< Deuteronomo 15 >
1 Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
De sept en sept ans tu célébreras [l'année de] relâche.
2 Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
Et c'est ici la manière [de célébrer l'année] de relâche. Que tout homme ayant droit d'exiger quelque chose que ce soit, qu'il puisse exiger de son prochain, donnera relâche, et ne l'exigera point de son prochain ni de son frère, quand on aura proclamé le relâche, en l'honneur de l'Eternel.
3 Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
Tu pourras exiger de l'étranger; mais quand tu auras à faire avec ton frère, tu lui donneras du relâche;
4 Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
Afin qu'il n'y ait au milieu de toi aucun pauvre; car l'Eternel te bénira certainement au pays que l'Eternel ton Dieu te donne en héritage pour le posséder.
5 Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
[Pourvu] seulement que tu obéisses à la voix de l'Eternel ton Dieu, et que tu prennes garde à faire ces commandements que je te prescris aujourd'hui.
6 Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
Parce que l'Eternel ton Dieu t'aura béni comme il t'en a parlé, tu prêteras sur gages à plusieurs nations, et tu n'emprunteras point sur gages. Tu domineras sur plusieurs nations, et elles ne domineront point sur toi.
7 Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
Quand un de tes frères sera pauvre au milieu de toi, en quelque lieu de ta demeure, dans le pays que l'Eternel ton Dieu te donne, tu n'endurciras point ton cœur, et tu ne resserreras point ta main à ton frère, qui sera pauvre.
8 Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
Mais tu ne manqueras pas de lui ouvrir ta main, et de lui prêter sur gages, autant qu'il en aura besoin pour son indigence, dans laquelle il se trouvera.
9 Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
Prends garde à toi, que tu n'aies dans on cœur quelque méchante intention, et [que] tu ne dises: La septième année, qui est l'année de relâche, approche; et que ton œil étant malin contre ton frère pauvre, afin de ne lui rien donner, il ne crie à l'Eternel contre toi, et qu'il n'y ait du péché en toi.
10 Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
Tu ne manqueras point de lui donner, et ton cœur ne lui donnera point à regret; car à cause de cela l'Eternel ton Dieu te bénira dans toute ton œuvre, et dans tout ce à quoi tu mettras la main.
11 Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
Car il ne manquera pas de pauvres au pays; c'est pourquoi je te commande, en disant: Ne manque point d'ouvrir ta main à ton frère, [savoir], à l'affligé, et au pauvre de ton peuple en ton pays.
12 Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
Quand quelqu'un d'entre tes frères, soit Hébreu ou Hébreue, te sera vendu, il te servira six ans; mais en la septième année tu le renverras libre de chez toi.
13 Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
Et quand tu le renverras libre de chez toi, tu ne le renverras point vide.
14 Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Tu ne manqueras pas de le charger de quelque chose de ton troupeau, de ton aire, et de ta cuve; tu lui donneras de ce en quoi l'Eternel ton Dieu t'aura béni.
15 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
Et qu'il te souvienne que tu as été esclave au pays d'Egypte, et que l'Eternel ton Dieu t'en a racheté; et c'est pour cela que je te commande ceci aujourd'hui.
16 Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
Mais s'il arrive qu'il te dise: Que je ne sorte point de chez toi; parce qu'il t'aime, toi, et ta maison, et qu'il se trouve bien avec toi;
17 pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
Alors tu prendras une alêne, et tu lui perceras l'oreille contre la porte, et il sera ton serviteur à toujours, tu en feras de même à ta servante.
18 Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
Qu'il ne te soit point fâcheux de le renvoyer libre de chez toi, car il t'a servi six ans, qui est le double du salaire du mercenaire; et l'Eternel ton Dieu te bénira en tout ce que tu feras.
19 Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
Tu sanctifieras à l'Eternel ton Dieu tout premier-né mâle qui naîtra de ton gros ou menu bétail. Tu ne laboureras point avec le premier-né de ta vache; et tu ne tondras point le premier-né de tes brebis.
20 Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
Tu le mangeras, toi et ta famille, chaque année en la présence de l'Eternel ton Dieu, au lieu que l'Eternel aura choisi.
21 Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
Mais s'il a quelque défaut, [tellement qu'il soit] boiteux ou aveugle, ou qu'il ait quelque autre mauvais défaut, tu ne le sacrifieras point à l'Eternel ton Dieu;
22 Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
Mais tu le mangeras au lieu de ta demeure. Celui qui est souillé, et celui qui est net [en mangeront], comme [on mange] du daim, et du cerf.
23 Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.
Seulement tu n'en mangeras point le sang, [mais] tu le répandras sur la terre, comme de l'eau.