< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
to acceptable before Darius and to stand: establish since kingdom [the] to/for satrap [the] hundred and twenty that to be in/on/with all kingdom [the]
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
and above from them chief three that Daniel one from them that to be satrap [the] these to give to/for them account [the] and king [the] not to be to suffer injury
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
then Daniel this to be to distinguish oneself since chief [the] and satrap [the] like/as to/for before: because that spirit preeminent in/on/with him and king [the] to plan to/for to stand: establish him since all kingdom [the]
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
then chief [the] and satrap [the] to be to ask pretext to/for to find to/for Daniel from side kingdom [the] and all pretext and to corrupt not be able to/for to find like/as to/for before: because that to trust he/she/it and all neglect and to corrupt not to find since him
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
then man [the] these to say that not to find to/for Daniel this all pretext except to find since him in/on/with law god his
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
then chief [the] and satrap [the] these to throng since king [the] and thus to say to/for him Darius king [the] to/for perpetuity to live
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
to counsel all chief kingdom [the] prefect [the] and satrap [the] counselor [the] and governor [the] to/for to stand: establish statute king [the] and to/for to grow strong injunction that all that to ask petition from all god and man till day thirty except from you king [the] to cast to/for den lion [the]
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
now king [the] to stand: establish injunction [the] and to sign inscription [the] that not to/for to change like/as law Mede and Persia that not to pass on/over/away
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
like/as to/for before: because this king [the] Darius to sign inscription [the] and injunction [the]
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
and Daniel like/as that to know that to sign inscription [the] to come to/for house his and window to open to/for him in/on/with roof his before Jerusalem and time three in/on/with day [the] he/she/it to bless since knee his and to pray and to praise before god his like/as to/for before: because that to be to make from previously this
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
then man [the] these to throng and to find to/for Daniel to ask and be gracious before god his
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
in/on/with then to approach and to say before king [the] since injunction king [the] not injunction to sign that all man that to ask from all god and man till day thirty except from you king [the] to cast to/for den lion [the] to answer king [the] and to say certain word [the] like/as law Mede and Persia that not to pass on/over/away
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
in/on/with then to answer and to say before king [the] that Daniel that from son captivity [the] that Judah not to set: put/give (since you *Q(k)*) king [the] command and since injunction [the] that to sign and time three in/on/with day [the] to ask petition his
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
then king [the] like/as that word [the] to hear greatly be displeased since him and since Daniel to set: put/give mind to/for to rescue him and till going down sun [the] to be to strive to/for to rescue him
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
in/on/with then man [the] these to throng since king [the] and to say to/for king [the] to know king [the] that law to/for Mede and Persia that all injunction and statute that king [the] to stand: establish not to/for to change
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
in/on/with then king [the] to say and to come to/for Daniel and to cast to/for den [the] that lion [the] to answer king [the] and to say to/for Daniel god your that (you *Q(k)*) to serve to/for him in/on/with continuance [the] he/she/it to rescue you
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
and to come stone one and to set: put/give since mouth den [the] and to seal her king [the] in/on/with signet ring his and in/on/with signet ring noble his that not to change thing in/on/with Daniel
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
then to go king [the] to/for temple: palace his and to lodge fasting and diversion not to come before him and sleep his to flee since him
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
in/on/with then king [the] in/on/with dawn [the] to stand: rise in/on/with daylight [the] and in/on/with to dismay to/for den [the] that lion [the] to go
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
and like/as to approach he to/for den [the] to/for Daniel in/on/with voice: sound to pain to cry out to answer king [the] and to say to/for Daniel Daniel servant/slave god [the] living [the] god your that (you *Q(k)*) to serve to/for him in/on/with continuance [the] be able to/for to rescue you from lion [the]
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
then Daniel with king [the] to speak king [the] to/for perpetuity to live
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
god my to send angel his and to shut mouth lion [the] and not to destroy me like/as to/for before: because that before him innocence to find to/for me and also (before you *Q(k)*) king [the] crime not to make
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
in/on/with then king [the] greatly be good since him and to/for Daniel to say to/for to ascend from den [the] and to ascend Daniel from den [the] and all harm not to find in/on/with him that to trust in/on/with god his
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
and to say king [the] and to come man [the] these that to devour charges his that Daniel and to/for den lion [the] to cast they son their and woman their and not to reach to/for bottom den [the] till that to rule in/on/with them lion [the] and all bone their to break up
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
in/on/with then Darius king [the] to write to/for all people [the] people [the] and tongue [the] that (to dwell *Q(k)*) in/on/with all earth: planet [the] peace your to grow great
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
from before me to set: make command that in/on/with all dominion kingdom my to be (to tremble *Q(k)*) and to fear from before god his that Daniel that he/she/it god [the] living [the] and enduring to/for perpetuity and kingdom his that not to destroy and dominion his till end [the]
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
to rescue and to rescue and to make sign and wonder in/on/with heaven [the] and in/on/with earth: planet [the] that to rescue to/for Daniel from hand lion [the]
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
and Daniel this to prosper in/on/with kingdom Darius and in/on/with kingdom Cyrus (Persian [the] *Q(k)*)

< Danieli 6 >