< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
In year one of Darius [the] son of Ahasuerus one of [the] descendant[s] of Media who he had been made king over [the] kingdom of [the] Chaldeans.
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
In year one of reigning his I Daniel I observed in the scrolls [the] number of the years which it came [the] word of Yahweh to Jeremiah the prophet to complete to [the] ruins of Jerusalem seventy year[s].
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
And I set! face my to [the] Lord God to seek prayer and supplications with fasting and sackcloth and ash[es].
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
And I prayed! to Yahweh God my and I confessed and I said! I beg you O Lord God great and awesome [who] keeps the covenant and covenant loyalty to [those who] love him and to [those who] keep commandments his.
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
We have sinned and we have committed iniquity (we have acted wickedly *Q(K)*) and we have rebelled and we have turned aside from commandments your and from judgments your.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
And not we have listened to servants your the prophets who they spoke in name your to kings our leaders our and ancestors our and to all [the] people of the land.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
[belongs] to You O Lord righteousness and [belongs] to us [the] shame of the faces as the day this to everyone of Judah and to [the] inhabitants of Jerusalem and to all Israel near and far in all the lands where you have banished them there in unfaithfulness their which they acted unfaithfully against you.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
O Yahweh [belongs] to us [the] shame of the faces to kings our to leaders our and to ancestors our that we have sinned to you.
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
[belong] to [the] Lord God our compassion and forgiveness for we have rebelled against him.
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
And not we have listened to [the] voice of Yahweh God our to walk in laws his which he set before us by [the] hand of servants his the prophets.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
And all Israel they have transgressed law your and they have turned aside to not to listen to voice your and it has poured forth on us the curse and the oath which [was] written in [the] law of Moses [the] servant of God for we have sinned to him.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
And he has carried out (word his *Q(K)*) which he spoke on us and on judges our who they judged us by bringing on us a calamity great which not it has been done under all the heavens just as it has been done on Jerusalem.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Just as [it is] written in [the] law of Moses all the calamity this it has come on us and not we have entreated [the] face of - Yahweh God our by turning away from iniquity our and by giving attention to faithfulness your.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
And he kept watch Yahweh over the calamity and he brought it on us for [has been] righteous Yahweh God our on all deeds his which he has done and not we listened to voice his.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
And now - O Lord God our who you brought out people your from [the] land of Egypt by a hand strong and you made for yourself a name as the day this we have sinned we have acted wickedly.
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
O Lord according to all righteousness your may it turn back please anger your and rage your from city your Jerusalem [the] mountain of holiness your for by sins our and by [the] iniquities of ancestors our Jerusalem and people your [have become] a reproach to all around us.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
And therefore - listen O God our to [the] prayer of servant your and to supplications his and make shine face your on sanctuary your desolate for [the] sake of [the] Lord.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Incline O God my - ear your and listen (open *Q(K)*) eyes your and see desolate [things] our and the city which it is called name your on it for - not on righteousness our we [are] making fall supplications our before you for on compassion your great.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
O Lord - hear! O Lord - forgive! O Lord be attentive! and act may not you delay for own sake your O God my for name your it is called on city your and on people your.
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
And still I [was] speaking and [was] praying and [was] confessing sin my and [the] sin of people my Israel and [was] making fall supplication my before Yahweh God my on [the] mountain of [the] holiness of God my.
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
And still I [was] speaking in prayer and the man Gabriel whom I had seen in the vision at the beginning wearied with weariness [was] approaching me about [the] time of [the] offering of [the] evening.
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
And he gave understanding and he spoke with me and he said O Daniel now I have come forth to give insight you understanding.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
At [the] beginning of supplications your it went forth a word and I I have come to declare for [are] precious you and understand the word and understand the vision.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Sevens seventy it has been decreed on people your - and on [the] city of holiness your to put an end to the transgression (and to complete sin *Q(K)*) and to atone for iniquity and to bring righteousness of perpetuity and to seal up vision and prophet and to anoint a holy place of holy places.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
So you may know and you will understand from [the] going forth of [the] word to restore and to rebuild Jerusalem until an anointed [one] a prince sevens seven and sevens sixty and two it will return and it will be built an open place and a moat and in [the] distress of the times.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
And after the sevens sixty and two he will be cut off an anointed [one] and nothing [will belong] to him and the city and the sanctuary it will destroy [the] people of a prince who is coming and end his [will be] by flood and [will be] until [the] end war [are] determined desolate [things].
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
And he will make strong a covenant to the many [people] seven one and [the] middle of the seven he will cause to cease - sacrifice and offering and on a wing of abomination desolating and until complete destruction and [what] has been decided it will be poured forth on [one who] is desolate.

< Danieli 9 >