< Deuteronomo 15 >

1 Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
E giko mar higa mar abiriyo gope duto nyaka we.
2 Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
Ma e kaka onego time: Ngʼato ka ngʼato nyaka we gope ma ja-Israel wadgi nigo. Ok onego okaw chudo kuom ja-Israel kata wadgi nikech ndalo mar weyo gowi e nyim Jehova Nyasaye oselandi.
3 Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
Jopinje mamoko to unyalo nyiso mondo ochulu gope ma gin-go, to gowi moro amora ma ja-Israel wadu nigo to nyaka iwene.
4 Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
Kata kamano, ngʼat modhier ok onego bedi e dieru, nikech piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou kod jou mondo ukaw kaka girkeni obiro gwedho,
5 Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
mana ka urito chike duto mag Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kendo urito buchene duto ma amiyou kawuono.
6 Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
Kuom mano Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro gwedhou kaka osewacho, kendo ubiro olo ogendini mangʼeny mwandu to un ok unuol kuomgi. Ubiro bedo gi loch kuom pinje mamoko to un onge manobed kod loch kuomu.
7 Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
Ka nitie jachan e kind owete moa e mier mag piny ma Jehova Nyasaye nomiu, to kik ubed gi chuny mapek kata lep ma wuoyo marach ewi owadu modhierno.
8 Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
To beduru mangʼwon kendo uholgi gimoro amora magidwaro.
9 Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
Kata bedni higa mar abiriyo chiegni chopo to kik ubed gi ich lit mutamru olo owadu man-gi dwaro. Ka mano otimore, to owaduno nyalo mako bura e nyim Jehova Nyasaye mi ubed joketho.
10 Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
Chiwreuru gi chuny man thuolo, to ka utimo kamano to Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro gwedho tijeu duto kod gimoro amora ma udwaro timo.
11 Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
Joma ochando nobedie e pinyu ndalo duto. Kuom mano achikou mondo ubed gi chuny ma thuolo kuom oweteu, joma odhier kod joma ochando e pinyu.
12 Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
Ka ja-Hibrania wadu madichwo kata madhako ochiwore mondo ingʼiewe kendo otini kuom higni auchiel, to e higa mar abiriyo nyaka iweye obed thuolo.
13 Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
Kendo ka iweye mondo odhi ka en thuolo, to kik igole odhi gi lwete nono.
14 Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Kowe mabup gi chuny ma thuolo kimiye jamni, kar dino cham kod divai. Bedne mangʼwon kendo imiye kaluwore gi kaka Jehova Nyasaye ma Nyasachi osegwedhi.
15 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
Paruru nine un wasumbini e piny Misri to Jehova Nyasaye ma Nyasachu noresou. Mano emomiyo amiyou chikni kawuono.
16 Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
Ka jatichni owacho niya, “Ok adwar weyi,” nikech oheri kod jo-dalani duto kendo owinjo maber ka odak kodu,
17 pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
to kaw riwi kendo ituchgo ite kiteno e dhoot mondo koro obed misumbani nyaka chiengʼ tim kamano bende nyaka ne jatichni madhako.
18 Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
Kik bedni matek weyo misumbani thuolo nimar higni auchiel mosebedo oromo chudo nyadiriyo maromre kod ngʼatno ma biro tiyoni ndalo. Kitimo kamano to Jehova Nyasaye ma Nyasachi nogwedh gik moko duto mitimo.
19 Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
Keturu tenge ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu jamni duto machwo mokwong nywolo e kweth jambu. Kik uket rwedhi ma dhou okwongo nywolo e jok bende kik ungʼad yie rombu mokwong nywolo.
20 Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
E higa ka higa in kod joodi onego uchamgi e nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu kama en owuon noyier.
21 Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
Ka chiayo moro nigi songa, ongʼol kata en muofu kata ka en gi mbala moro amora to ok onego utim kode misango ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
22 Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
Onego uchame e miechu uwuon. Joma ok ler gi jomaler nyalo chame mana kaka gichamo mwanda kata nyakech.
23 Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.
Kik ucham remo, to pukgiuru piny mana ka pi.

< Deuteronomo 15 >