< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
Прве године Дарија, сина Асвировог од племена мидског, који се зацари над царством халдејским,
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
Прве године његовог царовања ја Данило разумех из књига број година, које беше рекао Господ Јеремији пророку да ће се навршити развалинама јерусалимским, седамдесет година.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
И окретох лице своје ка Господу Богу тражећи Га молитвом и молбама с постом и с кострети и пепелом.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
И помолих се Господу Богу свом и исповедајући се рекох: О Господе, Боже велики и страшни, који држиш завет и милост онима који Те љубе и држе заповести Твоје;
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
Згрешисмо и зло чинисмо и бисмо безбожни, и одметнусмо се и одступисмо од заповести Твојих и од закона Твојих.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
И не слушасмо слуга Твојих пророка, који говораху у Твоје име царевима нашим, кнезовима нашим и очевима нашим и свему народу земаљском.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
У Тебе је, Господе, правда, а у нас срам на лицу, како је данас, у Јудејаца и у Јерусалимљана и у свих Израиљаца, који су близу и који су далеко по свим земљама куда си их разагнао за грехе њихове, којима Ти грешише.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Господе, у нас је срам на лицу, у царева наших, у кнезова наших и у отаца наших, јер Ти згрешисмо.
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
У Господа је Бога нашег милост и праштање, јер се одметнусмо од Њега,
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
И не слушасмо глас Господа Бога свог да ходимо по законима Његовим, које нам је дао преко слуга својих пророка.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
И сав Израиљ преступи закон Твој, и одступи да не слуша глас Твој; зато се изли на нас проклетство и заклетва написана у закону Мојсија, слуге Божијег, јер Му згрешисмо.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
И Он потврди речи своје које је говорио за нас и за судије наше, које су нам судиле, пустивши на нас зло велико, да тако не би под свим небом како би у Јерусалиму.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Како је писано у закону Мојсијевом, све то зло дође на нас, и опет се не молисмо Господу Богу свом да бисмо се вратили од безакоња свог и пазили на истину Твоју.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
И Господ наста око зла и наведе га на нас; јер је праведан Господ Бог наш у свим делима својим која чини, јер не слушасмо глас Његов.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
Али сада, Господе Боже наш, који си извео народ свој из земље мисирске руком крепком, и стекао си себи име, како је данас, згрешисмо, безбожни бисмо.
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
Господе, по свој правди Твојој нека се одврати гнев Твој и јарост Твоја од града Твог Јерусалима, свете горе Твоје; јер са греха наших и с безакоња отаца наших Јерусалим и Твој народ поста руг у свих који су око нас.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
Сада дакле послушај, Боже наш, молитву слуге свог и молбе његове, и обасјај лицем својим опустелу светињу своју, Господа ради.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Боже мој, пригни ухо своје, и чуј; отвори очи своје, и види пустош нашу и град, на који је призвано име Твоје, јер не ради своје правде него ради милости Твоје падамо пред Тобом молећи се.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Господе услиши, Господе опрости, Господе пази и учини, не часи себе ради Боже мој, јер је Твоје име призвано на овај град и на Твој народ.
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
А док ја још говорах и мољах се и исповедах грех свој и грех народа свог Израиља, и падах молећи се пред Господом Богом својим за свету гору Бога свог,
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
Док још говорах молећи се, онај човек Гаврило, ког видех пре у утвари, долете брзо и дотаче ме се о вечерњој жртви.
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
И научи ме и говори са мном и рече: Данило, сада изиђох да те уразумим.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
У почетку молитве твоје изиђе реч, и ја дођох да ти кажем, јер си мио; зато слушај реч, и разуми утвару.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Седамдесет је недеља одређено твом народу и твом граду светом да се сврши преступ и да нестане греха и да се очисти безакоње и да се доведе вечна правда, и да се запечати утвара и пророштво, и да се помаже Свети над светима.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
Зато знај и разуми: Откада изиђе реч да се Јерусалим опет сазида до помазаника војводе биће седам недеља, и шездесет и две недеље да се опет пограде улице и зидови, и то у тешко време.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
А после те шездесет и две недеље погубљен ће бити помазаник и ништа му неће остати; народ ће војводин доћи и разорити град и светињу; и крај ће му бити с потопом, и одређено ће пустошење бити до свршетка рата.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
И утврдиће завет с многима за недељу дана, а у половину недеље укинуће жртву и принос; и крилима мрским, која пустоше, до свршетка одређеног излиће се на пустош.

< Danieli 9 >