< Danieli 4 >

1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
UNebhukadinezari inkosi, kubo bonke abantu, izizwe, lezindimi, ezihlala emhlabeni wonke: Ukuthula kwenu kakwande!
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Bekukuhle kimi ukuthi ngikwazise izibonakaliso lezimangaliso uNkulunkulu oPhezukonke azenze kimi.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Yeka ubukhulu bezibonakaliso zakhe, njalo yeka amandla ezimangaliso zakhe! Umbuso wakhe ungumbuso ongulaphakade, lokubusa kwakhe kungokwesizukulwana lesizukulwana.
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Mina, uNebhukadinezari, ngangonwabile endlini yami, ngahluma esigodlweni sami,
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
ngabona iphupho elangesabisayo; lemicabango phezu kombheda wami, lemibono yekhanda lami kwangethusa.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
Ngakho umlayo wenziwa yimi wokuthi kungeniswe phambi kwami bonke abahlakaniphileyo beBhabhiloni, ukuze bangazise ingcazelo yephupho.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Kwasekungena izanuse, izangoma, amaKhaladiya, labalumbi; ngasengikhuluma iphupho phambi kwabo, kodwa kabangazisanga ingcazelo yalo.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
Kodwa ngasekucineni uDaniyeli wangena phambi kwami, obizo lakhe lalinguBeliteshazari, ngokwebizo likankulunkulu wami, lokukuye umoya wabonkulunkulu abangcwele; ngasengikhuluma iphupho phambi kwakhe, ngisithi:
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
Wena Beliteshazari, nduna yezanuse, ngoba mina ngiyazi ukuthi umoya wabonkulunkulu abangcwele ukuwe, lokuthi kakulamfihlakalo leyodwa ekuhluphayo, ngitshela imibono yephupho lami engilibonileyo, lengcazelo yalo.
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
Yayinjalo imibono yekhanda lami embhedeni wami: Ngabona, khangela-ke, isihlahla phakathi komhlaba, lobude baso babubukhulu.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
Isihlahla sakhula saba sikhulu, saqina, lobude baso bafinyelela emazulwini, lokubonakala kwaso kwaze kwaba sekucineni komhlaba wonke.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Amahlamvu aso ayemahle, lesithelo saso sasisinengi, kwakukhona kiso ukudla kwabo bonke; inyamazana zeganga zaba lomthunzi ngaphansi kwaso, lenyoni zamazulu zahlala ezingatsheni zaso, layo yonke inyama yondliwa kiso.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Ngabona emibonweni yekhanda lami embhedeni wami, khangela-ke, umlindi, ngitsho ongcwele, wehla evela emazulwini.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Wamemeza ngamandla watsho njalo: Sigamuleni isihlahla, liqume izingatsha zaso, liphulule amahlamvu aso, lichithachithe izithelo zaso; izinyamazana kazisuke ngaphansi kwaso, lezinyoni ngasezingatsheni zaso.
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Lanxa kunjalo tshiyani isidindi sempande zakhe emhlabathini, langebhanti lensimbi lethusi ohlazeni lwasendle; njalo kakumanziswe ngamazolo amazulu, lesabelo sakhe kasibe kanye lezinyamazana etshanini bomhlaba.
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Inhliziyo yakhe kayiphenduke ingabi ngeyomuntu, kayiphiwe inhliziyo yenyamazana; futhi kakwedlule phezu kwakhe izikhathi eziyisikhombisa.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
Loludaba lungesimemezelo sabalindi, lesilayezelo ngelizwi labangcwele; ukuze abaphilayo bazi ukuthi oPhezukonke uyabusa embusweni wabantu, njalo awunike loba kukubani amthandayo, amise phezu kwawo ophansi ebantwini.
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Leliphupho ngilibonile mina nkosi uNebhukadinezari. Wena-ke, Beliteshazari, yitsho ingcazelo yalo; ngoba bonke abahlakaniphileyo bombuso wami bengelakho ukungitshela ingcazelo; kodwa wena ulakho; ngoba umoya wabonkulunkulu abangcwele ukuwe.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Lapho uDaniyeli, obizo lakhe lalinguBeliteshazari, wamangala kakhulu okwesikhatshana, lemicabango yakhe yamkhathaza. Inkosi yaphendula, yathi: Beliteshazari, iphupho lengcazelo yalo kakungakukhathazi. UBeliteshazari waphendula wathi: Nkosi yami, iphupho kalibe kwabakuzondayo, lengcazelo yalo kuzo izitha zakho.
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Isihlahla osibonileyo, esakhula saba sikhulu saqina, lobude baso bafinyelela emazulwini, lokubonakala kwaso kwaze kwaba semhlabeni wonke,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
esimahlamvu aso ayemahle, lesithelo saso sisinengi, njalo kiso kulokudla kwabo bonke, lezinyamazana zeganga zahlala phansi kwaso, lenyoni zamazulu zahlala ezingatsheni zaso;
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
singuwe, wena nkosi, osukhulile waba mkhulu waqina; ngoba ubukhulu bakho bukhulile, bafinyelela emazulwini, lombuso wakho ekucineni komhlaba.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
Njengalokho inkosi yabona umlindi, ngitsho ongcwele, esehla evela emazulwini owathi: Gamulani isihlahla lisichithe; kodwa litshiye isidindi sezimpande emhlabathini sibotshwe ngebhanti lensimbi lethusi ohlazeni lwasendle; kakumanziswe ngamazolo amazulu, lesabelo sakhe kasibe kanye lezinyamazana zeganga, kuze kwedlule izikhathi eziyisikhombisa phezu kwakhe.
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
Nansi ingcazelo, nkosi, njalo nansi isimemezelo soPhezukonke, esiza phezu kwenkosi yami, inkosi:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Ukuthi bazakuxotsha ebantwini, lenhlalo yakho izakuba kanye lezinyamazana zeganga, bazakudlisa utshani njengezinkabi, bazakumanzisa ngamazolo amazulu, lezikhathi eziyisikhombisa zizadlula phezu kwakho, uze wazi ukuthi oPhezukonke uyabusa emibusweni yabantu, ayinike loba kukubani amthandayo.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
Njengalokho bathi kutshiywe isidindi sempande zesihlahla, umbuso wakho uzakuma kuwe, emva kokuthi ususazi ukuthi amazulu ayabusa.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Ngakho, nkosi, kasemukeleke kuwe iseluleko sami; wephule izono zakho ngokulunga, lobubi bakho ngokutshengisa isihawu kwabangabayanga, aluba kungaba lokwelulwa kokuthula kwakho.
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Konke lokhu kwamehlela uNebhukadinezari inkosi.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
Ekupheleni kwenyanga ezilitshumi lambili wayehambahamba phezu kwesigodlo sombuso weBhabhiloni.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
Inkosi yaphendula yathi: Kayisiyo yini le iBhabhiloni enkulu mina engiyakhe ukuba yindlu yombuso, ngamandla engalo yami, njalo ibe ludumo lobukhosi bami?
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Ilizwi lisesemlonyeni wenkosi, kwawa ilizwi livela emazulwini lisithi: Wena nkosi Nebhukadinezari, kuyatshiwo kuwe ukuthi: Umbuso usukile kuwe.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
Bazakuxotsha usuke ebantwini, lenhlalo yakho izakuba kanye lenyamazana zeganga, bazakudlisa utshani njengezinkabi, lezikhathi eziyisikhombisa zizadlula phezu kwakho, uze wazi ukuthi oPhezukonke uyabusa emibusweni yabantu, ayinike loba kukubani amthandayo.
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
Ngalesosikhathi lolulutho lwagcwaliseka phezu kukaNebhukadinezari; wasexotshwa ebantwini, wadla utshani njengezinkabi, lomzimba wakhe wamanziswa ngamazolo amazulu, zaze inwele zakhe zakhula njengensiba zelinqe, lenzipho zakhe njengezenyoni.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
Njalo ekupheleni kwezinsuku, mina Nebhukadinezari ngaphakamisela amehlo ami emazulwini, ngoba ukuqedisisa kwami kwabuyela kimi; ngasengibusisa oPhezukonke, ngamdumisa, ngamhlonipha yena ophila phakade, ngoba ukubusa kwakhe kuyikubusa okulaphakade, lombuso wakhe ungowesizukulwana lesizukulwana;
35 Anthu onse a dziko lapansi
futhi bonke abahlali bomhlaba babalwa njengokungelutho, njalo wenza njengentando yakhe ebuthweni lamazulu lakubahlali bomhlaba; njalo kakho ongavimbela isandla sakhe, loba athi kuye: Wenzani?
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
Ngasona lesosikhathi ingqondo yami yabuyela kimi, futhi ngenxa yenkazimulo yombuso wami udumo lwami lokucwebezela kwami kwabuyela kimi; njalo abeluleki bami lezikhulu zami zangidinga; ngasengimiswa futhi embusweni wami; lobukhulu obudluleleyo bengezelelwa kimi.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Khathesi, mina, Nebhukadinezari, ngiyayidumisa ngiyiphakamise ngiyihloniphe iNkosi yamazulu, ngoba imisebenzi yayo yonke iliqiniso, lezindlela zayo ziyisahlulelo; lalabo abahamba ngokuzigqaja ilakho ukubathobisa.

< Danieli 4 >