic přes noc masa toho, kteréž bys obětoval u večer toho dne prvního, až do jitra.
5 Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
Nebudeš moci obětovati Fáze v každém městě svém, kteréž Hospodin Bůh tvůj dává tobě,
6 koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
Ale na místě, kteréž by vyvolil Hospodin Bůh tvůj, aby přebývalo tam jméno jeho, tu obětovati budeš Fáze, a to u večer, při západu slunce v jistý čas vyjití tvého z Egypta.
7 Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
Péci pak budeš a jísti na místě, kteréž by vyvolil Hospodin Bůh tvůj, a ráno navracuje se, půjdeš do stanů svých.
8 Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Šest dní jísti budeš přesnice, dne pak sedmého bude slavnost Hospodinu Bohu tvému; ničehož v ní dělati nebudeš.
9 Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
Sedm téhodnů sečteš sobě; od začátku žně začneš počítati sedm téhodnů.
10 Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
Tehdy slaviti budeš slavnost téhodnů Hospodinu Bohu svému; seč budeš moci býti, to dáš dobrovolně vedlé toho, jakžť by požehnal Hospodin Bůh tvůj.
11 Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
I veseliti se budeš před Hospodinem Bohem svým, ty i syn tvůj i dcera tvá, služebník tvůj a děvka tvá, i Levíta, kterýž by byl v branách tvých, a příchozí, sirotek i vdova, kteříž by byli u prostřed tebe, na místě, kteréž by vyvolil Hospodin Bůh tvůj k přebývání tam jména svého.
12 Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
A tak rozpomínati se budeš, že jsi byl služebníkem v Egyptě, když ostříhati a vykonávati budeš ustanovení tato.
13 Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
Slavnost stanů světiti budeš za sedm dní, když shromáždíš s pole svého a z vinice své.
14 Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
I budeš se veseliti v slavnosti své, ty i syn tvůj i dcera tvá, služebník tvůj a služebnice tvá, Levíta i příchozí, sirotek i vdova, kteříž by byli v branách tvých.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Sedm dní svátek světiti budeš Hospodinu Bohu svému na místě, kteréž by vyvolil Hospodin, když požehná tobě Hospodin Bůh tvůj ve všech úrodách tvých, a ve všeliké práci rukou tvých, a tak budeš vesel.
16 Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
Třikrát v roce postaví se každý pohlaví mužského před Hospodinem Bohem tvým na místě, kteréž by vyvolil, na slavnost přesnic, na slavnost téhodnů a na slavnost stanů, a neukážeť se před Hospodinem prázdný;
17 Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Každý podlé daru sobě daného, vedlé požehnání Hospodina Boha tvého, jehož on udělil tobě.
18 Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
Soudce a správce ustanovíš sobě ve všech městech svých, kteráž Hospodin Bůh tvůj dá tobě v každém pokolení tvém, kteříž souditi budou lid soudem spravedlivým.
19 Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Neuchýlíš soudu, a nebudeš šetřiti osoby, aniž přijmeš daru; nebo dar oslepuje oči moudrých, a převrací slova spravedlivých.
20 Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Spravedlivě spravedlnosti následovati budeš, abys živ byl, a dědičně vládl zemí, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě.
21 Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
Nevysadíš sobě háje jakýmkoli dřívím u oltáře Hospodina Boha svého, kterýž uděláš sobě,
22 ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.
Ani vyzdvihneš sobě modly, což v ohavnosti má Hospodin Bůh tvůj.