< Deuteronomo 13 >
1 Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
S’il s’élève au milieu de toi un prophète, ou quelqu’un qui dise qu’il a vu un songe, qui prédise un signe ou un prodige,
2 chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
Qu’arrive ce qu’il a annoncé, et qu’il te dise: Allons, et suivons des dieux étrangers, que tu ne connais pas, et servons-les:
3 musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Tu n’écouteras point les paroles de ce prophète ou de ce songeur, parce que le Seigneur votre Dieu vous éprouve, afin qu’il soit démontré, si vous l’aimez ou non, en tout votre cœur et en toute votre âme.
4 Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
Ne suivez que le Seigneur votre Dieu, ne craignez que lui, ne gardez que ses commandements, et n’écoutez que sa voix; ne servez que lui, et ne vous attachez qu’à lui.
5 Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
Mais ce prophète ou cet inventeur de songes sera tué, parce qu’il a parlé pour vous détourner du Seigneur votre Dieu, qui vous a retirés de la terre d’Egypte, et vous a rachetés de la maison de servitude, pour te faire écarter de la voie que t’a prescrite le Seigneur ton Dieu: tu ôteras ainsi le mal du milieu de toi.
6 Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
Si ton frère, le fils de ta mère, ou ton fils ou ta fille, ou ta femme qui repose sur ton sein, ou ton ami, que tu aimes comme ton âme, veut te persuader, te disant en secret: Allons, et servons des dieux étrangers que tu n’as pas connus, ni toi ni tes pères,
7 milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
Les dieux de toutes les nations qui sont autour de vous, loin ou près, depuis le commencement jusqu’à la fin de la terre:
8 musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
N’aie point de déférence pour lui, ne l’écoute pas, et que ton œil ne le ménage point, en sorte que tu aies pitié de lui et que tu le caches;
9 Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
Mais tue-le aussitôt. Que ta main d’abord soit sur lui, et qu’ensuite tout le peuple y porte la main.
10 Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
Accablé de pierres, il périra, parce qu’il a voulu t’arracher au Seigneur ton Dieu, qui t’a retiré de la terre d’Egypte, de la maison de servitude;
11 Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
Afin que tout Israël entendant, craigne, et qu’à l’avenir, il ne fasse nullement rien de semblable à cela.
12 Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
Si dans une de tes villes que le Seigneur ton Dieu te donnera à habiter, tu entends quelques-uns disant:
13 kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
Des fils de Bélial sont sortis du milieu de toi, ils ont détourné les habitants de leur ville, et ont dit: Allons, et servons des dieux étrangers que vous ne connaissez pas:
14 mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
Fais des recherches avec sollicitude et un grand soin; la vérité de la chose bien examinée, si tu trouves, que ce qu’on dit est certain, et que cette abomination a été réellement commise,
15 muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
Tu frapperas aussitôt les habitants de cette ville du tranchant du glaive, et tu la détruiras, ainsi que tout ce qui est en elle, jusqu’aux animaux.
16 Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
De plus, tout ce qu’il y aura de meubles, tu le rassembleras au milieu de ses rues, et tu le brûleras avec la ville elle-même, de manière à ce que tu consumes tout en l’honneur du Seigneur ton Dieu, et que ce soit un monceau de ruines perpétuel: ainsi elle ne sera plus rebâtie,
17 Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
Et il ne s’attachera rien de cet anathème à ta main, afin que le Seigneur soit détourné de la colère de sa fureur, qu’il ait pitié de toi, et qu’il te multiplie, comme il a juré à tes pères,
18 chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.
Quand tu écouteras la voix du Seigneur ton Dieu, gardant tous ses préceptes que moi, je te prescris aujourd’hui, afin que tu fasses ce qui est agréable en la présence du Seigneur ton Dieu.