< Danieli 3 >

1 Mfumu Nebukadinezara anapangitsa fano la golide lotalika mamita 27 ndi mulifupi mwake mamita atatu, ndipo analiyimika mʼchigwa cha Dura mʼchigawo cha Babuloni.
Kral Nebukadnessar altın bir heykel yaptı; boyu altmış, eni altı arşındı. Onu Babil İli'nde, Dura Ovası'na dikti.
2 Kenaka iye anayitanitsa akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, kuti abwere ku mwambo wotsekula fano limene analiyimika lija.
Satrapları, kaymakamları, valileri, danışmanları, haznedarları, yargıçları, güvenlik görevlilerini ve illerin bütün öbür yüksek memurlarını diktiği heykeli adama törenine çağırttı.
3 Choncho akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa, ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, anasonkhana kudzachita mwambo wotsekulira fano limene mfumu Nebukadinezara analiyimika, ndipo mlaliki anayimirira pamaso pa fanolo nati:
Böylece satraplar, kaymakamlar, valiler, danışmanlar, haznedarlar, yargıçlar, güvenlik görevlileri ve illerin bütün öbür yüksek memurları Kral Nebukadnessar'ın diktiği heykeli adama töreni için toplanarak heykelin önünde durdular.
4 “Inu anthu a mitundu yonse ndi a ziyankhulo zonse, mukulamulidwa kuti muchite izi: mitundu ya anthu ndi a chiyankhulo chilichonse
Sonra haberci yüksek sesle bağırdı: “Ey halklar, uluslar, her dilden insanlar, size şöyle yapmanız buyruluyor:
5 mukadzamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muyenera kulambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika.
Boru, ney, lir, kanun, arp, davul ve her çeşit çalgı sesini duyar duymaz yere kapanıp Kral Nebukadnessar'ın dikmiş olduğu altın heykele tapınacaksınız.
6 Aliyense amene sadzalambira ndi kupembedza adzaponyedwa nthawi yomweyo mʼngʼanjo ya moto.”
Her kim yere kapanıp tapınmazsa hemen kızgın fırına atılacaktır.”
7 Choncho anthu onse aja atangomva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, analambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika.
Bu yüzden ne zaman boru, ney, lir, kanun, arp ve her çeşit çalgı sesi duyulsa, bütün halklar, uluslar, her dilden insanlar yere kapanıp Kral Nebukadnessar'ın diktiği altın heykele tapındılar.
8 Pa nthawi imeneyi alawuli ena anafika ndi kuwanenera zoyipa Ayuda.
Bunun üzerine bazı Kildaniler yaklaşıp Yahudiler'i suçladılar.
9 Iwo anati kwa mfumu Nebukadinezara, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
Kral Nebukadnessar'a, “Ey kral, sen çok yaşa!” dediler,
10 Inu mfumu, mwakhazikitsa lamulo kuti aliyense akamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, ayenera kulambira ndi kupembedza fano la golide,
“Boru, ney, lir, kanun, arp, davul ve her çeşit çalgı sesini duyan herkes yere kapanıp altın heykele tapınacak; kim yere kapanıp tapınmazsa kızgın fırına atılacak diye bir buyruk çıkardın, ey kral.
11 ndi kuti aliyense osalambira ndi kupembedza adzaponyedwa mʼngʼanjo ya moto.
12 Koma alipo Ayuda ena Sadirake, Mesaki ndi Abedinego amene munawayika kuti ayangʼanire ntchito ya dera la ku Babuloni. Anthu amenewa sakumvera inu mfumu. Iwo sakutumikira milungu yanu kapena kulambira fano la golide limene munaliyimikalo.”
Oysa Babil İli'nde yüksek görevlere atadığın Şadrak, Meşak, Abed-Nego adında bazı Yahudiler var. Bu adamlar seni saymadılar, ey kral. Senin ilahlarına kulluk etmiyor, diktiğin altın heykele tapınmıyorlar.”
13 Tsono Nebukadinezara anakwiya ndi kupsa mtima kwambiri, ndipo anayitanitsa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego. Choncho amuna awa anabwera pamaso pa mfumu,
Büyük öfkeye kapılan Nebukadnessar, Şadrak'ı, Meşak'ı, Abed-Nego'yu çağırttı. Bu kişiler kralın yanına getirildiler.
14 ndipo Nebukadinezara anawafunsa kuti, “Kodi ndi zoona, Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti simukutumikira milungu yanga kapena kupembedza fano la golide ndinaliyikalo?
Nebukadnessar, “Ey Şadrak, Meşak, Abed-Nego, ilahlarıma kulluk etmediğiniz, diktiğim altın heykele tapınmadığınız doğru mu?” diye sordu,
15 Tsopano ngati muli okonzeka kulambira ndi kupembedza fano ndinalipanga, mukangomva kulira kwa lipenga chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muchita bwino. Koma ngati simulipembedza, mudzaponyedwa mʼnganjo ya moto. Nanga ndi mulungu uti amene adzatha kukupulumutsani mʼmanja anga?”
“Şimdi boru, ney, lir, kanun, arp, davul ve her çeşit çalgı sesini duyar duymaz yere kapanıp yaptığım heykele tapınmaya hazırsanız ne iyi! Ama ona tapınmazsanız, hemen kızgın fırına atılacaksınız. O zaman bakalım hangi ilah sizi elimden kurtaracak?”
16 Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anayankha mfumu Nebukadinezara kuti, “Sikoyenera kuti tikuyankheni pa nkhani imeneyi.
Şadrak, Meşak, Abed-Nego, “Bu konuda kendimizi savunma gereğini duymuyoruz” diye karşılık verdiler,
17 Ngati tiponyedwa mʼngʼanjo ya moto, Mulungu amene timamutumikira akhoza kutipulumutsa ku ngʼanjo yamotoyo, ndipo adzatilanditsa mʼdzanja lanu mfumu.
“Kızgın fırına atılsak bile, ey kral, kendisine kulluk ettiğimiz Tanrı bizi kızgın fırından kurtarabilir; senin elinden de bizi kurtaracaktır.
18 Koma ngakhale Mulungu wathu atapanda kutipulumutsa, tikufuna mudziwe inu mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu kapena kupembedza fano la golide limene munaliyimika.”
Ama bizi kurtarmasa bile bil ki, ey kral, ilahlarına kulluk etmeyiz, diktiğin altın heykele tapınmayız.”
19 Pamenepo Nebukadinezara anapsa mtima ndi Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, ndipo anayipidwa nawo. Iye analamulira kuti ngʼanjo ayitenthetse kasanu ndi kawiri kuposa nthawi zonse,
Nebukadnessar Şadrak, Meşak, Abed-Nego'ya çok öfkelendi; onlara karşı tutumu değişti. Fırının her zamankinden yedi kat daha çok ısıtılmasını buyurdu.
20 ndipo analamula ena mwa asilikali amphamvu kwambiri mʼgulu lake lankhondo kuti amange Sadirake, Mesaki ndi Abedenego ndi kuwaponya mʼngʼanjo ya moto.
Sonra ordusundaki bazı güçlü askerlere Şadrak'ı, Meşak'ı, Abed-Nego'yu bağlayıp kızgın fırına atmalarını buyurdu.
21 Choncho amuna awa, atavala mikanjo yawo, mabuluku, nduwira ndi zovala zina zonse, anamangidwa ndi kuponyedwa mʼngʼanjo ya moto.
Böylece bu kişiler, şalvarları, kaftanları, sarıkları ve öbür giysileriyle birlikte bağlanıp kızgın fırına atıldılar.
22 Tsono popeza lamulo la mfumu linali lofulumiza, ngʼanjo inatenthetsedwa kowirikiza mwakuti malawi ake anapha asilikali amene ananyamula Sadirake, Mesaki ndi Abedenego,
Kralın buyruğu çok sıkı, fırın da çok ısıtılmış olduğundan, Şadrak'ı, Meşak'ı, Abed-Nego'yu götüren adamları ateşin alevleri yakıp öldürdü.
23 ndipo anyamata atatuwa, ali chimangidwire, anagwera mʼngʼanjo ya moto.
Üç adamsa –Şadrak, Meşak, Abed-Nego– bağlı olarak kızgın fırına düştüler.
24 Kenaka mfumu Nebukadinezara anadabwa ndipo anafunsa nduna zake kuti, “Kodi sanali amuna atatu amene anamangidwa ndi kuponyedwa mʼmoto?” Iwo anayankha kuti, “Ndi zoonadi, mfumu.”
O zaman Kral Nebukadnessar şaşkınlık içinde birden ayağa kalktı. Danışmanlarına, “Biz ateşin içine bağlı üç kişi atmadık mı?” diye sordu. Danışmanlar, “Kuşkusuz, ey kral” diye karşılık verdiler.
25 Iye anati, “Taonani! Ndikuona amuna anayi akuyendayenda mʼmoto, osamangidwa ndi osapwetekedwa ndipo wachinayi akuoneka ngati mwana wa milungu.”
Kral, “Ben dört kişi görüyorum” dedi, “Ateşin içinde yürüyorlar, bağlarından çözülmüş, hiçbir zarara uğramamışlar. Dördüncünün görünümü de bir ilahi varlığa benziyor.”
26 Pamenepo Nebukadinezara anayandikira pa khomo langʼanjo ya moto ndi kufuwula kuti, “Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, tulukani! Bwerani kuno!” Ndipo Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anatuluka mʼmoto,
Sonra kızgın fırının kapısına yaklaşarak, “Ey Yüce Tanrı'nın kulları Şadrak, Meşak, Abed-Nego, dışarı çıkıp buraya gelin!” diye seslendi. Bunun üzerine Şadrak, Meşak, Abed-Nego ateşin içinden çıktılar.
27 ndipo akalonga, akazembe, abwanamkubwa ndi nduna zamfumu anasonkhana mowazungulira. Anaona kuti moto sunatenthe matupi awo ngakhale tsitsi kumutu kwawo silinapse; zovala zawo sizinapse, ndipo sankamveka fungo la moto.
Satraplar, kaymakamlar, valiler, kralın danışmanları onların çevresinde toplandılar. Adamların bedenlerinde ateşin hiçbir etkisi olmadığını gördüler. Başlarındaki tek saç yanmamış, giysileri değişmemiş, ateşin kokusu üzerlerine sinmemişti.
28 Kenaka Nebukadinezara anati, “Atamandike Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, amene anatumiza mngelo wake ndi kupulumutsa atumiki ake! Iwo anakhulupirira Iye ndi kunyozera lamulo la mfumu ndipo anali okonzeka kutaya moyo wawo koposa kutumikira kapena kupembedza mulungu wina aliyense wosakhala Mulungu wawo.
Bunun üzerine Nebukadnessar, “Şadrak, Meşak ve Abed-Nego'nun Tanrısı'na övgüler olsun!” dedi, “Meleğini gönderip kendisine güvenen kullarını kurtardı. Onlar buyruğuma karşı geldiler, kendi Tanrıları'ndan başka bir ilaha kulluk edip tapınmamak için canlarını tehlikeye attılar.
29 Tsono ndikulamula kuti anthu a mitundu ina kaya chiyankhulo china chili chonse amene anganyoze Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego adulidwe nthulinthuli ndipo nyumba zawo ndidzagwetsa ndi kusandutsa bwinja, popeza palibe Mulungu amene akhoza kupulumutsa mʼnjira yotere.”
İşte buyuruyorum: Hangi halktan, ulustan ya da dilden olursa olsun, Şadrak, Meşak ve Abed-Nego'nun Tanrısı'ndan saygısızca söz eden herkes paramparça edilecek, evleri çöplüğe çevrilecek. Çünkü böyle kurtarabilen başka bir tanrı yoktur.”
30 Ndipo mfumu Nebukadinezara anakweza pa ntchito Sadirake, Mesaki ndi Abedenego mʼchigawo cha Babuloni.
Sonra Şadrak'ı, Meşak'ı, Abed-Nego'yu Babil İli'nde daha yüksek görevlere atadı.

< Danieli 3 >