< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Ye are the children of Jehovah your God: ye shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for the dead.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
For thou art a holy people unto Jehovah thy God, and Jehovah hath chosen thee to be a people for his own possession, above all peoples that are upon the face of the earth.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Thou shalt not eat any abominable thing.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
These are the beasts which ye may eat: the ox, the sheep, and the goat,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
the hart, and the gazelle, and the roebuck, and the wild goat, and the pygarg, and the antelope, and the chamois.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
And every beast that parteth the hoof, and hath the hoof cloven in two, [and] cheweth the cud, among the beasts, that may ye eat.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Nevertheless these ye shall not eat of them that chew the cud, or of them that have the hoof cloven: the camel, and the hare, and the coney; because they chew the cud but part not the hoof, they are unclean unto you.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
And the swine, because he parteth the hoof but cheweth not the cud, he is unclean unto you: of their flesh ye shall not eat, and their carcasses ye shall not touch.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
These ye may eat of all that are in the waters: whatsoever hath fins and scales may ye eat;
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
and whatsoever hath not fins and scales ye shall not eat; it is unclean unto you.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
Of all clean birds ye may eat.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
But these are they of which ye shall not eat: the eagle, and the gier-eagle, and the ospray,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
and the glede, and the falcon, and the kite after its kind,
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
and every raven after its kind,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
and the ostrich, and the night-hawk, and the sea-mew, and the hawk after its kind,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
the little owl, and the great owl, and the horned owl,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
and the pelican, and the vulture, and the cormorant,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
and the stork, and the heron after its kind, and the hoopoe, and the bat.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
And all winged creeping things are unclean unto you: they shall not be eaten.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
Of all clean birds ye may eat.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Ye shall not eat of anything that dieth of itself: thou mayest give it unto the sojourner that is within thy gates, that he may eat it; or thou mayest sell it unto a foreigner: for thou art a holy people unto Jehovah thy God. Thou shalt not boil a kid in its mother’s milk.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Thou shalt surely tithe all the increase of thy seed, that which cometh forth from the field year by year.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
And thou shalt eat before Jehovah thy God, in the place which he shall choose, to cause his name to dwell there, the tithe of thy grain, of thy new wine, and of thine oil, and the firstlings of thy herd and of thy flock; that thou mayest learn to fear Jehovah thy God always.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
And if the way be too long for thee, so that thou art not able to carry it, because the place is too far from thee, which Jehovah thy God shall choose, to set his name there, when Jehovah thy God shall bless thee;
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
then shalt thou turn it into money, and bind up the money in thy hand, and shalt go unto the place which Jehovah thy God shall choose:
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
and thou shalt bestow the money for whatsoever thy soul desireth, for oxen, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatsoever thy soul asketh of thee; and thou shalt eat there before Jehovah thy God, and thou shalt rejoice, thou and thy household.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
And the Levite that is within thy gates, thou shalt not forsake him; for he hath no portion nor inheritance with thee.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
At the end of every three years thou shalt bring forth all the tithe of thine increase in the same year, and shalt lay it up within thy gates:
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
and the Levite, because he hath no portion nor inheritance with thee, and the sojourner, and the fatherless, and the widow, that are within thy gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that Jehovah thy God may bless thee in all the work of thy hand which thou doest.

< Deuteronomo 14 >