< Danieli 4 >
1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
Inkosi uNebhukhadineza, Ezizweni zonke lebantwini benhlanga zonke abahlala emhlabeni wonke: Sengathi inganda kini inhlalakahle!
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Kuyintokozo kimi ukulitshela ngezibonakaliso ezimangalisayo lezinkinga uNkulunkulu oPhezukonke angenzele zona.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Zinkulu kangakanani izibonakaliso zakhe,
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Mina, Nebhukhadineza, ngangisekhaya esigodlweni sami, nganelisiwe njalo ngikhomba ngophakathi.
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
Ngehlelwa liphupho elangitshayisa uvalo. Ngathi ngilele embhedeni wami kwafika engqondweni yami izifanekiso lezibonakaliso ezangithuthumelisayo.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
Ngasengilaya ukuthi zonke izihlakaniphi zaseBhabhiloni zilethwe phambi kwami ukuthi zingihlahlulele lelophupho.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Kwathi sebefikile omasalamusi, lezangoma, lezingcazi zezinkanyezi lezanuse ngazitshela lelophupho kodwa zehluleka ukungichasisela lona.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
Ekucineni uDanyeli wafika kimi ngamtshela ngephupho lelo. (Uthiwa nguBhelitheshazari, ngokuphathelene lebizo likankulunkulu wami, njalo umoya wabonkulunkulu abangcwele uphakathi kwakhe.)
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
Ngathi kuye, Bhelitheshazari, nduna yabomasalamusi, ngiyazi ukuthi umoya wabonkulunkulu abangcwele uphakathi kwakho, njalo kakukho okuyinkinga kuwe. Nanti iphupho lami; ngihlahlulela lona.
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
Yile imibono eyangivelelayo ngilele embhedeni wami: Ngakhangela, ngabona kumi phambi kwami isihlahla phakathi komango. Ubude baso babule.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
Isihlahla sakhula saba sikhulu saqina, isiqongo saso sakhotha umkhathi; sasibonakala lasemikhawulweni yomhlaba.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Amahlamvu aso ayebukeka, izithelo zaso zinengi kuso kukhona ukudla kwakho konke. Ngaphansi kwaso izinyamazana zeganga zafumana isiphephelo lezinyoni zemoyeni zazihlala emagatsheni aso; zonke izidalwa zisongiwa kuso.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Ezibonakalisweni ezeza ngilele embhedeni wami, ngakhangela, ngabona khonapho phambi kwami kulesithunywa, singongcwele, sisehla sisuka ezulwini.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Samemeza ngelizwi elikhulu sathi: Gamulelani phansi isihlahla licakaze amagatsha aso; liwaphundle amahlamvu aso lihlakaze izithelo zaso. Yekelani izinyamazana zibaleke ngaphansi kwaso kanye lezinyoni emagatsheni aso.
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Kodwa akuthi isidindi saso kanye lempande zakhona kusale kugxumekile emhlabathini phakathi kotshani beganga, kubotshiwe ngensimbi langethusi. Kagxanxwe ngamazolo avela phezulu, njalo kahlale lezinyamazana phakathi kwezihlahla zeganga.
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Ingqondo yakhe kayiguqulwe isuke ebuntwini, aphiwe ingqondo yenyamazana, kuze kudlule iminyaka eyisikhombisa.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
“‘Isinqumo lesi sibikwa yizithunywa, zona ezingcwele yizo ezimemezela lesi isigwebo, ukuze kuthi abaphilayo bazi ukuthi oPhezukonke unguThixo yemibuso yabantu njalo uyabanikela loba kukubani amfunayo futhi enze babuswe ngumuntukazana.’
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Yilo iphupho engibe lalo mina inkosi uNebhukhadineza. Manje-ke Bhelitheshazari, ngitshela ukuthi litshoni, ngoba kasikho isihlakaniphi embusweni wami esingangihlahlulela lona. Kodwa wena ungakwenza, ngoba umoya wabonkulunkulu abangcwele uphakathi kwakho.”
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Yikho uDanyeli (njalo othiwa nguBhelitheshazari) wakhathazeka kakhulu okwesikhathi esithile, imicabango yakhe yamethusa. Yikho inkosi yasisithi, “Bhelitheshazari, ungethuswa liphupho lelo kumbe yincazelo yalo.” UBhelitheshazari waphendula wathi, Nkosi yami, sengathi ngabe iphupho lelo liqonde labo abayizitha zakho lengcazelo yalo ikhomba labo abakuzondayo!
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Isihlahla osibonileyo, esakhula saba sikhulu saqina, isiqongo saso sikhotha isibhakabhaka size sibonakale emhlabeni wonke,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
silamahlamvu abukekayo lezithelo ezinengi, sisipha ukudla kukho konke, siphe isiphephelo izinyamazana zeganga, emagatsheni aso silezindawo zezidleke zezinyoni zemoyeni,
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
wena, Oh nkosi, uyilesosihlahla! Usube mkhulu waba lamandla; ubukhulu bakho sebandile sebuze buthinta isibhakabhaka, lombuso wakho usufinyelela ezindaweni ezikude ezomhlaba.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
“Wena, Oh nkosi, wabona isithunywa, sona esingcwele, sisehla sivela ezulwini sisithi, ‘Sigamuleleni phansi isihlahla lisicakaze, kodwa litshiye isidindi, sibotshiwe ngensimbi langethusi, siphakathi kotshani beganga, impande zaso zisale emhlabathini. Kagxanxwe ngamazolo aphezulu; kaphile njengezinyamazana zeganga kuze kudlule iminyaka eyisikhombisa.’
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
Nansi ingcazelo, Oh nkosi, njalo lesi yisimiso soPhezukonke asimisele umhlekazi wami inkosi:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Uzaxotshwa ebantwini uyehlala lezinyamazana zeganga: uzakudla utshani njengezinkomo, ugxanxwe ngamazolo aphezulu. Kuzakudlula iminyaka eyisikhombisa uze uvume ukuthi oPhezukonke uyabusa phezu kwemibuso yabantu ayinika ingqe ngulowo amthandayo.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
Umlayo wokutshiya isidindi kanye lezimpande zaso utsho ukuthi umbuso wakho uzabuyiselwa kuwe nxatshana usuvuma ukuthi iZulu liyabusa.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Ngakho-ke, Oh nkosi, kuhle ukuthi wamukele ukucebisa kwami: Yekela izono zakho wenze okulungileyo, lobubi bakho ube lomusa kwabancindezelweyo. Lapho-ke mhlawumbe ukuphumelela kwakho kungaqhubeka.”
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Konke lokhu kwenzakala enkosini uNebhukhadineza.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
Sekudlule izinyanga ezilitshumi lambili, inkosi ihambahamba ephahleni lwesigodlo saseBhabhiloni,
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
yathi, “Kakusilo yini iBhabhiloni leli engalakha laba ngumuzi wobukhosi bami na?”
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Kwathi amazwi la elokhu esesemlonyeni wakhe kwehla ilizwi livela ezulwini lathi, “Nanku osukunqunyelwe, nkosi Nebhukhadineza: Amandla akho obukhosi asesusiwe kuwe.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
Uzaxotshwa ebantwini uyehlala lezinyamazana zeganga; uzakudla utshani njengezinkomo. Kuzadlula iminyaka eyisikhombisa uze uvume ukuthi oPhezukonke uyabusa phezu kwemibuso yabantu ayiphe ingqe ngubani ngokuthanda kwakhe.”
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
Masinyane nje okwakutshiwo ngoNebhukhadineza kwagcwaliseka. Waxotshwa ebantwini wadla utshani njengezinkomo. Umzimba wakhe wagxanxwa ngamazolo aphezulu, inwele zakhe zakhula njengezinsiba zengqungqulu, kwathi inzipho zakhe zaba njengenkumba zenyoni.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
Ekupheleni kwalesosikhathi, mina, Nebhukhadineza, ngaphakamisela amehlo ami ezulwini, ingqondo yami yabuya. Ngasengimdumisa oPhezukonke; ngambabaza, ngambonga yena ohlezi kuze kube phakade.
35 Anthu onse a dziko lapansi
Imihlobo yonke yabantu bomhlaba
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
Ngasonalesosikhathi ingqondo yami yabuya, udumo lwami lenkazimulo yami kwabuyiswa kimi ukusekela ubukhosi bombuso wami. Abeluleki bami lezikhulu zami bangidinga bangibuyisela esihlalweni sami sobukhosi, ngase ngisiba mkhulu kulakuqala.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Ngakho-ke mina, Nebhukhadineza, ngiyayidumisa njalo ngiyayibabaza, ngiyiphakamise iNkosi yezulu, ngoba konke ekwenzayo kuqondile futhi lezindlela zayo zonke zilungile. Njalo bonke abazigqajayo iyabathobisa.