< Danieli 4 >
1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
Nebuchadnezzar king the to all peoples the nations the and languages the which ([are] dwelling *Q(k)*) in all earth the peace your may it increase.
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Signs the and wonders the which he has done with me God (Most High the *Q(k)*) it seemed good before me to declare.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
[are] signs His how much! great and [are] wonders his how much! strong kingdom his [is] a kingdom of perpetuity and dominion his [is] with generation and generation.
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
I Nebuchadnezzar at ease I was in house my and flourishing in palace my.
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
A dream I saw and it made afraid me and imaginings on bed my and [the] visions of head my they alarmed me.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
And from me it was made a decree to bring in before me all [the] wise men of Babylon that [the] interpretation of dream the they will make known to me.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Then ([were] going in *Q(k)*) magicians the conjurers the (Chaldeans the *Q(K)*) and astrologers the and dream the [was] saying I before them and interpretation its not [they were] making known to me.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
And until at last he came in before me Daniel who name his [is] Belteshazzar like [the] name of god my and who a spirit of gods holy [is] in him and dream the before him I said.
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
O Belteshazzar [the] chief of magicians the whom - I I know that a spirit of gods holy [is] in you and any secret not [is] oppressing you [the] visions of dream my which I saw and interpretation its tell!
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
And [the] visions of head my on bed my seeing I was and lo! a tree in [the] midst of land the and height its [was] great.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
It grew great tree the and it grew strong and height its it reached to heavens the and [the] sight of it [was] to [the] end of all land the.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Foliage its [was] beautiful and fruit its [was] plentiful and food for all [was] on it under it it had shade - [the] animal[s] of field the and in branches its (they nested *Q(K)*) [the] birds of heavens the and from it it fed all flesh.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Seeing I was in [the] visions of head my on bed my and lo! a watcher and a holy [one] from heavens the [was] coming down.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
[he was] proclaiming With power and as follows [he was] saying cut down! tree the and cut off! branches its strip off! foliage its and scatter! fruit its let it flee animal[s] the from under it and birds the from branches its.
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Nevertheless [the] stump of roots its in ground the leave! and with a fetter of iron and bronze in grass the of field the and with [the] dew of heavens the let it become wet and [be] with animal[s] the portion its in [the] grass of earth the.
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Heart its away from (human the *Q(k)*) let it be changed and [the] heart of an animal let it be given to it and seven times let them pass over it.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
[is] by [the] decree of Watchers command the and [is by the] word of holy [ones] affair the to [the] cause that they will know living [people] the that [is] having mastery (Most High the *Q(k)*) over [the] kingdom of (human the *Q(k)*) and to whomever whom he will be pleased he will give it and a lowly [one] of humankind he will set up (over it. *Q(k)*)
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
This dream the I saw I king the Nebuchadnezzar (and you *Q(k)*) O Belteshazzar interpretation its - tell! as to because that - all [the] wise men of kingdom my not [are] able interpretation the to make known to me (and you *Q(k)*) [are] able who a spirit of gods holy [is] in you.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Then Daniel who name his [was] Belteshazzar he was appalled about a moment one and thoughts his they alarmed him [was] replying king the and [was] saying O Belteshazzar dream the and interpretation its may not it alarm you [was] replying Belteshazzar and [was] saying (O lord my *Q(k)*) dream the ([be] for enemy your *Q(K)*) and interpretation its ([be] for adversaries your. *Q(k)*)
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Tree the which you saw which it grew great and it grew strong and height its it reached to heavens the and [the] sight of it [was] to all land the.
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
And foliage its [was] beautiful and fruit its [was] plentiful and food for all [was] on it under it it dwelt [the] animal[s] of field the and in branches its they dwelt [the] birds of heavens the.
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
([is] you *Q(k)*) It king O who you have grown great and you have grown strong and greatness your it has grown great and it has reached to heavens the and dominion your [is] to [the] end earth the.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
And that he saw king the a watcher and a holy [one] coming down - from heavens the and saying cut down! tree the and destroy it nevertheless [the] stump of roots its in ground the leave! and with a fetter of iron and bronze in grass the of field the and with [the] dew of heavens the let it become wet and [be] with [the] animal[s] of field the portion its until that seven times they will pass over it.
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
This [is] interpretation the king O and [is] [the] decree of (Most High the *Q(k)*) it which it has reached to (lord my *Q(k)*) king the.
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
And you [they will be] chasing away from humankind and with [the] animal[s] of field the it will be dwelling place your and grass like oxen - to you they will feed and from [the] dew of heavens the you [they will be] making wet and seven times they will pass (over you *Q(k)*) until that you will know that [is] having mastery (Most High the *Q(k)*) over [the] kingdom of humankind and to whomever whom he will be pleased he will give it.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
And that they said to leave [the] stump of roots its of tree the kingdom your to you [will be] enduring from that you will know that [are] having mastery heavens the.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Therefore king O advice my let it be acceptable (to you *Q(k)*) (and sin your *Q(K)*) by right doing break off! and iniquities your by showing mercy to poor people whether it will be a prolonging of prosperity your.
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Everything it came on Nebuchadnezzar king the.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
To [the] end of months two [plus] ten on [the] palace of kingdom the of Babylon walking about he was.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
[was] replying King the and [was] saying ¿ not [is] this it Babylon great which I I built it to a house of a kingdom by [the] strength of power my and for [the] honor of majesty my.
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Still word the [was] in [the] mouth of king the a voice from heavens the it fell to you [they are] saying O Nebuchadnezzar king the kingdom the it has passed away from you.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
And away from humankind you [they are] about to chase and [will be] with [the] animal[s] of field the dwelling place your grass like oxen to you they will feed and seven times they will pass (over you *Q(k)*) until that you will know that [is] having mastery (Most High the *Q(k)*) over [the] kingdom of humankind and to whomever whom he will be pleased he will give it.
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
At it moment the word the it was fulfilled on Nebuchadnezzar and away from humankind he was chased and grass like oxen he ate and from [the] dew of heavens the body his it became wet until that hair his like eagles it grew long and nails his [were] like birds.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
And to [the] end of days the I Nebuchadnezzar eye my - to heavens the I lifted and understanding my on me it returned (and Most High the *Q(k)*) I blessed and [the] [one] living of perpetuity I praised and I glorified that dominion his [is] a dominion of perpetuity and kingdom his [is] with generation and generation.
35 Anthu onse a dziko lapansi
And all ([the] inhabitants of *Q(k)*) earth the [are] as not considered and as pleases he [he is] doing with [the] army of heavens the (and [the] inhabitants of *Q(k)*) earth the and not there [is] who he will strike on hand his so he may say to him what? have you done.
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
At it time the understanding my - it returned to me and to [the] honor of kingdom my majesty my and splendor my it returned to me and me counselors my and nobles my they sought and over kingdom my it was established and greatness surpassing it was added to me.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Now I Nebuchadnezzar [am] praising and [am] lifting up and [am] glorifying [the] king of heavens the who all deeds his [are] truth and ways his [are] justice and [those] who [are] walking in pride [he is] able to bring low.