< Deuteronomo 11 >

1 Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
“And so, love the Lord your God, and observe his precepts and ceremonies, his judgments and commandments, at all times.
2 Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
Acknowledge, on this day, the things that your sons did not know. For they did not see the chastisements of the Lord your God, his great acts, and powerful hand, and outstretched arm,
3 zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
the signs and works that he did in the midst of Egypt, to Pharaoh, the king, and to his entire land,
4 zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
and to the entire army of the Egyptians, and to their horses and chariots: how the waters of the Red Sea covered them as they were pursuing you, and how the Lord wiped them away, even to the present day;
5 Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
and the things that he accomplished for you in the wilderness, until you arrived at this place;
6 ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
and to Dathan and Abiram, sons of Eliab, who was the son of Reuben, those whom the earth, opening its mouth, engulfed with their households and tents, and with their entire substance which they had in the midst of Israel.
7 Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
Your eyes have seen all the great works of the Lord, which he has accomplished,
8 Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
so that you would keep all his commandments, which I entrust to you this day, and so that you would be able to enter and possess the land, toward which you are advancing,
9 ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
and so that you may live, for a long time, in the land which the Lord promised under oath to your fathers, and to their offspring, a land flowing with milk and honey.
10 Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
For the land, which you shall enter and possess, is not like the land of Egypt, from which you departed, where, when seed has been sown, waters are brought in by irrigation, in the manner of gardens.
11 Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
Rather, it has mountainous regions and plains, which lay waiting for rain from heaven.
12 Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
And the Lord your God always visits it, and his eyes are upon it, from the beginning of the year, all the way to its end.
13 Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
So then, if you obey my commandments, which I am instructing to you this day, so that you love the Lord your God, and serve him with your whole heart and your whole soul,
14 pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
he will give to your land the early rain and the late rain, so that you may gather your grain, and your wine, and your oil,
15 Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
and your hay from the fields in order to feed your cattle, and so that you yourselves may eat and be satisfied.
16 Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
Be careful, lest perhaps your heart may be deceived, and you might withdraw from the Lord, and serve strange gods, and adore them.
17 Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
And the Lord, becoming angry, might close up heaven, so that the rain would not descend, nor would the earth produce her seedlings, and then you would quickly perish from the excellent land, which the Lord will give to you.
18 Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
Place these words of mine in your hearts and minds, and hang them as a sign on your hands, and arrange them between your eyes.
19 Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
Teach your sons to meditate on them, when you sit in your house, and when you walk along the way, and when you lie down or rise up.
20 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
You shall write them upon the doorposts and the gates of your house,
21 kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
so that your days may be multiplied, and the days of your sons, in the land which the Lord swore to your fathers, that he would give it to them for as long as heaven is suspended above the earth.
22 Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
For if you keep the commandments which I am entrusting to you, and if you do them, so that you love the Lord your God, and walk in all his ways, clinging to him,
23 Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
the Lord will scatter all these nations before your face, and you shall possess them, though they are greater and stronger than you.
24 Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
Every place upon which your foot shall tread will be yours. From the desert, and from Lebanon, from the great river Euphrates, as far as the western sea, shall be your borders.
25 Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
No one will stand against you. The Lord your God will spread the terror and dread of you over all the land upon which you shall tread, just as he has spoken to you.
26 Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
Behold, I am setting forth in your sight today a blessing and a curse.
27 dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
It will be a blessing, if you obey the commandments of the Lord your God, which I am instructing to you this day.
28 Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
It will be a curse, if you do not obey the commandments of the Lord your God, but instead you withdraw from the way, which I am revealing to you now, and you walk after foreign gods that you have not known.
29 Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
Yet truly, when the Lord your God will have led you into the land, to which you are traveling for a habitation, you shall place the blessing upon Mount Gerizim, the curse upon Mount Ebal,
30 Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
which are across the Jordan, behind the way which slopes toward the setting of the sun, in the land of the Canaanite, who lives in the plains opposite Gilgal, which is near the valley extending toward and entering a distant place.
31 Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
For you shall cross over the Jordan, so that you may possess the land which the Lord your God will give you, so that you may have it and possess it.
32 mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.
Therefore, see to it that you fulfill the ceremonies and judgments, which I am placing in your sight this day.”

< Deuteronomo 11 >