< Danieli 4 >

1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
Kong Nebukadnesar til alle folk, ætter og tungemål som bor på den hele jord: Alt godt bli eder i rikt mål til del
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
De tegn og under som den høieste Gud har gjort mot mig, har jeg funnet for godt å kunngjøre.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Hvor store er ikke hans tegn, hvor mektige hans under! Hans rike er et evig rike, og hans herredømme varer fra slekt til slekt.
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Jeg, Nebukadnesar, satt i god ro i mitt hus, levde lykkelig i mitt palass.
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
Da hadde jeg en drøm; den forferdet mig, og tankene på mitt leie og synene i mitt indre skremte mig.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
Og det blev av mig utstedt det bud at alle Babels vismenn skulde føres inn for mig, forat de skulde kunngjøre mig drømmens uttydning.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Da kom tegnsutleggerne, åndemanerne, kaldeerne og sannsigerne inn, og jeg fortalte dem drømmen; men de kunde ikke si mig hvorledes den skulde tydes.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
Til sist kom også Daniel inn for mig, han som hadde fått navnet Beltsasar efter navnet på min gud, og i hvem de hellige guders ånd er, og jeg fortalte ham drømmen:
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
Beltsasar, du tegnsutleggernes mester! Efterdi jeg vet at de hellige guders ånd er i dig, og at ingen hemmelighet er dig for vanskelig, så si mig nu de syner jeg har sett i min drøm - si mig hvorledes de skal tydes!
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
Dette var de syner jeg hadde i mitt indre mens jeg hvilte på mitt leie: Jeg så i mitt syn et tre som stod midt på jorden, og som var meget høit;
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
det var et stort og sterkt tre, og så høit at det nådde til himmelen, og det kunde sees helt til jordens ende;
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
dets løv var fagert, og det bar rikelig frukt, så det gav føde for alle; markens dyr fant skygge under det, og himmelens fugler bodde på dets grener, og alt levende nærte sig av det.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Og i de syner jeg hadde i mitt indre mens jeg hvilte på mitt leie, så jeg en hellig vekter som steg ned fra himmelen.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Han ropte med høi røst, og således lød hans ord: Fell treet, hugg dets grener av, riv løvet av det og spred fruktene omkring! Dyrene under det skal rømme, og fuglene flyve bort fra dets grener.
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Men la dets rotstubb stå igjen i jorden, men i lenker av jern og kobber, midt i gresset på marken! Og med himmelens dugg skal han vætes, og med dyrene skal han ha del i jordens urter.
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Hans hjerte skal forandres, så det ikke lenger er et menneskes hjerte; et dyrs hjerte skal han få, og syv tider skal skride frem over ham.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
Dette budskap har sin grunn i vekternes rådslutning, og sådan er de helliges avgjørelser i denne sak, forat alle som lever, skal sanne at den Høieste har makt over kongedømmet blandt menneskene og gir det til den han vil, og setter den ringeste av menneskene til å råde over det.
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Det var den drøm som jeg kong Nebukadnesar, så; kunngjør nu du Beltsasar mig dens uttydning. For ingen av mitt rikes vismenn kan si mig hvad den betyr; men du kan det, fordi de hellige guders ånd er i dig.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Da stod Daniel, han som hadde fått navnet Beltsasar, en stund slått av redsel, og hans tanker forferdet ham. Så tok kongen til orde og sa: Beltsasar! La ikke drømmen og dens uttydning forferde dig! Beltsasar svarte: Min herre! Gid denne drøm måtte gjelde dem som hater dig, og dens uttydning dine fiender!
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Det tre du så, som var så stort og sterkt, og så høit at det nådde til himmelen, og som kunde sees over hele jorden,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
og som hadde så fagert løv og bar så rikelig frukt at det gav føde for alle - som markens dyr hadde tilhold under, og på hvis grener himmelens fugler bodde,
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
det er du selv, konge, du som er så stor og mektig, og hvis velde har vokset så det når til himmelen, og hvis herredømme strekker sig like til jordens ende.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
Men at kongen så en hellig vekter som steg ned fra himmelen og sa: Fell treet og ødelegg det, men la dets rotstubb stå igjen i jorden, men i lenker av jern og kobber, midt i gresset på marken, og med himmelens dugg skal han vætes, og med markens dyr skal han dele lodd så lenge til syv tider har skredet frem over ham,
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
det betyr, konge, og så er den Høiestes rådslutning, som kommer over min herre kongen:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Du skal bli utstøtt fra menneskene, og din bolig skal være hos markens dyr, og urter skal du ete likesom oksene, og med himmelens dugg skal du vætes, og syv tider skal skride frem over dig, inntil du sanner at den Høieste har makt over kongedømmet blandt menneskene og gir det til den han vil.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
Men at det blev sagt at treets rotstubb skulde stå igjen, det betyr at ditt rike skal være ditt fra den tid du sanner at himmelen har makten.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Derfor, konge, la mitt råd tekkes dig, og løs dig fra dine synder ved rettferdighet og fra dine misgjerninger ved barmhjertighet mot ulykkelige, om din lykke skal bli varig.
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Alt dette kom over kong Nebukadnesar.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
Da tolv måneder var til ende, gikk han engang omkring på taket av det kongelige palass i Babel.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
Da tok kongen til orde og sa: Er ikke dette det store Babel, som jeg har bygget til kongesete ved min veldige makt og til ære for min herlighet?
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Før kongen ennu hadde talt ut, kom det brått en røst fra himmelen: Til dig, kong Nebukadnesar, sies nu dette ord: Riket er tatt fra dig,
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
fra menneskene blir du utstøtt, og hos markens dyr skal din bolig være, urter skal du ete likesom oksene, og syv tider skal skride frem over dig, inntil du sanner at den Høieste har makt over kongedømmet blandt menneskene og gir det til den han vil.
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
I samme stund blev dette ord fullbyrdet på Nebukadnesar; han blev utstøtt fra menneskene og åt urter likesom oksene, og av himmelens dugg blev hans kropp vætet, til hans hår vokste og blev som ørnefjær, og hans negler som fugleklør.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
Men da tiden var utløpet, løftet jeg, Nebukadnesar, mine øine til himmelen, og min forstand vendte tilbake, og jeg lovet den Høieste og priste og æret ham som lever evindelig, han hvis herredømme er et evig herredømme, og hvis rike varer fra slekt til slekt.
35 Anthu onse a dziko lapansi
Alle de som bor på jorden, er som intet å akte, og han gjør med himmelens hær og med dem som bor på jorden, hvad han vil, og det er ingen som kan hindre ham og si til ham: Hvad gjør du?
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
Så vendte da på den tid min forstand tilbake, og jeg fikk mitt kongedømmes herlighet, min prakt og min glans igjen, og mine rådsherrer og stormenn søkte mig op, og jeg blev atter innsatt i mitt kongedømme og fikk ennu større makt enn før.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Nu priser og ophøier og ærer jeg, Nebukadnesar, himmelens konge; for alle hans gjerninger er sannhet, og hans stier rettferdighet, og dem som ferdes i overmot, makter han å ydmyke.

< Danieli 4 >