< Deuteronomo 15 >

1 Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
In the seuenthe yeer thou schalt make remyssioun,
2 Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
that schal be fillid bi this ordre. To whom ony thing is `dettid, ethir owid of his freend, ether neiybore, and brother, he schal not mowe axe, for it is the yeer of remyssioun of the Lord.
3 Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
Thou schalt axe of a pilgrym and comelyng; thou hast not power to axe of a citeseyn and neiybore;
4 Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
and outerli a nedi man and begger schal not be among you, that thi Lord God blesse thee, in the lond which he schal yyue to thee in to the possessioun.
5 Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
If netheles thou schalt here the vois of thi Lord God, and schalt kepe alle thingis whiche he comaundide, and whiche Y comaunde to dai to thee, he schal blesse thee, as he bihiyte.
6 Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
Thou schalt leene to many folkis, and thou schalt not take borewyng of ony man; thou schalt be lord of ful many naciouns, and no man schal be lord of thee.
7 Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
If oon of thi britheren that dwellen with ynne the yatis of thi citee, in the lond which thi Lord God schal yyue to thee, cometh to pouert, thou schalt not make hard thin herte, nether thou schalt `drawe to gydere the hond,
8 Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
but thou schalt opene it to the pore man, and thou schalt `yyue loone to which thou siest hym haue nede.
9 Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
Be thou war lest perauenture wickid thouyt crepe priueli to thee, and thou seie in thin herte, The seuenthe yeer of remyssioun neiyeth; and thou turne awey the iyen fro thi pore brother, and thou nyle yyue to hym the loone that he axith; lest he crie ayens thee to the Lord, and it be maad to thee in to synne.
10 Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
But thou schalt yyue to hym, and thou schalt `not do ony thing falsly in releuynge `hise nedis, that thi Lord God blesse thee in al tyme, and in alle thingis to whiche thou schalt sette to hond.
11 Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
Pore men schulen not faile in the lond of `thin habitacioun; therfor Y comaunde to thee, that thou opene the hond to thi brother nedi and pore, that lyuen with thee in the lond.
12 Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
Whanne thi brothir an Ebrew man, ethir an Ebrew womman, is seeld to thee, and hath serued thee sixe yeer, in the seuenthe yeer thou schalt delyuere hym fre.
13 Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
And thou schalt not suffre hym go awey voide, to whom thou hast yyue fredom;
14 Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
but thou schalt yyue lijflode in the weye, of flockis, and of cornfloor, and of thi pressour, in whiche thi Lord God hath blessid thee.
15 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
Haue thou mynde that also thou seruedist in the lond of Egipt, and thi Lord God delyurede thee, `ether made thee free, and therfor Y comaunde now to thee.
16 Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
Forsothe if `the seruaunt seith, Y nyle go out, for he loueth thee, and thin hows, and feelith that it is wel to hym at thee, thou schalt take `a nal,
17 pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
and thou schalt peerse his eere in the yate of thin hous, and he schal serue thee til in to the world, `that is til to the iubilee, ethir fiftithe yeer; also thou schalt do in lijk maner to the handmayde.
18 Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
Thou schalt not turne awei fro hem thin iyen, whanne thou schalt delyure hem fre, for bi the hire of an hirid man thei serueden thee bi sixe yeer; that thi Lord God blesse thee, in alle the werkis whiche thou doist.
19 Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
Of the first gendrid thingis that ben borun in thi droues, and scheep, what euer is of male kynde, thou schalt halewe to thi Lord God. Thou schalt not worche in the firste gendrid thing `of oxe, and thou schalt not clippe the firste gendrid thinges of scheep.
20 Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
Thou schalt ete tho bi alle yeeris in the siyt of thi Lord God, thou, and thin hows, in the place `which the Lord chees.
21 Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
Sotheli if it hath a wem, ethir is crokid, ethir is blynd, ethir is foul, ethir feble in ony part, it schal not be offrid to thi Lord God;
22 Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
but thou schalt ete it with ynne the yatis of thi citee, bothe a cleene man and vncleene schulen ete tho in lijk maner, as a capret and an hert.
23 Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.
Onely thou schalt kepe this, that thou ete not the blood of tho, but schede out as watir in to erthe.

< Deuteronomo 15 >