< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
It pleased Darius, and so he appointed over the kingdom one hundred twenty governors, to be placed throughout his whole kingdom.
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
And over these, three leaders, of whom Daniel was one, so that the governors would be accountable to them and the king would have no trouble.
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
And so Daniel excelled above all the leaders and governors, because a greater spirit of God was in him.
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
Furthermore, the king considered setting him over the entire kingdom; whereupon the leaders and the governors sought to find a complaint against Daniel and in favor of the king. And they could find no case, or even suspicion, because he was faithful, and no fault or suspicion was found in him.
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
Therefore, these men said, “We will not find any complaint against this Daniel, unless it is against the law of his God.”
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
Then the leaders and governors took the king aside privately and spoke to him in this way: “King Darius, live forever.
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
All the leaders of your kingdom, the magistrates and governors, the senators and judges, have taken counsel that an imperial decree and edict should be published, so that all who ask any petition of any god or man for thirty days, except of you, O king, will be cast into the den of lions.
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
Now, therefore, O king, confirm this judgment and write the decree, so that what is established by the Medes and Persians may not be altered, nor will any man be allowed to transgress it.”
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
And so king Darius set forth the decree and established it.
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
Now when Daniel learned of this, namely, that the law had been established, he entered his house, and, opening the windows in his upper room towards Jerusalem, he knelt down three times a day, and he adored and gave thanks before his God, as he had been accustomed to do previously.
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
Therefore, these men, inquiring diligently, discovered that Daniel was praying and making supplication to his God.
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
And they approached and spoke to the king about the edict. “O king, did you not decree that every man who makes a request to any of the gods or men for thirty days, except to yourself, O king, would be cast into the den of lions?” To which the king replied, saying, “The sentence is true, and according to the decree of the Medes and Persians, it is not lawful to violate it.”
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
Then they answered and said before the king, “Daniel, of the sons of the captivity of Judah, is not concerned about your law, nor about the decree that you have established, but three times a day he prays his supplication.”
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
Now when the king had heard these words, he was greatly grieved, and, on behalf of Daniel, he set his heart to free him, and he labored even until sunset to rescue him.
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
But these men, knowing the king, said to him, “You know, O king, that the law of the Medes and Persians is that every decree which the king has established may not be altered.”
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
Then the king commanded, and they brought Daniel and cast him into the den of lions. And the king said to Daniel, “Your God, whom you always serve, he himself will free you.”
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
And a stone was brought, and it was placed over the mouth of the den, which the king sealed with his own ring, and with the ring of his nobles, so that no one would act against Daniel.
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
And the king departed into his house, and he went to bed without eating, and food was not set before him, moreover, even sleep fled from him.
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
Then the king, getting himself up at first light, went quickly to the den of lions.
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
And coming near to the den, he cried out with a tearful voice to Daniel and spoke to him. “Daniel, servant of the living God, your God, whom you serve always, do you believe he has prevailed to free you from the lions?”
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
And Daniel, answering the king, said, “O king, live forever.
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
My God has sent his angel, and he has closed the mouths of the lions, and they have not harmed me, because before him justice has been found in me, and, even before you, O king, I have committed no offense.”
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
Then was the king exceedingly glad for him, and he commanded that Daniel should be taken out of the den. And Daniel was taken out of the den, and no wound was found in him, because he believed in his God.
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
Moreover, by order of the king, those men were brought who had accused Daniel, and they were cast into the lions’ den, they, and their sons, and their wives, and they did not reach the bottom of the den before the lions seized them and crushed all their bones.
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
Then king Darius wrote to all peoples, tribes, and languages dwelling in all the land. “May peace be increased with you.
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
It is hereby established by my decree that, in all my empire and my kingdom, they shall begin to tremble and fear the God of Daniel. For he is the living and eternal God forever, and his kingdom will not be destroyed, and his power will last forever.
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
He is the liberator and the savior, performing signs and wonders in heaven and on earth, who has freed Daniel from the lions’ den.”
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
Thereafter, Daniel continued through the reign of Darius until the reign of Cyrus, the Persian.

< Danieli 6 >