< Danieli 4 >
1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
"Le roi Nabuchodonosor à toutes les nations, à tous les peuples et idiomes, qui habitent sur toute la terre: Grande prospérité à vous!
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Les miracles et les prodiges que le Dieu suprême a accomplis à mon égard, j’ai trouvé bon de les faire connaître.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Combien grands sont ses miracles et puissants ses prodiges! Son règne est un règne éternel, et sa domination s’étend d’âge en âge.
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Moi, Nabuchodonosor, j’étais tranquille dans ma maison et florissant dans mon palais,
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
lorsque j’eus un songe qui m’effraya: les pensées qui me hantèrent sur ma couche et les visions de mon esprit m’inspirèrent de l’épouvante.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
Et j’émis l’ordre qu’on introduisît auprès de moi tous les sages de Babylone, afin qu’ils me fissent connaître l’explication du songe.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Alors se présentèrent les devins, les magiciens, les astrologues et les mages; je leur exposai le songe, mais ils ne purent m’en indiquer la signification.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
En dernier lieu se présenta, devant moi Daniel, surnommé Beltchaçar, du nom de mon Dieu, et en qui est l’esprit du Dieu saint; je lui racontai le songe:
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
"Beltchaçar, chef des devins, en qui, je le sais, respire l’esprit du Dieu saint et que ne dépasse aucun mystère, écoute ce que j’ai vu en songe et dis-m’en l’explication.
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
Telle était la vision de mon esprit sur ma couche: je regardais, et voilà qu’un arbre se dressait sur la terre, d’une hauteur énorme.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
L’Arbre était grand et vigoureux, son sommet atteignait le ciel, et on l’apercevait de l’extrémité de toute la terre.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Son feuillage était beau et ses fruits abondants; il fournissait de la nourriture à tous. A son ombre s’abritaient les bêtes des champs, dans ses branches nichaient les oiseaux du ciel, et tous les êtres s’alimentaient de lui.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Je regardais dans la vision de mon esprit sur ma couche, et voilà qu’un ange, un saint descendait du ciel.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Il cria avec force et parla ainsi: Coupez l’arbre, abattez ses branches, faites tomber son feuillage et dispersez ses fruits! Que les bêtes s’enfuient de son ombrage et les oiseaux du ciel de ses branches!
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Seulement laissez subsister dans le sol la souche de ses racines, entourée de chaines de fer et d’airain, au milieu de la verdure des champs. Qu’il soit humecté par la rosée du ciel et qu’avec les bêtes il prenne sa part de l’herbe de da terre!
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Qu’on lui enlève son cœur d’homme et qu’on lui donne un cœur d’animal, et qu’ainsi sept époques passent sur lui!
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
Tel est l’arrêt prononcé par la volonté des anges et la résolution décrétée par les saints, aux seules fins que les vivants reconnaissent que le Très-Haut domine sur la royauté des hommes, qu’il la donne à qui il veut, et qu’il y élève le plus humble des mortels.
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Voilà le songe que j’ai eu, moi le roi Nabuchodonosor; mais toi, Beltchaçar, dis-moi ce qu’il signifie, puisque tous les sages de mon royaume sont incapables de m’en donner l’explication, tandis que toi tu en es capable, l’esprit des Dieux saints étant en toi.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
AIors Daniel, surnommé Beltchaçar, resta environ une heure plongé dans la stupeur, terrifié par ses pensées; mais le roi prit la parole et dit: "Beltchaçar, ne te laisse pas effrayer par le songe et par sa signification!" Et Beltchaçar répondit: "Mon seigneur, puisse ce songe s’appliquer à tes ennemis et sa signification à tes adversaires!
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
L’Arbre que tu as vu, qui était grand et vigoureux, dont le sommet atteignait le ciel et qu’on apercevait de l’extrémité de la terre,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
l’arbre dont le feuillage était beau et les fruits abondants, qui fournissait de la nourriture à tous, à l’ombre duquel habitaient les bêtes des champs et dont les branches servaient d’abri aux oiseaux du ciel,
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
c’est toi-même, ô roi, qui es grand et puissant, dont la grandeur s’est accrue jusqu’à atteindre le ciel et dont le pouvoir s’est étendu jusqu’aux extrémités de la terre!
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
Et si le roi a vu un ange, un saint descendre du ciel et s’écrier: Coupez l’arbre et détruisez-le; seulement laissez subsister dans le sol la souche de ses racines, entourée de chaines de fer et d’airain, au milieu de la verdure des champs; qu’il soit humecté par la rosée du ciel et qu’il partage le sort des bêtes des champs, jusqu’à ce que sept époques aient passé sur lui,
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
voici ce que cela signifie, et tel est l’arrêt du Très-Haut qui atteint mon seigneur le roi:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
On va te chasser du milieu des hommes, et ta demeure sera avec les bêtes des champs; comme aux bœufs on te donnera de l’herbe pour nourriture, on t’humectera par la rosée du ciel, et sept époques passeront ainsi sur toi, jusqu’à ce que tu reconnaisses que le Très-Haut domine sur la royauté des hommes et qu’il la donne à qui il veut.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
Et si l’on a dit de laisser subsister la souche des racines de l’arbre, c’est que ta royauté te sera tenue en réserve pour le moment où tu auras reconnu que le ciel est souverain maître.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
C’Est pourquoi, ô roi, puisse mon conseil t’agréer: Rachète tes péchés par la charité et tes iniquités par la pitié envers les pauvres, si tu veux que ta prospérité se prolonge."
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Tout cela arriva au roi Nabuchodonosor:
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
Au bout de douze mois, il se promenait sur le haut du palais de la royauté à Babylone.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
Alors le roi s’écria: "N’Est-ce pas là Babylone la grande, que j’ai édifiée pour en faire une résidence royale, grâce à ma formidable puissance et pour la gloire de ma majesté?"
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Il n’avait pas encore cessé de parler qu’une voix retentit du haut du ciel: "On t’annonce, roi Nabuchodonosor, que la royauté t’est enlevée.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
On va t’expulser de la société des hommes, et ta demeure sera avec les bêtes des champs; on te fera manger de l’herbe comme aux bœufs, et sept époques passeront sur toi, jusqu’à ce que tu reconnaisses que le Très-Haut est le maître de la royauté des hommes et qu’il la donne à qui il veut."
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
Sur l’heure, cette parole se réalisa pour Nabuchodonosor: il fut chassé du milieu des hommes, mangea de l’herbe comme les bœufs, son corps fut humecté par la rosée du ciel, au point qu’il lui poussa des poils pareils aux plumes des aigles et des ongles comme des griffes d’oiseaux.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
"Mais au terme des jours fixés, moi, Nabuchodonosor, je levai les yeux au ciel, et la raison me revint; je bénis le Très-Haut, je louai et exaltai celui qui vit éternellement, dont la domination dure sans fin et dont la royauté s’étend d’âge en âge.
35 Anthu onse a dziko lapansi
Tous les habitants de la terre sont comptés comme rien devant lui, il agit à sa volonté avec l’armée du ciel et les hôtes de la terre; il n’est personne qui fasse obstacle à son pouvoir et lui dise: "Que fais-tu?"
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
Dès lors, la raison me revint, l’éclat de ma royauté, ma majesté et ma splendeur me furent restitués; mes conseillers et mes grands me recherchèrent, je fus rétabli dans ma royauté, et ma puissance s’accrut encore.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Maintenant, moi, Nabuchodonosor, je loue, exalte et glorifie le roi du ciel, dont tous les actes sont vérité et les voies justice, et qui peut abaisser ceux qui se comportent avec orgueil.