< Danieli 7 >
1 Chaka choyamba cha ufumu wa Belisazara wa ku Babuloni, Danieli akugona pa bedi lake analota maloto ndipo anaona masomphenya. Iye analemba malotowo mwachidule.
Ngomnyaka wokuqala kaBhelishazari inkosi yaseBhabhiloni, uDanyeli waphupha iphupho, kwaphithika imibono engqondweni yakhe elele embhedeni wakhe. Wakubhala phansi okwakuqukethwe liphupho lakhe.
2 Danieli anati, “Mʼmasomphenya anga usiku, ndinaona nyanga yayikulu ikuvunduka ndi mphepo zochokera mbali zonse zinayi za mlengalenga.
UDanyeli wathi: “Embonweni wami ebusuku ngakhangela ngabona phambi kwami imimoya emine yasezulwini iqubula ulwandle olukhulu.
3 Ndipo mʼnyangayo munatuluka zirombo zazikulu zinayi, chilichonse chosiyana ndi chinzake.
Izilo ezine ezinkulu, yileso singafanani lezinye, zaqhamuka olwandle.
4 “Choyamba chinali ngati mkango, ndipo chinali ndi mapiko ngati a chiwombankhanga. Ndinayangʼanitsitsa, kenaka mapiko ake anakhadzuka ndipo chinanyamulidwa ndi kuyimirira ndi miyendo yake iwiri ngati munthu, ndipo anachipatsa mtima wa munthu.
Esakuqala sasinjengesilwane, njalo silamaphiko engqungqulu. Ngabukela amaphiko aso aze akhutshwa, sasesiphakanyiswa emhlabathini sema ngezinyawo ezimbili njengomuntu, sasesiphiwa inhliziyo yomuntu.
5 “Ndipo ndinaona chirombo chachiwiri, chimene chimaoneka ngati chimbalangondo. Chinali chonyamuka mbali imodzi, ndipo chinapana nthiti zitatu mʼkamwa mwake pakati pa mano ake. Anachilamula kuti, ‘Nyamuka, idya nyama yambiri!’
Khonapho phambi kwami kwakujame isilo sesibili esasifana lebhele. Sasiphakanyisiwe kwelinye icele laso, njalo emlonyeni waso sasilezimbambo ezintathu emazinyweni aso. Satshelwa kwathiwa, ‘Sukuma udle inyama usuthe!’
6 “Pambuyo pake, ndinaona chirombo china, chimene chinkaoneka ngati kambuku. Pa msana pake chinali ndi mapiko anayi onga a mbalame. Chirombo ichi chinali ndi mitu inayi, ndipo chinapatsidwa mphamvu kuti chilamulire.
Ngemva kwalokho ngakhangela ngabona phambi kwami esinye isilo esasikhangeleka njengengwe. Emhlane waso sasilamaphiko amane afana lawenyoni. Isilo lesi sasilamakhanda amane, saphiwa amandla okuba sibuse.”
7 “Zitatha izi, mʼmasomphenya anga usiku, ndinaonanso chirombo chachinayi chitayima patsogolo panga. Chinali choopsa, chochititsa mantha ndi champhamvu kwambiri. Chinali ndi mano akuluakulu a chitsulo. Chimati chikatekedza ndi kumeza adani ake kenaka chinapondereza chilichonse chotsala. Ichi chinali chosiyana ndi zirombo zoyambirira zija, ndipo chinali ndi nyanga khumi.
Ngemva kwalokho, embonweni wami ebusuku ngakhangela, kwathi phambi kwami kwema isilo sesine esithuthumelisayo, sisesabeka njalo silamandla amakhulu. Sasilamazinyo ensimbi amakhulu; safohloza esikubambileyo sakudla, okuseleyo sakugxobela phansi. Sasingafanani lazozonke izilo zakuqala, sona silempondo ezilitshumi.
8 “Ndikulingalira za nyangazo, ndinaona nyanga ina, yocheperapo, imene inkatuluka pakati pa zinzake. Zitatu mwa nyanga zoyamba zija zinazulidwa mwa icho. Nyanga iyi inali ndi maso a munthu ndi pakamwa pamene pankayankhula zodzitama.
Ngisalokhu ngicabanga ngempondo lezo, khonapho phambi kwami kwaba lolunye uphondo oluncinyane olwama phakathi kwazo; kwathi ezintathu zempondo zakuqala zagunyulwa phambi kwalo. Uphondo lolu lwalulamehlo anjengamehlo omuntu lomlomo owawukhuluma okokuzikhukhumeza.
9 “Ine ndikuyangʼanabe ndinaona “mipando yaufumu ikukhazikitsidwa, ndipo Mkulu Wachikhalire anakhala pa mpando wake. Zovala zake zinali zoyera ngati chisanu chowundana; tsitsi la kumutu kwake linali loyera ngati thonje. Mpando wake waufumu unali wonga malawi a moto, ndipo mikombero yake yonse inkayaka moto.
“Ngisakhangele, kwabekwa izihlalo zobukhosi, uSimakade wahlala kwesakhe. Izigqoko zakhe zazimhlophe njengeqhwa; inwele zekhanda lakhe zimhlophe njengoboya bezimvu. Isihlalo sakhe sasilavuka umlilo, lamavili aso wonke evutha umlilo.
10 Mtsinje wa moto unkayenda, kuchokera patsogolo pake. Anthu miyandamiyanda ankamutumikira; ndipo anthu osawerengeka anayima pamaso pake. Abwalo anakhala malo awo, ndipo mabuku anatsekulidwa.
Kwakugeleza umfula womlilo, uthutsha ngaphambi kwakhe. Izinkulungwane lezinkulungwane zazimkhonza; izinkulungwane ezilitshumi ziphindwe ngezinkulungwane ezilitshumi zema phambi kwakhe. Inkundla yokwahlulela yahlala phansi, kwasekuvulwa izincwadi.”
11 “Ndinapitiriza kuyangʼanitsitsa chifukwa cha mawu odzitamandira amene nyanga ija inkayankhula. Ndili chiyangʼanire choncho chirombo chachinayi chija chinaphedwa ndipo thupi lake linawonongedwa ndi kuponyedwa mʼngʼanjo ya moto.
Ngasengiqhubeka ngilokhu ngibukele ngenxa yamazwi okuzikhukhumeza ayekhulunywa luphondo. Ngala ngilokhu ngikhangele isilo saze sabulawa, isidumbu saso saphoselwa emlilweni ovuthayo.
12 Zirombo zina zija zinalandidwa ulamuliro wawo, koma zinaloledwa kukhala ndi moyo kwa kanthawi.
(Leziyana ezinye izilo zase ziphuciwe ubukhulu bazo kodwa zavunyelwa ukuphila okwesikhathi esithile.)
13 “Ndikuyangʼanabe zinthu mʼmasomphenya usiku, ndinaona wina ngati mwana wa munthu, akubwera ndi mitambo ya kumwamba. Anayandikira Mkulu Wachikhalire uja. Ena anamuperekeza kwa Iye.
Embonweni wami ebusuku ngakhangela kwabonakala khonapho phambi kwami lowo owayefana lendodana yomuntu esiza ngamayezi ezulu. Yasondela kuSimakade yasiwa phambi kwakhe.
14 Anapatsidwa ulamuliro, ulemerero ndi mphamvu za ufumu kuti anthu a mitundu ina yonse, mayiko ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana apembedze iye. Mphamvu zake ndi mphamvu zamuyaya zimene sizidzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongeka konse.
Yaphiwa amandla lobukhosi lamandla okubusa; bonke abantu, lezizwe zonke labantu bendimi zonke bamkhonza. Ubukhosi bakhe yibukhosi obungapheliyo obungayikwedlula, lombuso wakhe kawusoze uchithwe.
15 “Ine Danieli ndinavutika mu mzimu, ndipo zimene ndinaziona mʼmasomphenya zinandisautsa mʼmaganizo.
Mina Danyeli, ngakhathazeka emoyeni, lemibono eyayidlula engqondweni yami yangidabula.
16 Ndinayandikira mmodzi mwa amene anayima pamenepo ndi kumufunsa tanthauzo lenileni la zonsezi. “Kotero anandiwuza ndi kundipatsa tanthauzo la zinthu zonse izi:
Ngasondela komunye walabo ababemi khonapho ngambuza okuyikho okutshiwo yikho konke lokhu. Yikho wangitshela wangipha ingcazelo yezinto lezi, wathi:
17 ‘Zirombo zikuluzikulu zinayi zija ndi maufumu anayi amene adzaoneka pa dziko lapansi.
“Izilo ezine ezinkulu yimibuso emine ezaqhamuka emhlabeni.
18 Koma oyera mtima a Wammwambamwamba adzalandira ufumu ndipo udzakhala nawo mpaka muyaya, inde ku nthawi zonse.’
Kodwa abangcwele bakhe oPhezukonke bazawemukela umbuso ube ngowabo lanininini, yebo, okwanini lanini.”
19 “Kenaka ndinafuna kudziwa tanthauzo lenileni la chirombo chachinayi chija, chimene chinali chosiyana ndi zinzake zonse ndi choopsa kwambiri, cha mano ake achitsulo ndi zikhadabo zamkuwa; chirombo chimene chinapweteka ndi kumeza zinazo ndi kupondaponda chilichonse chimene chinatsala.
Ngase ngifisa ukwazi ingcazelo eqotho eyesilo sesine, esasingafanani lezinye njalo sisesabeka kakhulu, ngamazinyo aso ensimbi lenzipho zethusi, isilo esafohloza sadla esikubambileyo sagxobagxoba okuseleyo.
20 Ndinafunanso kudziwa za nyanga khumi za pa mutu pake ndiponso ina ija, nyanga imene inaphuka pambuyo pake ndi kugwetsa zitatu zija. Imeneyi ndi nyanga ija yokhala ndi maso ndi pakamwa poyankhula modzitamandira, ndipo inkaoneka yayikulu kupambana zina zonse.
Ngafuna njalo ukwazi ngempondo ezilitshumi ekhanda laso langalolo olunye uphondo olwamilayo, okwathi ezinye ezintathu zawa phambi kwalo lolophondo olwabonakala kakhulu kulezinye, olwalulamehlo kanye lomlomo owawukhuluma ngokukloloda.
21 Ndikuyangʼanitsitsa, nyanga imeneyi inathira nkhondo anthu oyera mtima ndi kuwagonjetsa,
Ngilokhu ngibukele, uphondo lolu lwalusilwa luhlasela abangcwele lubehlula,
22 mpaka pamene Mkulu Wachikhalire uja anafika ndi kuweruza mokomera oyera mtima a Wammwambamwamba. Tsono nthawi inafika imene anthu oyera mtimawo analandira ufumu.
kwaze kwafika uMvelinqaki wabalamulela abangcwele bakhe oPhezukonke, kwafika isikhathi bawuthatha umbuso.
23 “Tsono anandifotokozera kuti, ‘Chirombo chachinayi chija ndi ufumu wachinayi umene udzaoneka pa dziko lapansi. Udzakhala wosiyana ndi maufumu anzake onse ndipo udzawononga dziko lonse lapansi. Udzalipondaponda ndi kuliphwasula.
Wangipha ingcazelo le: Isilo sesine singumbuso wesine ozavela emhlabeni. Uzaba lomahluko kweminye yonke imibuso njalo uzawuthumba wonke umhlaba, uwugxobagxobe, uwufohloze.
24 Nyanga khumi zija ndiwo mafumu khumi amene adzatuluka mu ufumu umenewu. Pambuyo pake mfumu ina idzadzuka, yosiyana ndi mafumu a mʼmbuyomu; iyo idzagonjetsa mafumu atatu.
Impondo ezilitshumi ngamakhosi alitshumi azavela kuwo lo umbuso. Ngemva kwawo kuzavela enye inkosi engafani lalayana awokuqala; izanqoba amakhosi amathathu.
25 Idzayankhula motsutsana ndi Wammwambamwamba ndipo adzazunza oyera mtima ndi kusintha masiku azikondwerero ndi malamulo. Oyera mtimawo adzalamulidwa ndi mfumuyi kwa zaka zitatu ndi theka.
Izakhuluma okubi ngoPhezukonke incindezele abangcwele bakhe izame ukuguqula izikhathi ezimisiweyo kanye lemithetho. Abangcwele bazanikelwa kuyo okwesikhathi esithile, izikhathi ezilengxenye yesikhathi.
26 “‘Koma bwalo lidzapereka chiweruzo, ndipo mphamvu zake zidzalandidwa ndi kuwonongedwa kotheratu mpaka muyaya.
Kodwa umthethwandaba uzahlala phansi, amandla ayo asuswe abhidlizwe okwanini lanini.
27 Kenaka ulamuliro, mphamvu ndi ukulu wa maufumu pa dziko lonse lapansi zidzaperekedwa kwa oyera mtima, a Wammwambamwamba. Ufumu wawo udzakhala ufumu wosatha, ndipo olamulira onse adzawalamulira ndi kuwamvera.’”
Lapho-ke ubukhosi, lamandla lobukhulu bemibuso leyo ngaphansi kwezulu lonke kuzaphiwa abangcwele, abantu bakhe oPhezukonke. Umbuso wakhe uzakuba ngumbuso ongapheliyo, njalo bonke ababusi bazamkhonza bamlalele.
28 “Apa ndiye pa mapeto pa nkhaniyi. Ine Danieli, ndinasautsidwa kwambiri mʼmaganizo anga, ndipo nkhope yanga inasandulika, koma ndinasunga nkhaniyi mu mtima mwanga.”
“Lokhu yikho ukuphela kwendaba. Mina Danyeli ngakhathazeka kakhulu ngemicabango yami, ubuso bami bahloba, kodwa indaba le yaba yimfihlo yami.”