< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
You are the children of the Lord your God: you are not to make cuts on your bodies or take off the hair on your brows in honour of the dead;
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
For you are a holy people to the Lord your God, and the Lord has taken you to be his special people out of all the nations on the face of the earth.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
No disgusting thing may be your food.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
These are the beasts which you may have for food: the ox, the sheep, and the goat;
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
The hart, the gazelle, and the roe, the mountain goat and the pygarg and the antelope and the mountain sheep.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Any beast which has a division in the horn of its foot and whose food comes back into its mouth to be crushed again, may be used for food.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
But even among these, there are some which may not be used for food: such as the camel, the hare, and the coney, which are unclean to you, because, though their food comes back, the horn of their feet is not parted in two.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
And the pig is unclean to you, because though it has a division in the horn of its foot, its food does not come back; their flesh may not be used for food or their dead bodies touched by you.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
And of the things living in the waters, you may take all those who have wings for swimming with and skins formed of thin plates.
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
But any which have no skin-plates or wings for swimming, you may not take; they are unclean for you.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
All clean birds may be used for food.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
But these birds you may not take: the eagle and the gier-eagle and the ospray;
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
The falcon and the kite, and birds of that sort;
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
Every raven, and all birds of that sort;
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
And the ostrich and the night-hawk and the sea-hawk and birds of that sort;
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
The little owl and the great owl and the water-hen;
17 tsekwe, vuwo, dembo,
And the pelican and the vulture and the cormorant;
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
The stork and the heron and birds of that sort, and the hoopoe and the bat.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
Every winged thing which goes flat on the earth is unclean to you and may not be used as food.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
But all clean birds you may take.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
You may not have as food anything which has come to a natural death; the man from another country who is living with you may take it for food, or you may get a price for it from one of another nation; for you are a holy people to the Lord your God. The young goat is not to be cooked in its mother's milk.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Put on one side a tenth of all the increase of your seed, produced year by year.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
And make a feast before the Lord your God, in the place which is to be marked out, where his name will be for ever, of the tenth part of your grain and your wine and your oil, and the first births of your herds and your flocks; so that you may have the fear of the Lord your God in your hearts at all times.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
And if the way is so long that you are not able to take these things to the place marked out by the Lord your God for his name, when he has given you his blessing, because it is far away from you;
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Then let these things be exchanged for money, and, taking the money in your hand, go to the place marked out by the Lord your God for himself;
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
And with the money get whatever you have a desire for, oxen or sheep or wine or strong drink, whatever your soul's desire may be: and make a feast there before the Lord your God, and be glad, you and all your house;
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
And give a thought to the Levite who is living among you, for he has no part or heritage in the land.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
At the end of every three years take a tenth part of all your increase for that year, and put it in store inside your walls:
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
And the Levite, because he has no part or heritage in the land, and the man from a strange country, and the child who has no father, and the widow, who are living among you, will come and take food and have enough; and so the blessing of the Lord your God will be on you in everything you do.

< Deuteronomo 14 >