< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Synové jste Hospodina Boha vašeho, protož nebudete se řezati, aniž sobě uděláte lysiny mezi očima vašima nad mrtvým.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
Nebo lid svatý jsi Hospodinu Bohu svému, a tebe vyvolil Hospodin, abys jemu byl za lid zvláštní ze všech národů, kteříž jsou na tváři země.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Nebudeš jísti žádné věci ohavné.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
Tato jsou hovada, kteráž jísti budete: Voly, ovce a kozy,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
Jelena, dannele, srnu, kamsíka, jezevce, bůvola a losa.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Každé hovado, kteréž má kopyta rozdělená, tak aby rozdvojená byla, a přežívá mezi hovady, jísti je budete.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
A však ne všech přežívajících, aneb těch, kteráž kopyta rozdělená mají, budete jísti, jako velblouda, zajíce a králíka; nebo ač přežívají, však kopyta rozděleného nemají, nečistá jsou vám.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
Též svině, nebo rozdělené majíc kopyto, nepřežívá, nečistá vám bude; masa jejího jísti nebudete, a mrchy její se nedotknete.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Ze všech pak živočichů, kteříž u vodách jsou, tyto jísti budete: Cožkoli má plejtvy a šupiny, jísti budete.
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
Což pak nemá plejtví a šupin, toho jísti nebudete; nečisté vám bude.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
Všecko ptactvo čisté jísti budete.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
Těchto pak jísti nebudete: Orla, noha, orlice mořské,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
A sokola, supa a luňáka vedlé pokolení jeho,
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
A žádného krkavce vedlé pokolení jeho,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
Pstrosa, sovy, vodní káně a krahulce vedlé pokolení jeho,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
Raroha, kalousa a labuti,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
Pelikána, porfiriána a křehaře,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
Čápa, volavky vedlé pokolení jejího, dedka a netopýře.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
A všeliký zeměplaz létající nečistý bude vám, nebudete ho jísti.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
Každého ptáka čistého jísti budete.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Žádné umrliny jísti nebudete; příchozímu, kterýž jest v branách tvých, dáš ji, a jísti ji bude, aneb prodáš cizozemci, nebo lid svatý jsi Hospodinu Bohu svému. Nebudeš vařiti kozelce v mléce matky jeho.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Ochotně dávati budeš desátky ze všech užitků semene svého, kteřížť by přišli s pole každého roku.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
A jísti budeš před Hospodinem Bohem svým, (na místě, kteréž by vyvolil, aby tam přebývalo jméno jeho, ) desátky z obilí, vína i oleje svého, a prvorozené z volů svých a drobného dobytka svého, abys se učil báti Hospodina Boha svého po všecky dny.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
Jestliže by pak daleká byla cesta, a nemohl bys donésti toho, proto že daleko jest od tebe to místo, kteréž by vyvolil Hospodin Bůh tvůj k přebývání tam jména svého, když požehná tobě Hospodin Bůh tvůj:
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Tedy zpeněžíš je, a svázané peníze vezma v ruku svou, půjdeš k místu, kteréž by vyvolil Hospodin Bůh tvůj,
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
A vynaložíš ty peníze na všecko, čehož žádá duše tvá, na voly, na ovce, na víno, aneb jiný nápoj silný, a na všecko, čehož by sobě žádala duše tvá, a jísti budeš tam před Hospodinem Bohem svým, a veseliti se budeš ty i dům tvůj.
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
Levíty pak, kterýž by v branách tvých bydlil, neopustíš, nebo nemá dílu a dědictví s tebou.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
Každého léta třetího oddělíš všecky desátky z užitků svých toho léta, a složíš je v branách svých.
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
I přijde Levíta, (nebo nemá dílu a dědictví s tebou, ) a host a sirotek i vdova, kteříž jsou v branách tvých, i budou jísti a nasytí se, aby požehnal tobě Hospodin Bůh tvůj při všelikém díle rukou tvých, kteréž bys dělal.

< Deuteronomo 14 >