< Danieli 2 >

1 Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
In the second year of the reign of Nebuchadnezzar, Nebuchadnezzar saw a dream, and his spirit was terrified, and his dream fled from him.
2 Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
Yet the king commanded that the seers, and the astrologers, and the sorcerers, and the Chaldeans be gathered together to reveal to the king his dreams. When they arrived, they stood in front of the king.
3 mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
And the king said to them, “I saw a dream, and, being confused in mind, I do not know what I saw.”
4 Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
And the Chaldeans answered the king in Syriac, “O king, live forever. Tell the dream to your servants, and we will reveal its interpretation.”
5 Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
And in answer, the king said to the Chaldeans, “The memory of it has slipped away from me. Unless you reveal the dream to me, and its meaning, you will be put to death, and your houses will be confiscated.
6 Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
But if you explain the dream and its meaning, you will receive from me rewards, and gifts, and great honor. Therefore, reveal to me the dream and its interpretation.”
7 Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
They answered again and said, “Let the king tell the dream to his servants, and we will reveal its interpretation.”
8 Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
The king answered and said, “I am certain that you are stalling for time because you know that the memory of it has slipped away from me.
9 Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
Therefore, if you do not reveal to me the dream, there is only one conclusion to be reached about you, that the interpretation is likewise false, and packed full of deception, so as to speak before me until the time passes away. And so, tell me the dream, so that I will also know that the interpretation that you tell me is likewise true.”
10 Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
Then the Chaldeans answered before the king, and they said, “There is no man on earth who can accomplish your word, O king. For neither has any king, however great and mighty, asked for an answer of this kind from every seer, and astrologer, and Chaldean.
11 Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
For the answer that you seek, O king, is very difficult. Neither can anyone be found who can reveal it in the sight of the king, except the gods, whose conversation is not with men.”
12 Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
When he heard this, the king commanded, in fury and in great wrath, that all the wise men of Babylon should be destroyed.
13 Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
And when the decree had gone forth, the wise men were put to death; and Daniel and his companions were sought, to be destroyed.
14 Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
Then Daniel inquired, about the law and the sentence, of Arioch, the general of the king’s army, who had gone forth to execute the wise men of Babylon.
15 Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
And he asked him, who had received the orders of the king, for what reason such a cruel sentence had gone forth from the face of the king. And so, when Arioch had revealed the matter to Daniel,
16 Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
Daniel went in and asked of the king that he would grant him time to reveal the solution to the king.
17 Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
And he went into his house and explained the task to Hananiah, and Mishael, and Azariah, his companions,
18 Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
so that they would seek mercy before the face of the God of heaven, about this mystery, and so that Daniel and his companions might not perish with the other wise men of Babylon.
19 Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
Then the secret was revealed to Daniel by a vision in the night. And Daniel blessed the God of heaven,
20 ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
and speaking aloud, he said, “May the name of the Lord be blessed by the present generation and forever; for wisdom and fortitude are his.
21 Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
And he alters the times and the ages. He takes away kingdoms and he establishes them. He gives wisdom to those who are wise and teaching skills to those who understand.
22 Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
He reveals deep and hidden things, and he knows what has been established in darkness. And the light is with him.
23 Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
To you, God of our fathers, I confess, and you, I praise. For you have given wisdom and fortitude to me, and now you have revealed to me what we asked of you, for you have uncovered for us the king’s thoughts.”
24 Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
After this, Daniel went in to Arioch, whom the king had appointed to destroy the wise men of Babylon, and he spoke to him in this way, “Do not destroy the wise men of Babylon. Bring me in before the king, and I will explain the solution to the king.”
25 Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
Then Arioch quickly brought Daniel to the king, and he said to him, “I have found a man of the sons of the transmigration of Judah, who would announce the solution to the king.”
26 Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
The king answered and said to Daniel, whose name was Belteshazzar, “Do you really think that you can reveal to me the dream that I saw and its interpretation?”
27 Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
And Daniel, facing the king, answered and said, “The secret that the king seeks, the wise men, the seers, and the soothsayers are unable to reveal to the king.
28 koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
But there is a God in heaven who reveals mysteries, who has revealed to you, king Nebuchadnezzar, what will happen in the latter times. Your dream and the visions of your head upon your bed, are such as these.
29 “Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
You, O king, began to think, while in your blanket, about what will be hereafter. And he who reveals secrets showed you what will happen.
30 Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
To me, likewise, this mystery is revealed, not according to the wisdom that is in me more than in other living things, but so that the interpretation might be made manifest to the king, and so that you may know the thoughts of your mind.
31 “Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
You, O king, saw, and behold, something like a great statue. This statue, which was great and high, stood exalted above you, and you considered how terrible it was.
32 Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
The head of this statue was of the finest gold, but the breast and the arms were of silver, and further on, the belly and the thighs were of brass;
33 Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
but the shins were of iron, a certain part of the feet were of iron and another part were of clay.
34 Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
And so you looked until a stone was broken off without hands from a mountain, and it struck the statue on its feet, which were of iron and clay, and it shattered them.
35 Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
Then the iron, the clay, the brass, the silver, and the gold were crushed together and diminished like the ashes of a summer courtyard, and they were quickly taken away by the wind, and no place was found for them; but the stone that struck the statue became a great mountain and filled the whole earth.
36 “Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
This is the dream; we will also tell its interpretation before you, O king.
37 Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
You are a king among kings, and the God of heaven has given to you a kingdom, and fortitude, and power, and glory,
38 Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
and all the places wherein the sons of men and the beasts of the field dwell. He has likewise given the flying creatures of the air into your hand, and he has placed all things under your realm. Therefore, you are the head of gold.
39 “Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
And after you, another kingdom will rise up, inferior to you, of silver, and another third kingdom of brass, which will rule over the whole world.
40 Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
And the fourth kingdom will be like iron. Just as iron shatters and conquers all things, so will it shatter and crush all these.
41 Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
Furthermore, because you saw the feet and the toes to be part of potter’s clay and part of iron, the kingdom will be divided, but still, from the slip of iron it will take its origin, since you saw the iron mingled with the earthenware from clay.
42 Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
And as the toes of the feet were partly of iron and partly of clay, part of the kingdom will be strong and part will be crushed.
43 Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
Yet, because you saw the iron mingled with pottery from the earth, they will indeed be combined together with the offspring of man, but they will not adhere to one another, just as iron cannot be mixed with earthenware.
44 “Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
But in the days of those kingdoms, the God of heaven will inspire a kingdom that will never be destroyed, and his kingdom will not be handed over to another people, and it will crush and will consume all these kingdoms, and this kingdom itself will stand in eternity.
45 Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
In accordance with what you saw, because the stone was torn away from the mountain without hands, and it crushed the earthenware, and the iron, and the brass, and the silver, and the gold, the great God has shown the king what will happen after this. And the dream is true, and its interpretation is faithful.”
46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
Then king Nebuchadnezzar fell on his face and adored Daniel, and he commanded that they should offer in sacrifice to him victims and incense.
47 Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
And so the king spoke with Daniel and said, “Truly, your God is the God of gods, and Lord of kings, and also a revealer of secrets, since you could uncover this mystery.”
48 Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
Then the king raised Daniel to a high rank and gave him many great gifts, and he appointed him as leader over all the provinces of Babylon and as chief of the magistrates over all the other wise men of Babylon.
49 Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.
However, Daniel required of the king that he appoint Shadrach, Meshach, and Abednego over the works of the province of Babylon. But Daniel himself was at the king’s door.

< Danieli 2 >