< Deuteronomo 14 >
1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
“Lingabantwana bakaThixo uNkulunkulu wenu. Lingabozisika loba liphuce amakhanda enu lizilela abafileyo,
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
ngoba lingabantu abangcwele kuThixo uNkulunkulu wenu. Ebantwini bonke abasemhlabeni, uThixo ulikhethile lina ukuthi libe ngabantu bakhe abaligugu.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Lingadli loba kuyini okunengisayo.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
Nanzi izinyamazana elingazidla: inkomo, imvu, imbuzi,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
umziki, impala, umziki obomvu, imbuzi yeganga, imbuzi mawa, umtshwayeli lemvu yentaba.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Lingadla zonke izinyamazana ezilenklagu ezivulekileyo lezentshisayo.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Kodwa-ke kulezo ezilenklagu ezivulekileyo loba lezo ezentshisayo zilani lingadli ikamela, umvundla loba imbila. Zingcolile kini ngokomkhuba.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
Ingulube layo ayihlanzekanga; lanxa ilenklagu ezivulekileyo kayentshisi. Lingabokudla inyama yazo, lingathinti lezidumbu zazo.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Kuzozonke izidalwa ezihlala emanzini, lingadla zonke lezo ezilempiko lamaxolo.
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
Kodwa konke lokho okungelampiko lamaxolo akumelanga likudle; kungcolile kini.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
Lingadla loba yiphi inyoni ehlanzekileyo.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
Kodwa lezi lingazidli: ukhozi, ilinqe elimnyama,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
uhelwane olubomvu, uhelwane olumnyama, loba yiwuphi umhlobo womzwazwa
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
loba yiphi imihlobo yamawabayi,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
isikhova esilesicholo, ingabuzane, idada lolwandle, loba wuphi umhlobo wokhozi,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
umandukulo, isikhova esikhulu, isikhova esimhlophe,
isikhova senkangala, ukhozi lwenhlanzi, itshayamanzi,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
ingabuzane, lawuphi umhlobo welanda, imvenduna lomalulwane.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
Zonke izibungu eziphaphayo zingcolile kini; lingabozidla.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
Kodwa konke okulempiko okuhlanzekileyo kudleni.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Lingabokudla ingcuba. Lingakunika loba ngubani owezizweni ohlezi loba kukuliphi phakathi kwamadolobho enu, yena angakudla, ulakho njalo ukuthi angathengisela omunye laye owezizweni. Kodwa lina lingabantu abangcwele kuThixo uNkulunkulu wenu. Lingapheki izinyane lembuzi ngochago lukanina.”
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
“Wobani leqiniso ukuthi libeka eceleni lokhu okuyingxenye eyodwa yetshumi yesivuno somnyaka.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
Dlanini okwetshumi kwamabele enu, iwayini elitsha lamafutha, kanye lamazibulo emihlambi yenkomo zenu lawezimvu emehlweni kaThixo uNkulunkulu wenu endaweni azalikhethela yona ukuba ibe leBizo lakhe, ukuze lifunde ukumphakamisa uThixo uNkulunkulu wenu ngezikhathi zonke.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
Kodwa nxa leyondawo ikhatshana kakhulu lina libusisiwe nguThixo uNkulunkulu wenu njalo lingenelisi ukuthwala okwetshumi kwenu (ngenxa yokuthi lapho uThixo akhethe ukubeka khona iBizo lakhe kukhatshana kakhulu),
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
thengisani okwetshumi kwenu ngesiliva, libe selithatha lihambe lesiliva liye endaweni leyo ezabe ikhethwe nguThixo uNkulunkulu wenu.
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
Sebenzisani isiliva lithenge ngaso loba yini elifuna ukuyithenga: inkomo, izimvu, iwayini loba kuyini elikufunayo. Ngakho lina kanye labendlu yenu lizakudla khonapho phambi kukaThixo uNkulunkulu wenu njalo libe lokujabula.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
Njalo lingakhohlwa abaLevi abahlala emadolobheni enu, ngoba abalaso isabelo esingesabo njalo abaphiwanga ilifa.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
Ekupheleni kweminyaka emithathu, lethani okwetshumi kwesivuno salowomnyaka likugcine emadolobheni enu,
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
yikho kuzakuthi abaLevi (bona abangelasabelo loba ilifa elingelabo) kanye labezizweni, izintandane ezingelaboyise labafelokazi abahlala emadolobheni enu beze labo bazokudla basuthe, njalo kuze kuthi uThixo uNkulunkulu wenu alibusise kuyo yonke imisebenzi yezandla zenu.”