< Danieli 5 >

1 Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
Balsazar král učinil hody veliké tisíci knížatům svým, a před nimi víno pil.
2 Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
A když pil víno Balsazar, rozkázal přinésti nádobí zlaté a stříbrné, kteréž vynesl Nabuchodonozor otec jeho z chrámu Jeruzalémského, aby z něho pili král i knížata jeho, ženy jeho i ženiny jeho.
3 Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
I přineseno jest nádobí zlaté, kteréž vynesli z chrámu domu Božího, kterýž byl v Jeruzalémě, a pili z něho král i knížata jeho, ženy jeho i ženiny jeho.
4 Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
Pili víno, a chválili bohy zlaté a stříbrné, měděné, železné, dřevěné a kamenné.
5 Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
V touž hodinu vyšli prstové ruky lidské, a psali naproti svícnu na stěně paláce královského, a král hleděl na částky ruky, kteráž psala.
6 Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
Tedy jasnost královská změnila se, a myšlení jeho zkormoutila ho, a pasové bedr jeho rozpásali se, i kolena jeho jedno o druhé se tlouklo.
7 Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
A zkřikl král ze vší síly, aby přivedeni byli hvězdáři, Kaldejští a hadači. I mluvil král a řekl mudrcům Babylonským: Kdokoli přečte psání toto, a výklad jeho mi oznámí, šarlatem odín bude, a řetěz zlatý na hrdlo jeho, a třetím v království po mně bude.
8 Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
I předstoupili všickni mudrci královští, ale nemohli písma toho čísti, ani výkladu oznámiti králi.
9 Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
Pročež král Balsazar velmi předěšen byl, a jasnost jeho změnila se na něm, ano i knížata jeho zkormouceni byli.
10 Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
Královna pak, příčinou té věci královské a knížat jeho, do domu těch hodů vešla, a promluvivši královna, řekla: Králi, na věky živ buď. Nechť tě neděsí myšlení tvá, a jasnost tvá nechť se nemění.
11 Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
Jest muž v království tvém, v němž jest duch bohů svatých, v kterémž za dnů otce tvého osvícení, rozumnost a moudrost, jako moudrost bohů, nalezena, jehož král Nabuchodonozor otec tvůj knížetem mudrců, hvězdářů, Kaldejských a hadačů ustanovil, otec tvůj, ó králi,
12 Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
Proto že duch znamenitý, i umění a rozumnost vykládání snů a oznámení pohádek, i rozvázání věcí nesnadných nalezeno při Danielovi, jemuž král jméno dal Baltazar. Nechať nyní zavolán jest Daniel, a oznámíť výklad ten.
13 Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
Tedy přiveden jest Daniel před krále. I mluvil král a řekl Danielovi: Ty-li jsi ten Daniel, jeden z synů zajatých Judských, kteréhož přivedl král otec můj z Judstva?
14 Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
Slyšel jsem zajisté o tobě, že duch bohů svatých jest v tobě, a osvícení i rozumnost a moudrost znamenitá nalezena jest v tobě.
15 Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
A nyní přivedeni jsou přede mne mudrci a hvězdáři, aby mi písmo toto přečtli, a výklad jeho oznámili, a však nemohli výkladu věci té oznámiti.
16 Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
Já pak slyšel jsem o tobě, že můžeš to, což jest nesrozumitelného, vykládati, a což nesnadného, rozvázati. Protož nyní, budeš-li moci písmo to přečísti, a výklad jeho mně oznámiti, v šarlat oblečen budeš, a řetěz zlatý na hrdlo tvé, a třetím v království po mně budeš.
17 Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
Tedy odpověděl Daniel a řekl před králem: Darové tvoji nechť zůstávají tobě, a odplatu svou dej jinému, a však písmo přečtu králi, a výklad oznámím jemu.
18 “Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
Ty králi, slyš: Bůh nejvyšší královstvím a důstojností i slávou a okrasou obdařil Nabuchodonozora otce tvého,
19 Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
A pro důstojnost, kterouž ho obdařil, všickni lidé, národové a jazykové třásli a báli se před ním. Kohokoli chtěl, zabil, a kterékoli chtěl, bil, kteréž chtěl, povyšoval, a kteréž chtěl, ponižoval.
20 Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
Když se pak bylo pozdvihlo srdce jeho, a duch jeho zmocnil se v pýše, ssazen byl z stolice království svého, a slávu odjali od něho.
21 Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Ano i z spolku synů lidských vyvržen byl, a srdce jeho zvířecímu podobné učiněno bylo, a s divokými osly bylo bydlení jeho. Bylinu jako volům dávali jemu jísti, a rosou nebeskou tělo jeho smáčíno bylo, dokudž nepoznal, že panuje Bůh nejvyšší nad královstvím lidským, a že kohož chce, ustanovuje nad ním.
22 “Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
Ty také, synu jeho Balsazaře, neponížil jsi srdce svého, ačkolis o tom o všem věděl.
23 Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
Ale pozdvihls se proti Pánu nebes; nebo nádobí domu jeho přinesli před tebe, a ty i knížata tvá, ženy tvé i ženiny tvé pili jste víno z něho. Nadto bohy stříbrné a zlaté, měděné, železné, dřevěné a kamenné, kteříž nevidí, ani slyší, aniž co vědí, chválil jsi, Boha pak, v jehož ruce jest dýchání tvé i všecky cesty tvé, neoslavoval jsi.
24 Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
Protož nyní od něho poslána jest částka ruky této, a písmo to napsáno jest.
25 “Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
A totoť jest písmo napsané: Mene, mene, tekel, ufarsin, totiž: Zčetl jsem, zčetl, zvážil a rozděluji.
26 “Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
Tento pak jest výklad slov: Mene, zčetl Bůh království tvé, a k konci je přivedl.
27 Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
Tekel, zvážen jsi na váze, a nalezen jsi lehký.
28 Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
Peres, rozděleno jest království tvé, a dáno jest Médským a Perským.
29 Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
Tedy z rozkazu Balsazarova oblékli Daniele v šarlat, a řetěz zlatý dali na hrdlo jeho, a rozhlašovali o něm, že má býti pánem třetím v království.
30 Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
V touž noc zabit jest Balsazar král Kaldejský.
31 ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.
Darius pak Médský ujal království v letech okolo šedesáti a dvou.

< Danieli 5 >