< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
Сподо́балося Дарієві, і він поставив над царством сто й двадцять сатра́пів, щоб були над усім царством.
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
А вище від них — три найвищі урядники, що одним із них був Даниїл, яким ці сатра́пи здавали звіт, а цар щоб не був пошкодо́ваний.
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
Тоді цей Даниїл блищав над найвищими урядниками та сатра́пами, бо в ньому був високий дух, і цар заду́мував поставити його над усім царством.
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
Тоді найвищі урядники та сатра́пи стали шукати причини оска́ржити Даниїла в справі царства, але жодної причини чи ва́ди знайти не могли́, бо той був вірний, і жодна по́милка чи вада не була зна́йдена на нього.
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
Тоді ці люди сказали: „Ми не зна́йдемо на цього Даниїла жодної причини, якщо не зна́йдемо проти нього в зако́ні його Бога“.
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
Тоді найвищі урядники та ті сатра́пи поспішили до царя, і так йому говорили: „Ца́рю Да́ріє, живи навіки!
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
Нара́дилися всі найвищі урядники царства, заступники та сатра́пи, радники та підсатрапи встановити царську́ постанову та видати заборо́ну, щоб аж до тридцяти день кожен, хто буде просити яке проха́ння від якогобудь бога чи люди́ни, крім від тебе, о ца́рю, був уки́нений до ле́в'ячої ями.
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
Тепер, ца́рю, затверди́ цю заборону, і напиши це писа́ння, яке не могло б бути змінене за зако́ном мі́дян та персів, що не міг би бути відмі́нений“.
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
Тому́ цар Дарій написав це писа́ння та заборо́ну.
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
А Даниїл, коли довідався, що було написане те писа́ння, пішов до свого дому, — а ві́кна його в його го́рниці були відчинені навпроти Єрусалиму, і в три уста́лені порі́ на день він па́дав на свої коліна, і молився та сла́вив свого Бога, бо робив так і перед тим.
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
Тоді ці мужі поспішили до нього, і знайшли Даниїла, що він просив та благав свого Бога.
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
Тоді вони підійшли й розповіли́ перед царем про царську́ заборону: „Чи ж не написав ти заборони, що кожна люди́на, яка буде просити аж до тридцяти день від якогобудь бога чи люди́ни, окрім від тебе, ца́рю, буде вкинена до ле́в'ячої ями?“Цар відповів та й сказав: „Це слово певне, як право мі́дян та персів, що не може бути відмінене“.
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
Тоді вони відповіли́ та й сказали перед царем: „Даниїл, що з вигна́ння Юдиних синів, не звернув уваги на тебе, о ца́рю, та на заборону, яку написав ти, і в три уста́лені порі́ на день приносить свою молитву“.
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
Тоді цар, як почув це слово, сильно засмути́вся, і звернув свою думку на Даниїла, щоб його врятувати, і аж до за́ходу сонця силувався ви́зволити його.
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
Того ча́су ці мужі поспішили до царя, і говорили цареві: „Знай, ца́рю, що за правом мі́дян та персів усяка заборона та постанова, яку цар устано́вить, не може бути змі́нена“.
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
Тоді цар звелів, і привели́ Даниїла, та й кинули до ле́в'ячої ями. Цар заговорив і сказав Даниїлові: „Твій Бог, що ти Йому служиш, Він за́вжди врятує тебе!“
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
І прине́сений був один камінь, і був покладений на о́твір ями, а цар запеча́тав її своєю печаткою та печаткою своїх вельмо́ж, що не бу́де змінена Даниїлова справа.
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
Тоді цар пішов до свого пала́цу, і провів ніч у по́сті, і до нього не впроваджено нало́жниці, а сон його помандрува́в від нього.
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
Того ча́су цар устав за зірни́ці на світа́нку, і в по́спіху пішов до ле́в'ячої ями.
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
А як цар наближа́вся до ями, до Даниїла, то кликнув сумним голосом. Цар заговорив та й сказав до Даниїла: „Даниїле, ра́бе Бога Живого, чи твій Бог, Якому ти за́вжди служиш, міг урятувати тебе від ле́вів?“
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
Тоді Даниїл заговорив із царем: „Ца́рю, навіки живи!
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
Мій Бог послав Свого Ангола, і позамикав па́щі ле́вів, і вони не пошко́дили мені, бо перед Ним зна́йдено було мене невинним, а також перед тобою, ца́рю, я не зробив шкоди“.
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
Тоді цар сильно зрадів, і сказав вивести Даниїла з ями. І Даниїл був ви́ведений з ями, і жодної шкоди не зна́йдено на ньому, бо він вірував у Бога свого́.
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
І сказав цар, і привели́ тих мужів, що доне́сли на Даниїла, і повкида́ли до ле́в'ячої ями їх, їхніх дітей та їхніх жіно́к. І вони не сягнули ще до дна ями, як леви вже похапа́ли їх, і поторо́щили всі їхні кості.
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
Того ча́су цар Дарій написав до всіх наро́дів, племе́н та язи́ків, що ме́шкали по всій землі: „Нехай мир вам примно́житься!
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
Від мене виданий нака́з, щоб у всьому панува́нні мого царства тремтіли та боялися перед Даниїловим Богом, бо Він Бог Живий і існує повіки, і царство Його не буде зруйно́ване, а панува́ння Його — аж до кінця.
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
Він рятує та визволя́є, і чинить зна́ки та чу́да на небі та на землі, Він урятував Даниїла від ле́в'ячої сили“.
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
І той Даниїл мав пово́дження за царюва́ння Да́рія та за царюва́ння Кіра перського.

< Danieli 6 >