< Deuteronomo 13 >

1 Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
“Possibly there will be people among you who [say that they] are prophets. They may say that they are able to interpret the meaning of dreams or perform various kinds of miracles [DOU].
2 chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
They will say those things in order to induce/persuade you to worship gods that you have never known about before. But even if what they predict happens,
3 musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
do not pay attention to what they say. Yahweh our God will be testing you to find out if you love him with all your inner being.
4 Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
You must conduct your lives as Yahweh our God wants you to, and you must revere him, and do what he tells you to do [MTY], and worship only him, and (be faithful to/have a close relationship with) him.
5 Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
“But you must execute anyone who [falsely says that he] is a prophet, or someone who [falsely] says that he can interpret dreams, or who tells you to rebel against Yahweh our God, who rescued your ancestors from being slaves in Egypt. People like that are only wanting to cause you to stop conducting your lives as Yahweh has commanded you to do. Execute them, to get rid of this evil among you.
6 Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
It does not matter if even your brother or your daughter or your wife or some close/dear friend secretly urges you, saying ‘Let’s worship other gods. They are gods which you or your ancestors have never known about.
7 milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
Some of them may encourage you to worship gods that people-groups that live near you worship, or gods that groups who live far away worship.
8 musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
Do not [SYN] do what they suggest. Do not even listen to them. Do not even be merciful to them, and do not keep secret what they have done.
9 Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
Execute them! You [who are their relative] must be the first one to [throw stones at them to] kill them, and then let everyone else [MTY] throw stones at them, too.
10 Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
Kill such people by throwing stones at them, because they are trying to cause you to stop worshiping Yahweh our God, who rescued your ancestors from being slaves in Egypt.
11 Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
When they are executed, all the Israeli people will hear [what happened], and they will become afraid, and none of them will do such an evil thing again.
12 Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
“When you are living in one of the towns in the land that Yahweh our God is giving to you, you may hear
13 kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
that some worthless people there among you [IDM] are deceiving the people of their town, saying, ‘Let’s go and worship other gods,’ but they are gods that you have never heard about before.
14 mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
Investigate it thoroughly/carefully. If [you find out that] it is true that such a disgraceful thing has happened,
15 muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
kill all the people in that town. And kill all their livestock, too. Destroy the town completely.
16 Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
Gather all the possessions that belonged to the people who lived there and pile them up in the city plaza. Then burn the town and everything in it, as though it were an offering to Yahweh that would be completely burned [on the altar]. The ruins/ashes must stay there forever; the town must never be rebuilt.
17 Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
None of you Israelis must take for yourselves [IDM] anything that Yahweh has said must be destroyed. But if you do what I say, Yahweh will stop being angry with you, and he will act mercifully toward you. And he will cause you to have many children/descendants, which is what he promised our ancestors that he would do.
18 chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.
Yahweh our God will do all those things if you do what he is telling you to do, and if you obey all the commandments that I am giving to you today and do what Yahweh says is right [for you to do].”

< Deuteronomo 13 >