< Danieli 4 >

1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
Rong Nebukadnezar til alle Folk, Stammer og Tungemaal, som bo paa den ganske Jord: Eders Fred være mangfoldig!
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Det behager mig at forkynde de Tegn og de underfulde Gerninger, som den højeste Gud har gjort imod mig;
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Hans Tegn — hvor store! og hans underfulde Gerninger — hvor mægtige! hans Rige er et evigt Rige og hans Herredømme fra Slægt til Slægt!
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Jeg Nebukadnezar var tryg i mit Hus og livsfrisk i mit Palads.
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
Jeg saa en Drøm, og den forfærdede mig, og Tanker paa mit Leje og mit Hoveds Syner forvirrede mig.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
Derfor blev givet Befaling af mig, at man skulde føre alle vise i Babel ind for mig, for at de skulde kundgøre mig Drømmens Udtydning.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Da kom Spaamændene, Besværgerne, Kaldæerne og Sandsigerne ind; og jeg sagde dem Drømmen, men de kunde ikke kundgøre mig Udtydningen derpaa.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
Men til sidst kom Daniel, som kaldes Beltsazar efter min Guds Navn, og i hvem de hellige Guders Aand er, ind for mig; og jeg sagde ham Drømmen.
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
Beltsazar, du Øverste for Spaamændene! efterdi jeg ved, at de hellige Guders Aand er i dig, og at ingen Hemmelighed er dig vanskelig: Sig mig Synerne i min Drøm, som jeg saa, og Udtydningen derpaa.
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
Og mit Hoveds Syner paa mit Leje vare: Jeg saa og se, der var et Træ midt i Landet, og det var meget højt.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
Træet blev stort og stærkt, og dets Højde rakte til Himmelen, og man kunde se det indtil hele Jordens Ende.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Løvet derpaa var dejligt, og der var megen Frugt derpaa, og der var Føde for alt, som var derpaa; under det fandt Dyrene paa Marken Skygge, og i Grenene derpaa boede Himmelens Fugle, og alt Kød nærede sig deraf.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Jeg saa i mit Hoveds Syner paa mit Leje, og se, en Vægter, det er en hellig, for ned fra Himmelen.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Han raabte med Vælde og sagde saaledes: Hugger Træet om og afhugger dets Grene, afriver dets Løv og spreder dets Frugt; Dyrene flygte fra dets Læ og Fuglene fra dets Grene!
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Dog lader Stubben med dens Rødder blive tilbage i Jorden, men i Baand af Jern og Kobber, i Markens Græs; og lad ham vædes med Himmelens Dug, og hans Del være med Dyrene af Urterne paa Jorden!
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Hans Hjerte skal forandres, saa at det ikke er et Menneskes, og et Dyrs Hjerte skal gives ham; og syv Tider skulle omskiftes over ham.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
Tingen er i Vægternes besluttede Raad, og Sagen er de helliges Befaling, paa det de, som leve, kunne kende, at den Højeste har Magt over Menneskens Rige og giver det til hvem, han vil, og ophøjer den ringe iblandt Menneskene over det.
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Denne Drøm saa jeg, Kong Nebukadnezar; men du, Beltsazar! sig Udtydningen, efterdi alle vise i mit Rige ikke kunne kundgøre Udtydningen, men du kan det, fordi de hellige Guders Aand er i dig.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Da stod Daniel, hvis Navn er Beltsazar, en Stund forskrækket, og hans Tanker forfærdede ham; men Kongen svarede og sagde: Beltsazar! lad Drømmen og Udtydningen ikke forfærde dig; Beltsazar svarede og sagde: Min Herre! Drømmen gælde dine Hadere og dens Udtydning dine Fjender!
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Træet, som du saa, og som blev stort og stærkt, og hvis Højde rakte til Himmelen, og som saas over al Jorden,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
og hvorpaa der var dejligt Løv og megen Frugt og Føde for alt, som var derpaa, under hvilket Dyrene paa Marken boede, og i hvis Grene Himmelens Fugle byggede:
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
Dette er dig selv, o Konge! i thi du er bleven stor og stærk; og din Magt er bleven stor og rækker til Himmelen og dit Herredømme til Jordens Ende.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
Men at Kongen saa en Vægter, det er en hellig, fare ned fra Himmelen og sige: Hugger Træet om og ødelægger det, dog lader Stubben med dens Rødder blive tilbage i Jorden, men i Baand af Jern og Kobber, i Markens Græs; og lad ham vædes af Himmelens Dug og hans Del være med Dyrene paa Marken, indtil syv Tider omskiftes over ham,
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
da er dette Udtydningen, o Konge! og dette er den Højestes besluttede Raad, som skal komme over min Herre, Kongen:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Nemlig, man skal støde dig ud fra Folk, og din Bolig skal være hos Dyrene paa Marken, og man skal lade dig æde Urter som Øksne og vædes af Himmelens Dug, og syv Tider skulle omskiftes over dig, indtil du kender, at den Højeste har Magt over Menneskens Rige og giver det til, hvem han vil.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
Men at der sagdes: Man skulde lade Træets Stub med dens Rødder blive tilbage, det betyder, at dit Rige skal overdrages dig igen fra den Tid, du erkender, at Himlene ere mægtige.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Derfor, o Konge! lad mit Raad behage dig, og afbryd dine Synder ved Retfærdighed og dine Misgerninger ved Barmhjertighed imod de elendige, dersom din Fred skal have Varighed.
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Alt dette kom over Kong Nebukadnezar.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
Der tolv Maaneder vare til Ende, gik han omkring paa det kongelige Palads i Babel.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
Kongen svarede og sagde: Er dette ikke det store Babel, som jeg har bygget til et kongeligt Hus ved min Styrkes Magt og til min Herligheds Ære?
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Da Ordet endnu var i Kongens Mund, faldt der en Røst af Himmelen: Det være dig sagt, Kong Nebukadnezar! Riget er gaaet bort fra dig.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
Og man skal støde dig ud fra Folk, og din Bolig skal være hos Dyrene paa Marken, man skal lade dig æde Urter som Øksne, og syv Tider skulle omskiftes over dig, indtil du kender, at den Højeste har Magt over Menneskens Rige og giver det til, hvem han vil.
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
I samme Stund gik Ordet i Opfyldelse over Nebukadnezar, og han blev udstødt fra Menneskene og aad Urter som Øksne, og hans Legeme blev vædet af Himmelens Dug, indtil hans Haar voksede som Ørnefjer og hans Negle som Fuglekløer.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
Men der disse Dage vare til Ende, opløftede jeg, Nebukadnezar, mine Øjne til Himmelen, og min Forstand kom til mig igen, og jeg lovede den Højeste og priste og ærede ham, som lever evindelig; thi hans Herredømme er et evigt Herredømme, og hans Rige varer fra Slægt til Slægt.
35 Anthu onse a dziko lapansi
Og alle, som bo paa Jorden, ere som intet at regne, efter sin Villie gør han med Himmelens Hær og med dem, som bo paa Jorden; og der er ingen, som kan hindre hans Haand og sige ham: Hvad gør du?
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
Paa samme Tid kom min Forstand til mig igen, og til mit Kongedømmes Ære kom min Herlighed og Glans til mig igen, og mine Raadsherrer og mine Fyrster søgte mig; og jeg blev indsat i mit Rige, og større Herlighed blev mig tillagt.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Nu priser og ophøjer og ærer jeg, Nebukadnezar, Himmelens Konge; thi alle hans Gerninger ere Sandhed, og hans Stier ere Retfærdighed, og han kan ydmyge dem, som vandre i Hovmodighed.

< Danieli 4 >