< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
Léta prvního Daria syna Asverova z semene Médského, kteréhož učiněn jest králem v království Kaldejském,
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
Léta prvního kralování jeho já Daniel porozuměl jsem z knih počtu let, o nichž se stalo slovo Hospodinovo k Jeremiášovi proroku, že se vyplní zpuštění Jeruzaléma sedmdesátého léta.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
A obrátil jsem tvář svou ku Pánu Bohu, hledaje ho modlitbou a pokornými prosbami, v postu, v žíni a popele.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
I modlil jsem se Hospodinu Bohu svému, a vyznávaje se, řekl jsem: Prosím, Pane Bože silný, veliký a všeliké cti hodný, ostříhající smlouvy a dobrotivosti k těm, kteříž tě milují, a ostříhají přikázaní tvých.
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
Zhřešiliť jsme a převráceně jsme činili, bezbožnost jsme páchali, a protivili jsme se, a odvrátili od přikázaní tvých a soudů tvých.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
Aniž jsme poslouchali služebníků tvých proroků, kteříž mluvívali ve jménu tvém králům našim, knížatům našim a otcům našim, i všemu lidu země.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
Toběť, ó Pane, přísluší spravedlnost, nám pak zahanbení tváři, jakž se to děje nyní mužům Judským a obyvatelům Jeruzalémským, a všechněm Izraelským, blízkým i dalekým, ve všech zemích, kamž jsi je zahnal pro přestoupení jejich, jímž přestupovali proti tobě.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Námť, ó Hospodine, sluší zahanbení tváři, králům našim, knížatům našim a otcům našim, neboť jsme zhřešili proti tobě,
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
Pánu Bohu pak našemu milosrdenství a slitování, poněvadž jsme se protivili jemu,
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
A neposlouchali jsme hlasu Hospodina Boha našeho, abychom chodili v naučeních jeho, kteréž předkládal před oči naše skrze služebníky své proroky.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
Nýbrž všickni Izraelští přestoupili zákon tvůj a odvrátili se, aby neposlouchali hlasu tvého; protož vylito jest na nás to prokletí a klatba, kteráž jest zapsána v zákoně Mojžíše služebníka Božího, nebo jsme zhřešili proti němu.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
Pročež splnil slovo své, kteréž mluvil proti nám a proti soudcům našim, kteříž nás soudili, a uvedl na nás toto zlé veliké, jehož se nestalo pode vším nebem, jakéž se stalo v Jeruzalémě.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Tak jakž zapsáno jest v zákoně Mojžíšově, všecko to zlé přišlo na nás, a však ani tak jsme se nekořili před tváří hněvivou Hospodina Boha našeho, abychom se odvrátili od nepravostí svých, a šetřili pravdy jeho.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
Protož neobmeškal Hospodin s tím zlým, ale uvedl je na nás; nebo spravedlivý jest Hospodin Bůh náš ve všech skutcích svých, kteréž činí, jehož hlasu poslušni jsme nebyli.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
Nyní však, ó Pane Bože náš, kterýž jsi vyvedl lid svůj z země Egyptské rukou silnou, a způsobils sobě jméno, jakéž jest dnešního dne, zhřešili jsme, bezbožně jsme činili.
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
Ó Pane, podlé vší tvé dobrotivosti nechť se, prosím, odvrátí hněv tvůj a prchlivost tvá od města tvého Jeruzaléma, hory svatosti tvé; nebo pro hříchy naše a pro nepravosti otců našich Jeruzalém a lid tvůj v pohanění jest u všech, kteříž jsou vůkol nás.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
Nyní tedy, ó Bože náš, vyslyš modlitbu služebníka svého, a pokorné prosby jeho, a zasvěť tvář svou nad svatyní svou spuštěnou, pro Pána.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Nakloň, Bože můj, ucha svého a slyš, otevři oči své a viz zpuštění naše i města, kteréž jest nazváno od jména tvého; nebo ne pro nějaké naše spravedlnosti padajíce, pokorně prosíme tebe, ale pro milosrdenství tvá mnohá.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Vyslyšiž, ó Pane, Pane, odpusť, Pane, pozoruj a učiň; neprodlévejž pro sebe samého, můj Bože, nebo od jména tvého nazváno jest město toto i lid tvůj.
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
Ještě jsem mluvil a modlil se, a vyznával hřích svůj i hřích lidu svého Izraelského, a padna, pokorně jsem se modlil před tváří Hospodina Boha svého, za horu svatosti Boha svého,
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
Ještě, pravím, mluvil jsem při modlitbě, a muž ten Gabriel, kteréhož jsem viděl v tom vidění na počátku, rychle přiletěv, dotekl se mne v čas oběti večerní.
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
A slouže mi k srozumění, mluvil se mnou a řekl: Danieli, nyní jsem vyšel, abych tě naučil vyrozumívati tajemstvím.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
Při počátku pokorných proseb tvých vyšlo slovo, a já jsem přišel, aťbych je oznámil, nebo jsi velmi milý; pročež pozoruj slova toho, a rozuměj vidění tomu.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Sedmdesáte téhodnů odečteno jest lidu tvému a městu svatému tvému k zabránění převrácenosti a k zapečetění hříchů, i vyčištění nepravosti a k přivedení spravedlnosti věčné, a k zapečetění vidění i proroctví, a ku pomazání Svatého svatých.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
Věziž tedy a rozuměj, že od vyjití výpovědi o navrácení a o vystavení Jeruzaléma až do Mesiáše vývody bude téhodnů sedm, potom téhodnů šedesáte dva, když již zase vzdělána bude ulice a příkopa, a ti časové budou přenesnadní.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
Po téhodnech pak těch šedesáti a dvou zabit bude Mesiáš, však jemu to nic neuškodí; nýbrž to město i tu svatyni zkazí, i lid ten svůj budoucí, tak že skončení jeho bude hrozné, ano i do vykonání boje bude boj stálý všelijak do vyplénění.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
Utvrdí však smlouvu mnohým v téhodni posledním, u prostřed pak toho téhodne učiní konec oběti zápalné i oběti suché; a skrze vojsko ohavné, až do posledního a uloženého poplénění hubící, na popléněné vylito bude zpuštění.

< Danieli 9 >