< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Lingabantwana beNkosi uNkulunkulu wenu. Kaliyikuzisika, lingenzi impabanga phakathi laphakathi kwamehlo enu ngenxa yabafileyo.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
Ngoba uyisizwe esingcwele eNkosini uNkulunkulu wakho; leNkosi ikukhethile ukuthi ube yisizwe esikhethekileyo kuyo, ngaphezu kwezizwe zonke ezisebusweni bomhlaba.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Ungadli loba yikuphi okunengekayo.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
Yilezi inyamazana elingazidla: Inkabi, imvu, lembuzi,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
indluzele, lomziki, lomziki olempondo ezilembaxambaxa, lembuzi yeganga, lomtshwayeli, lenkabi yeganga, legogo,
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
layo yonke inyamazana edabula isondo, edabula okudabukileyo kube zinklagu ezimbili, eyetshisayo phakathi kwezinyamazana; leyo lingayidla.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Kodwa lezi kaliyikuzidla kuzo ezetshisayo, lakuzo ezidabula isondo elidabukileyo: Ikamela lomvundla lembila, ngoba ziyetshisa kodwa kazidabulanga isondo; zingcolile kini.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
Lengulube, ngoba idabula isondo kodwa kayetshisi; ingcolile kini. Lingadli okwenyama yazo, lingathinti izidumbu zazo.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Lezi lingazidla kuzo zonke ezisemanzini: Zonke ezilempiko lamaxolo lingazidla.
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
Kodwa loba yikuphi okungelampiko lamaxolo lingakudli; kungcolile kini.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
Zonke inyoni ezihlambulukileyo lingazidla.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
Kodwa yilezi elingayikudla kuzo: Ukhozi lelinqe lengqungqulu edla inhlanzi,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
lomzwazwa, lohelwane, lelinqe ngohlobo lwalo,
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
lalo lonke iwabayi ngohlobo lwalo,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
lesikhova, lomandukulo, lenkanku, lokhozi ngohlobo lwalo,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
isikhova esincinyane, lesikhova esikhulu, lesikhova esimhlophe,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
lewunkwe, lelinqe elikhulu, letshayamanzi,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
lengabuzane, lehemu ngohlobo lwalo, lemvenduna, lolulwane.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
Lazo zonke izibungu ezilempiko zingcolile kini; kazingadliwa.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
Zonke izinyoni ezihlambulukileyo lingazidla.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Lingabokudla langcuba; ungayinika owemzini ophakathi kwamasango akho ukuthi ayidle, loba uyithengise kowezizwe; ngoba uyisizwe esingcwele eNkosini uNkulunkulu wakho. Ungapheki izinyane lembuzi ngochago lukanina.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Uzanikela ngoqotho okwetshumi kwesithelo sonke senhlanyelo yakho, insimu ekuthelayo iminyaka ngeminyaka.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
Njalo uzakudla phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho, endaweni ezayikhetha ukuthi ibeke ibizo layo khona, okwetshumi kwamabele akho, okwewayini lakho elitsha, lokwamafutha akho, lamazibulo enkomo zakho lawezimvu zakho, ukuze ufunde ukuyesaba iNkosi uNkulunkulu wakho insuku zonke.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
Uba-ke indlela inde kakhulu kuwe, uze wehluleke ukukuthwala, ngoba ikhatshana kakhulu lawe indawo iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha ukuthi ibeke ibizo layo khona, lapho iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusisile,
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
uzakuguqula-ke kube yimali, ubophele imali esandleni sakho, uye endaweni iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha,
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
uthenge ngaleyomali loba kuyini umphefumulo wakho okufisayo, izinkabi loba izimvu loba iwayini loba okunathwayo okulamandla, loba kuyini umphefumulo wakho okufisayo; udle khona phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho, uthabe wena lendlu yakho.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
LomLevi ophakathi kwamasango akho, ungamdeli, ngoba kalasabelo lelifa kanye lawe.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
Ekupheleni kweminyaka emithathu uzakhupha konke okwetshumi kwezithelo zakho ngalowomnyaka, ukugcine phakathi kwamasango akho.
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
LomLevi, lokhu engelasabelo lelifa kanye lawe, lowemzini, lentandane, lomfelokazi, abaphakathi kwamasango akho, bazakuza, badle, basuthe, ukuze iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusise emsebenzini wonke wesandla sakho owenzayo.

< Deuteronomo 14 >