< Deuteronomo 11 >

1 Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
Therefore you shall love the LORD your God, and keep his instructions, and his statutes, and his ordinances, and his commandments, always.
2 Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
Know this day: for I do not speak with your children who have not known, and who have not seen the chastisement of the LORD your God, his greatness, his mighty hand, and his outstretched arm,
3 zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
and his signs, and his works, which he did in the midst of Egypt to Pharaoh the king of Egypt, and to all his land;
4 zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
and what he did to the army of Egypt, to their horses, and to their chariots; how he made the water of the Red Sea to overflow them as they pursued after you, and how the LORD has destroyed them to this day;
5 Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
and what he did to you in the wilderness, until you came to this place;
6 ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
and what he did to Dathan and Abiram, the sons of Eliab, the son of Reuben; how the earth opened its mouth, and swallowed them up, and their households, and their tents, and every living thing that followed them, in the midst of all Israel:
7 Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
but your eyes have seen all the great work of the LORD which he did.
8 Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
Therefore you shall keep every commandment which I command you this day, that you may be strong, and multiply, and go in and possess the land, where you go over to possess it;
9 ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
and that you may prolong your days in the land, which the LORD swore to your fathers to give to them and to their descendants, a land flowing with milk and honey.
10 Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
For the land, where you go in to possess it, isn't as the land of Egypt, that you came out from, where you sowed your seed, and watered it with your feet, as a garden of herbs;
11 Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
but the land, where you go over to possess it, is a land of hills and valleys which drinks water of the rain of the sky,
12 Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
a land which the LORD your God cares for: the eyes of the LORD your God are always on it, from the beginning of the year even to the end of the year.
13 Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
It shall happen, if you shall listen diligently to my commandments which I command you this day, to love the LORD your God, and to serve him with all your heart and with all your soul,
14 pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
that I will give the rain of your land in its season, the former rain and the latter rain, that you may gather in your grain, and your new wine, and your oil.
15 Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
I will give grass in your fields for your livestock, and you shall eat and be full.
16 Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
Be careful, lest your heart be deceived, and you turn aside, and serve other gods, and worship them;
17 Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
and the anger of the LORD be kindled against you, and he shut up the sky, so that there shall be no rain, and the land shall not yield its fruit; and you perish quickly from off the good land which the LORD gives you.
18 Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
Therefore you shall lay up these my words in your heart and in your soul; and you shall bind them for a sign on your hand, and they shall be for symbols between your eyes.
19 Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
You shall teach them your children, talking of them, when you sit in your house, and when you walk by the way, and when you lie down, and when you rise up.
20 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
You shall write them on the door posts of your house, and on your gates;
21 kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
that your days may be multiplied, and the days of your children, in the land which the LORD swore to your fathers to give them, as the days of the heavens above the earth.
22 Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
For if you shall diligently keep all this commandment which I command you to do, to love the LORD your God, to walk in all his ways, and to cling to him;
23 Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
then will the LORD drive out all these nations from before you, and you shall dispossess nations greater and mightier than yourselves.
24 Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
Every place whereon the sole of your foot shall tread shall be yours: from the wilderness, and Lebanon, from the river, the river Perath, even to the western sea shall be your border.
25 Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
No man shall be able to stand before you: the LORD your God shall lay the fear of you and the dread of you on all the land that you shall tread on, as he has spoken to you.
26 Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
Look, I set before you this day a blessing and a curse:
27 dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
the blessing, if you shall listen to the commandments of the LORD your God, which I command you this day;
28 Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
and the curse, if you shall not listen to the commandments of the LORD your God, but turn aside out of the way which I command you this day, to go after other gods, which you have not known.
29 Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
It shall happen, when the LORD your God shall bring you into the land where you go to possess it, that you shall set the blessing on Mount Gerizim, and the curse on Mount Ebal.
30 Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
Aren't they beyond the Jordan, behind the way of the going down of the sun, in the land of the Canaanites who dwell in the Arabah, over against Gilgal, beside the oaks of Moreh?
31 Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
For you are to pass over the Jordan to go in to possess the land which the LORD your God gives you, and you shall possess it, and dwell in it.
32 mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.
You shall observe to do all the statutes and the ordinances which I set before you this day.

< Deuteronomo 11 >