< Deuteronomo 11 >
1 Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
Heruru Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo urit dwarone, buchene, kod chikene ndalo duto.
2 Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
Paruru kawuononi puonj mane uyudo kuom Jehova Nyasaye ma Nyasachu nimar kata obedo ni nyithindu pok ongʼeyo kata neno puonjno, to un to ungʼeye. Bende paruru duongʼ mar Jehova Nyasaye gi tekone kod bat morie;
3 zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
kaachiel gi ranyisi mane otimo kod honni mane onyiso e dier jo-Misri, ne Farao ruodh Misri kod pinye duto.
4 zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
Bende nuneno gima notimone jolwenj Misri, faresegi kod gechegi kane gilawou mi Nam Makwar oimogi kendo mi Jehova Nyasaye otiekogi pep.
5 Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
Nyithindu ne ok oneno gima Jehova Nyasaye notimonu e thim nyaka ne uchopo kama untiereni.
6 ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
Kendo gima ne otimone Dathan kod Abiram yawuot Eliab mawuok e dhood Reuben kane piny oyawo dhoge e dieru tir e kind jo-Israel duto ma omwonyogi duto kod joutgi, hembegi kod gik moko duto ma mekgi.
7 Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
To un ema ne uneno giwengeu gik madongo duto mane Jehova Nyasaye otimo.
8 Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
Rituru chike duto ma amiyou kawuononi mondo ubed gi teko kendo ukaw piny man loka mar Jordan mudhi kawono;
9 ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
kendo mondo udagi amingʼa e piny mane Jehova Nyasaye osingo ne kwereu ni nomigi kod nyikwagi ma en piny maber mopongʼ gi chak kod mor kich.
10 Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
Piny ma udonjoe mondo ukaw ok chal gi piny Misri muwuokie, ma en kama nuchwoyoe kothe ka uolonegi pi mana kaka iolone puoth alot.
11 Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
To piny ma ungʼado Jordan mondo udhi ukaw en piny gode kod holo ma mwonyo pi moa e polo.
12 Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
En piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro ritoue; kendo orange pile ka pile higa ngima.
13 Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
Koro ka urito chike mamiyou adimba kawuono, ka uhero Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo tiyone gi chunyu duto kod ngimau duto,
14 pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
to abiro oro koth e pinyu e ndalo mowinjore e ndalo oro kod ndalo chwiri, mondo uyud cham, gi mzabibu kod mo.
15 Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
Abiro chiwo lum ne jamni mau kendo unuchiem ma uyiengʼ.
16 Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
Beduru motangʼ mondo pachu kik maki gi gik ma kamago ma ulam nyiseche mamoko ka ukulorenegi.
17 Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
Mirimb Nyasaye nyalo lwar kuomu, ma olor ranga polo, mi koth bed maonge kendo puothe ok nochieg cham, ma uduto utho e piny maber ma Jehova Nyasaye miyou.
18 Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
Kanuru wechenagi e chunyu kod pachu, twegiuru e bedeu ka ranyisi kendo e pat wengeu.
19 Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
Puonjuru nyithindu wechegi, ka uwuoyo kuomgi ka ubet e dala, ka uwuotho e yo, ka unindo kata ka uchiewo.
20 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
Ndikgiuru ewi dhoutu kendo e rangeyeu,
21 kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
mondo ndalo magu kod mag nyithindu omedre e piny mane Jehova Nyasaye osingore ni nomi nyithindu, mondo obed maru nyaka chiengʼ.
22 Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
Ka urito adimba chike duto ma amiyou mondo uluw mi uhero Jehova Nyasaye ma Nyasachu ka uwuotho e yorene kendo ka urito wechene,
23 Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
to Jehova Nyasaye biro riembo ogendinigi duto e nyimu, kendo ubiro kawo pinje madongo kendo maroteke moloyou.
24 Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
Kamoro amora ma unyono, nobed maru, tongʼ maru noyarre koa e thim mar Lebanon kokalo Aora mar Yufrate nyaka nam man yo podho chiengʼ.
25 Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
Onge ngʼama nosiru. Jehova Nyasaye ma Nyasachu mana kaka osechikou, biro kelo luoro kod kibaji e piny duto kamoro amora ma udhiyoe.
26 Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
Winjuru, kawuononi aketo gweth kod kwongʼ e nyimu.
27 dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
Ka urito chike Jehova Nyasaye ma Nyasachu ma amiyou kawuononi, to unuyud gweth.
28 Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
Ka ok uluwo chike Jehova Nyasaye ma Nyasachu mi ulokoru uweyo yore ma amiyou kawuono, kendo ka uluwo nyiseche mamoko ma ok usengʼeyo, to unuyud kwongʼ.
29 Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
Ka Jehova Nyasaye ma Nyasachu osekelou e piny mudhiye mondo ukaw obed maru, to nyaka uhul weche gweth e got Gerizim, to weche mag kwongʼ to uhul e got Ebal.
30 Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
Kaka ungʼeyo, godegi ni yo podho chiengʼ mar holo mar Jordan kama jo-Kanaan odakie. Gin gode mantiere Araba but Gilgal kama yiende madongo mag More nitie.
31 Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
Uchiegni ngʼado Jordan mondo ukaw piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou. Ka usekawe ma udakie,
32 mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.
to neuru ni uluwo chike duto kod buche ma amiyou kawuononi.