< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
Darius deemed it proper, and he set over the kingdom one hundred and twenty lieutenants, who should be over all the kingdom;
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
And over these, three presidents, of whom Daniel was one; that these lieutenants should give accounts unto them, so that the king might suffer no damage.
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
Then did this Daniel excel [all] the presidents and lieutenants, because a superior spirit was in him: and the king thought to appoint him over the whole kingdom.
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
Then sought the presidents and lieutenants to find a pretext against Daniel on account of the management of the kingdom; but they were not able to find any pretext or fault, forasmuch as he was faithful, and no kind of error or fault was to be found on him.
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
Then said these men, We shall not find any pretext against this Daniel, except we find it against him in the law of his God.
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
Then came these presidents and lieutenants tumultuously to the king, and thus said they unto him, King Darius, live for ever.
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
All the presidents of the kingdom, the superintendents, and the lieutenants, the counsellors, and the governors, have consulted together to establish a royal statute, and to make a firm prohibition, that whosoever will ask any thing by prayer of any God or man within thirty days, save of thee, O king, shall be cast into the den of lions.
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
Now, O king, establish the prohibition, and sign the writing, that it cannot be changed, according to the law of the Medes and Persians, which is not to be repealed.
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
In view of this king Darius signed the writing and the prohibition.
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
Now when Daniel knew that the writing was signed, he went up unto his house, where he had open windows in his upper chamber in the direction of Jerusalem; and three times every day he kneeled upon his knees, and prayed, and offered thanks before his God, as he had been doing before that time.
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
Then came in these men tumultuously, and found Daniel praying and making supplication before his God.
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
Then came they near, and spoke before the king concerning the king's prohibition, Hast thou not signed a prohibition, that every man that will pray [for aught] of any God or man, within thirty days, save of thee, O king, shall be cast into the den of lions? The king answered and said, The thing is certainly so, according to the law of the Medes and Persians, which cannot he repealed.
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
Then answered they and said before the king, That Daniel, who is of the children of the exiles of Judah, hath paid no regard to thee, O king, nor to the prohibition which thou hast signed; but three times every day he offereth up his prayer.
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
Then the king, when he heard this matter, felt very much distressed within himself, and on account of Daniel he sought an excuse to deliver him; and till the going down of the sun he strove hard to rescue him.
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
Then came these men tumultuously unto the king, and said unto the king, Know, O king, that it is the law of the Medes and Persians. That every prohibition and statute which the king hath established is not to be changed.
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
Then gave the king the order, and they brought Daniel, and cast him into the den of lions. The king commenced and said unto Daniel, May thy God whom thou worshippest continually, truly deliver thee.
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
And a stone was brought, and placed upon the mouth of the den; and the king sealed it with his own signet-ring, and with the signet-ring of his lords, that nothing should be changed in the purpose concerning Daniel.
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
Then went the king to his palace, and passed the night fasting: and no food was brought before him; and his sleep fled from him.
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
Then arose the king by the morning-dawn, as soon as it was light, and went in great haste unto the den of lions.
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
And when he came near to the den, he cried with a mournful voice unto Daniel: the king commenced and said to Daniel, O Daniel, servant of the living God, hath thy God, whom thou worshippest continually, been able to deliver thee from the lions!
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
Then spoke Daniel with the king, O king, live for ever.
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
My God sent his angel, and locked up the mouths of the lions, and they have not hurt me; forasmuch as before him innocency was found in me; and also before thee, O king, had I done nothing injurious.
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
Then was the king exceedingly glad within himself, and concerning Daniel he ordered to bring him up out of the den. So was Daniel brought up out of the den, and no manner of hurt was found upon him, because he had trusted in his God.
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
And the king gave the order, and they brought those men who had accused Daniel treacherously, and they cast into the den of lions them, their children, and their wives; and they had not yet touched the bottom of the den when the lions had the mastery over them, and ground up all their bones.
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
Then wrote king Darius unto all people, nations, and languages, that dwell on all the earth, May your welfare increase.
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
From me is it decreed, That in all the dominion of my kingdom men shall tremble and have fear before the God of Daniel; for he is the living God, and endureth for ever, and it is his kingdom which will not be destroyed, and his dominion will be unto the end [of things].
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
He delivereth and rescueth, and he displayeth sings and wonders in heaven and on earth, he who hath delivered Daniel from the power of the lions.
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
So this Daniel prospered in the reign of Darius, and in the reign of Cyrus the Persian.

< Danieli 6 >