< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Ye are sons of Jehovah your God: ye shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for a dead person.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
For thou art a holy people unto Jehovah thy God, and thee hath Jehovah chosen for a people of possession unto himself, out of all the peoples that are upon the face of the earth.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Thou shalt not eat any abominable thing.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
These are the beasts which ye shall eat: the ox, the sheep, and the goat;
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
the hart, and the gazelle, and the stag, and the wild goat, and the dishon and the oryx, and the wild sheep.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
And every beast that hath cloven hoofs, and the feet quite split open into double hoofs, [and] which cheweth the cud, among the beasts, that ye shall eat.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Only these ye shall not eat of those that chew the cud, or of those with hoofs cloven and split open: the camel, and the hare, and the rock-badger; for they chew the cud, but have not cloven hoofs — they shall be unclean unto you;
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
and the swine, for it hath cloven hoofs, yet cheweth not the cud — it shall be unclean unto you. Of their flesh shall ye not eat, and their carcase shall ye not touch.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
These shall ye eat of all that are in the waters: whatsoever hath fins and scales shall ye eat;
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
but whatsoever hath not fins and scales ye shall not eat: it shall be unclean unto you.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
All clean birds shall ye eat.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
But these are they of which ye shall not eat: the eagle, and the ossifrage, and the sea-eagle,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
and the falcon, and the kite, and the black kite after its kind;
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
and every raven after its kind;
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
and the female ostrich, and the male ostrich, and the sea-gull, and the hawk after its kind;
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
the owl, and the ibis and the swan,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
and the pelican, and the carrion vulture, and the gannet,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
and the stork, and the heron after its kind, and the hoopoe, and the bat.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
And every winged crawling thing shall be unclean unto you; they shall not be eaten.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
All clean fowls shall ye eat.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Ye shall eat of no carcase; thou shalt give it unto the stranger that is within thy gates, that he may eat it, or sell it unto a foreigner; for thou art a holy people to Jehovah thy God. Thou shalt not boil a kid in its mother's milk.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Thou shalt truly tithe all the increase of thy seed, the produce of the field, year by year.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
And thou shalt eat before Jehovah thy God, in the place which he will choose to cause his name to dwell there, the tithe of thy corn, of thy new wine, and of thine oil, and the firstlings of thy herds and of thy flocks; that thou mayest learn to fear Jehovah thy God continually.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
And if the way be too long for thee, so that thou art not able to carry it, because the place is too far from thee, which Jehovah thy God will choose to set his name there, when Jehovah thy God blesseth thee;
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
then shalt thou give it for money, and bind the money together in thy hand, and go to the place which Jehovah thy God will choose,
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
and thou shalt give the money for whatever thy soul desireth, for oxen, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatever thy soul asketh of thee; and thou shalt eat there before Jehovah thy God, and thou shalt rejoice, thou, and thy house.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
And thou shalt not forsake the Levite that is within thy gates; for he hath no portion nor inheritance with thee.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
At the end of three years thou shalt bring forth all the tithe of thine increase the same year, and shalt lay it up within thy gates;
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
and the Levite — for he hath no portion nor inheritance with thee — and the stranger, and the fatherless, and the widow, that are within thy gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that Jehovah thy God may bless thee in all the work of thy hand which thou doest.

< Deuteronomo 14 >