< Deuteronomo 14 >
1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Ye [are] the children of the LORD your God: ye shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for the dead.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
For thou [art] a holy people to the LORD thy God, and the LORD hath chosen thee to be a peculiar people to himself, above all the nations that [are] upon the earth.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Thou shalt not eat any abominable thing.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
These [are] the beasts which ye shall eat: the ox, the sheep, and the goat,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
The hart, and the roebuck, and the fallow-deer, and the wild-goat, and the pygarg, and the wild ox, and the chamois.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
And every beast that parteth the hoof, and cleaveth the cleft into two claws, [and] cheweth the cud among the beasts, that ye shall eat.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Nevertheless, these ye shall not eat, of them that chew the cud, or of them that divide the cloven hoof; the camel, and the hare, and the coney: for they chew the cud, but divide not the hoof; [therefore] they [are] unclean to you.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
And the swine, because it divideth the hoof, yet cheweth not the cud, [is] unclean to you: ye shall not eat of their flesh, nor touch their dead carcass.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
These ye shall eat, of all that [are] in the waters: all that have fins and scales shall ye eat:
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
And whatever hath not fins and scales ye may not eat; it [is] unclean to you.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
[Of] all clean birds ye shall eat.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
But these [are they] of which ye shall not eat: the eagle, and the ossifrage, and the ospray,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
And the glede, and the kite, and the vultur after his kind,
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
And every raven after his kind,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
And the owl, and the night-hawk, and the cuckow, and the hawk after his kind,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
The little owl, and the great owl, and the swan,
And the pelican, and the gier-eagle, and the cormorant,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
And the stork, and the heron after her kind, and the lapwing, and the bat.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
And every creeping animal that flieth [is] unclean to you: they shall not be eaten.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
[But of] all clean fowls ye may eat.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Ye shall not eat [of] any thing that dieth of itself: thou shalt give it to the stranger that [is] in thy gates, that he may eat it; or thou mayest sell it to an alien: for thou [art] a holy people to the LORD thy God. Thou shalt not seethe a kid in his mother's milk.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Thou shalt truly tithe all the increase of thy seed, that the field bringeth forth year by year.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
And thou shalt eat before the LORD thy God, in the place which he shall choose to place his name there, the tithe of thy corn, of thy wine, and of thy oil, and the firstlings of thy herds and of thy flocks; that thou mayest learn to fear the LORD thy God always.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
And if the way is too long for thee, so that thou art not able to carry it; [or] if the place is too far from thee, which the LORD thy God shall choose to set his name there, when the LORD thy God hath blessed thee:
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Then shalt thou turn [it] into money, and bind up the money in thy hand, and shalt go to the place which the LORD thy God shall choose:
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
And thou shalt bestow that money for whatever thy soul desireth, for oxen, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatever thy soul desireth: and thou shalt eat there before the LORD thy God, and thou shalt rejoice, thou, and thy household.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
And the Levite that [is] within thy gates, thou shalt not forsake him; for he hath no part nor inheritance with thee.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
At the end of three years thou shalt bring forth all the tithe of thy increase the same year, and shalt lay [it] up within thy gates:
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
And the Levite, (because he hath no part nor inheritance with thee) and the stranger, and the fatherless, and the widow, who [are] within thy gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that the LORD thy God may bless thee in all the work of thy hand which thou doest.