< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
I Darius, Ahasveruses søns første regeringsår, han som var af medisk Byrd og var blevet Konge over kaldæernes Rige,
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
i hans første Regeringsår lagde jeg, Daniel, i Skrifterne Mærke til det Åremål, i hvilket Jerusalem efter HERRENs Ord til Profeten Jeremias skulde ligge i Grus, halvfjerdsindstyve År.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
Jeg vendte mit Ansigt til Gud Herren for at fremføre Bøn og Begæring under Faste i Sæk og Aske.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
Og jeg bad til HERREN min Gud, bekendte og sagde: "Ak, Herre, du store, forfærdelige Gud, som holder fast ved Pagten og Miskundheden mod dem, der elsker dig og holder dine Bud!
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
Vi har syndet og handlet ilde, været gudløse og genstridige; vi veg fra dine Bud og Vedtægter
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
og hørte ikke på dine Tjenere Profeterne, som talte i dit Navn til vore Konger, Fyrster og Fædre og til alt Folket i Landet.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
Du står med Retten, Herre, vi med vort Ansigts Blusel, som det nu viser sig, vi Judas Mænd, Jerusalems Borgere, ja alt Israel fjernt og nær i alle Lande, hvor du drev dem hen for deres Troløshed imod dig.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Herre, vi står med vort Ansigts Blusel, vore Konger, Fyrster og Fædre, fordi vi syndede imod dig.
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
Men hos Herren vor Gud er Barmhjertighed og Tilgivelse, thi vi stod ham imod
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
og adlød ikke HERREN vor Guds Røst, så vi fulgte hans Love, som han forelagde os ved sine Tjenere Profeterne.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
Nej, hele Israel overtrådte din Lov og faldt fra, ulydige mod din Røst; så udøste den svorne Forbandelse, som står skrevet i Guds Tjener Mosess Lov, sig over os, thi vi syndede imod ham;
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
og han fuldbyrdede de Ord, han havde talet imod os og de Herskere, som herskede over os, så han bragte en Ulykke over os så stor, at der ingensteds under Himmelen er sket Mage til den Ulykke, som ramte Jerusalem.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Som skrevet står i Mose Lov, kom hele denne Ulykke over os; og vi stemte ikke HERREN vor Gud til Mildhed ved at vende om fra vore Misgerninger og vinde Indsigt i din Sandhed.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
Derfor var HERREN årvågen over Ulykken og bragte den over os; thi HERREN vor Gud er retfærdig mod alle Skabninger, som han har skabt, og vi adlød ikke hans Røst.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
Og nu, Herre vor Gud, du, som med stærk Hånd førte dit Folk ud af Ægypten og vandt dig et Navn, som er det samme den Dag i Dag: Vi syndede og var gudløse!
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
Herre, lad dog efter alle dine Retfærdshandlinger din Vrede og Harme vende sig fra din By Jerusalem, dit hellige Bjerg; thi ved vore Synder og vore Fædres Misgerninger er Jerusalem og dit Folk blevet til Spot for alle vore Naboer.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
Så lyt da nu, vor Gud, til din Tjeners Bøn og Begæring og lad dit Ansigt lyse over din ødelagte Helligdom for din egen Skyld, o Herre!
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Bøj dit Øre, min Gud, og hør, oplad dine Øjne og se Ødelæggelsen, som er overgået os, og Byen, dit Navn er nævnet over; thi ikke i Tillid til vore Retfærdshandlinger fremfører vi vor Begæring for dit Åsyn, men i Tillid til din store Barmhjertighed.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Herre, hør! Herre, tilgiv! Herre, lån Øre og grib uden Tøven ind for din egen Skyld, min Gud; thi dit Navn er nævnet over din By og dit Folk!"
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
Medens jeg endnu talte således, bad og bekendte min og mit Folk Israels Synd og for HERREN min Guds Åsyn fremførte min Forbøn for min Guds hellige Bjerg,
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
medens jeg endnu bad, kom Manden Gabriel, som jeg tidligere havde set i Synet, hastigt flyvende nær hen til mig ved Aftenofferets Tid;
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
og da han var kommet, talede han således til mig: "Daniel, jeg er nu kommet for at give dig Indsigt.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
Straks du begyndte at bede, udgik et Ord, og jeg er kommet for at kundgøre dig det; thi du er højt elsket; så mærk dig Ordet og agt på Åbenbaringen!
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Halvfjerdsindstyve Uger er fastsat over dit Folk og din hellige By, indtil Overtrædelsen er fuldendt, Syndens Målfuldt, Misgerningen sonet, evig Retfærdighed hidført, Syn og Profet beseglet og en højhellig Helligdom salvet.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
Og du skal vide og forstå: Fra den Tid Ordet om Jerusalems Genrejsning og Opbyggelse udgik, indtil en Salvet, en Fyrste, kommer, er der syv Uger; og i to og tresindstyve Uger skal det genrejses og opbygges med Torve og Gader under Tidernes Trængsel.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
Men efter de to og tresindstyve Uger skal en Salvet bortryddes uden Dom, og Byen og Helligdommen skal ødelægges tillige med en Fyrste. Og Enden kommer med Oversvømmelse, og indtil Enden skal der være Krig, den fastsatte Ødelæggelse.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
Og pagten skal ophæves for de mange i een Uge, og i Ugens sidste Halvdel skal Slagtoffer og Afgrødeoffer ophøre, og Ødelæggelsens Vederstyggelighed skal sættes på det hellige Sted, indtil den fastsatte Undergang udøser sig over Ødelæggeren.

< Danieli 9 >