< Danieli 2 >
1 Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
Nebukhanezar ram kah a kum bae ah Nebukhanezar loh mang a man tih a mueihla a cahoeh dongah amah khaw a ih a hoelh pah.
2 Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
Te dongah manghai loh hmayuep neh khungvatuk khaw, hlangbi neh manghai kah a mang aka thui la Khalden rhoek khaw khue hamla a thui pah. Te dongah a pha uh neh manghai mikhmuh ah pai uh.
3 mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
Te vaengah manghai loh amih te, “Mang ka man tih mang te ming hamla ka mueihla a cahoeh,” a ti nah.
4 Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
Khalden rhoek loh manghai te Aramaih ol la, “Manghai tah, dungyan la hing pai saeh. Mang te na tueihyoeih rhoek taengah thui lamtah na tueihyoeih loh thuicaihnah ka phoe eh?,” a ti nauh.
5 Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
Manghai loh a doo tih Khalden rhoek te, “Kai lamkah ol he cak coeng. Ka mang neh a thuicaihnah na mingpha sak pawt atah maehpoel la n'sah vetih na im te kawnhnawt om ni.
6 Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
Tedae mang neh a thuicaihnah te na phoe uh atah kai taeng lamkah kutdoe, thapang neh thangpomnah muep na dang uh ni. Mang neh a thuicaihnah te kai taengah phoe uh dae,” a ti nah.
7 Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
Koep a doo uh tih, “Manghai kah mang te a tueihyoeih taengah thui saeh lamtah a thuicaihnah kam phoe uh eh,” a ti nauh.
8 Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
Manghai loh a doo tih, “Kai lamkah ol a cak te na hmuh dongah nangmih a tue na yuengyet uh tila rhep ka ming.
9 Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
Ka mang te na mingpha sak uh pawt atah nangmih oltlueh pakhat ni a om. Laithae ol neh a tue a hoilae hil ka taengah a hong thui ham na cai khaw na cai uh. Mang te kai taengah thui uh dae lamtah kai hamla a thuingaihnah nan phoe uh te ka ming eh?,” a ti nah.
10 Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
Manghai taengkah Khalden rhoek loh a doo uh tih, “Manghai kah ol phoe hamla aka noeng te diklai ah hlang a om moenih. Boeilen neh aka hung manghai boeih long khaw he bang ol he hmayuep, rhaitonghma neh Khalden boeih he a dawt noek moenih.
11 Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
Manghai kah a dawt he tongmang ol tih manghai taengah te aka phoe thai he pakhat khaw a om moenih. Pathen rhoek pawt atah amih pumsa lakli kah khosaknah he te bang a om moenih,” a ti uh.
12 Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
He kong dongah he manghai tah sai tih a thintoek muep. Te dongah Babylon hlang cueih boeih te thup hamla a thui.
13 Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
Hlang cueih ngawn hamla oltlueh a khuen dongah Daniel neh a hui khaw ngawn hamla a tlap uh.
14 Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
Te dongah Babylon hlang cueih te ngawn hamla aka cet manghai kah imtawt boeilen Aryawk te Daniel loh khuelnah neh saithainah neh a mael sak.
15 Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
Manghai aka hung Aryawk te a doo tih, “Balae tih manghai taeng lamkah oltlueh he a tok aih?” a ti nah hatah ol te Aryawk loh Daniel te a ming sak.
16 Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
Te dongah Daniel te cet tih amah te a tue a paek phoeiah thuingaihnah te manghai mah taengah thui pah hamla manghai taengah a bih.
17 Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
Te phoeiah Daniel te a im la mael tih a hui rhoek Hananiah, Mishael neh Azariah taengah olka te a thuicaih pah.
18 Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
He oldung dongah Daniel neh a hui rhoek neh Babylon kah hlang cueih a ngen te thup pawt hamla vaan Pathen taeng lamkah haidamnah a bih.
19 Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
Te khoyin kah mangthui dongah tah Daniel taengah oldung te a thoeng pah. Te dongah Daniel loh vaan kah Pathen te a koeh.
20 ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
Daniel loh a doo tih, “Pathen tah a ming om pai saeh, khosuen lamloh kumhal duela a yoethen pai. Cueihnah neh thayung thamal khaw amah kah ni.
21 Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
Amah loh a tue neh khoning a hoilae. Manghai rhoek te a khoe tih manghai patoeng a thoh. Aka cueih taengah cueihnah neh yakmingnah aka thuicaih taengah mingnah a paek.
22 Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
Amah loh a thuuk neh a thuh khaw a tueng sak. Hmuepnah neh vangnah khuikah te khaw a ming. Te dongah vangnah tah anih taengah om.
23 Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
A pa rhoek kah Pathen namah te kang uem tih kang oep. Kai he ka taengah cueihnah neh thayung thamal nan paek. Namah taengah kam bih bangla kai nan ming sak coeng tih manghai kah olka te kaimih nan ming sak,” a ti.
24 Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
Te dongah he kong neh Daniel te manghai loh a hmoel tih Babylon hlang cueih rhoek thup hamla aka cet Aryawk taengla cet. Te phoeiah anih te, “Babylon hlang cueih rhoek te thup boeh, kai he manghai taengla n'hui lamtah a thuingaihnah te manghai taengah ka phoe eh?,” a ti nah.
25 Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
Te dongah Aryawk loh Daniel te manghai taengah thintawn la a khuen tih, “Manghai taengah a thuingaihnah thuicaih hamla Judah hlangsol koca lamkah hlang ka hmuh,” a ti nah.
26 Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
Manghai loh a doo tih Daniel la a ming aka om Belteshazzar te, “Na om pai a? Mang ka man neh a thuingaihnah te kai taengah thuicaih hamla aka noeng, na om rhoe a?” a ti nah.
27 Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
Daniel loh manghai taengah a doo tih, “Manghai kah na dawt he oldung tih manghai taengah phoe hamla aka noeng hlang cueih, rhaitonghma, hmayuep rhoek, aisi aka suep a om moenih.
28 koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
Tedae oldung aka tueng he vaan ah Pathen om tih hmailong khohnin ah metla a om ham khaw manghai Nebukhadnezzar te na thingkong dongah na mang neh na lu dongkah mangthui neh he he han thuicaih coeng.
29 “Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
Manghai nang, na thingkong dongkah na poeknah te he lamloh aka om la thoeng coeng. Aka om ham te ni oldung aka tueng loh nang m'ming sak.
30 Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
Kai khaw ka taengah oldung a tueng he khaw mulhing boeih lakah kamah kah cueihnah a om dongah moenih. Tedae te kong dongah he a thuingaihnah te manghai taengah a thuicaih vetih na thinko kah poeknah loh a ming nah ham ni.
31 “Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
Manghai nang, na hmuh tih na om coeng. Na mikhmuh ah muei pakhat la aka pai te. Tekah muei tah len sang tih a aa yet. A suisak mah rhimom coeng.
32 Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
Te muei kah a lu te sui cim, a rhang neh a ban rhoi te cak, a bung neh a phai rhoi tah rhohum,
33 Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
A khotanlan rhoi te thi, a khobom te a ngawncawn te thi tih a ngawncawn dikpo la om.
34 Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
Na sawt li vaengah kut loh a saii mueh lungto te coe tih muei te a khobom dongkah a dae. Te vaengah thi neh dikpo khaw phaeng a nuei pah.
35 Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
Te phoeiah thi, dikpo, rhohum, cak neh sui khaw pakhat la phaeng nuei uh. Te dongah khohal cangtil hmuen kah cangkik bangla om tih te rhoek te khohli loh a yawn. Te dongah te rhoek te a hmuen boeih hmu voel pawh. Tedae muei dongah aka cu lungto te tlang sang la poeh tih diklai pum ah bae.
36 “Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
Mang kah a thuingaihnah te manghai taengah ka thui uh pawn eh.
37 Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
Manghai nang, namah he manghai rhoek kah manghai ni. Vaan kah Pathen loh ram neh thadueng khaw, sarhi neh thangpomnah khaw namah taengah m'paek coeng.
38 Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
Khosa, khosa boeih khuikah hlang koca rhoek khaw, kohong rhamsa neh vaan kah vaa khaw na kut ah m'paek. A cungkuem soah nang m'boei sak tih nang te na lu sui la hang khueh.
39 “Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
Nang phoeiah tah nang lakah diklai la aka yalh ram pakhat pai ni. A pathum dongkah ram tahrhohum vetih diklai boeih soah boei ni.
40 Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
A pali kah ram tah thi ning bangla om ni. He kong ah he thi loh a neet tih boeih a noeng. Te dongah thi bangla a cungkuem he a phop coeng tih a nuei a pil la om ni.
41 Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
Na hmuh bangla khobom neh khodawn tah a ngawncawn te ambop kah dikpo tih a ngawncawn thi. A khuiah thi dongkah thacang om cakhaw ram te aka rhek aka boe la om ni. Te kong ah ni thi neh laicang dikpo neh a thoek na hmuh.
42 Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
Khobom dongkah khodawn khaw a ngawncawn, a ngawncawn thi tih, a ngawncawn a ngawncawn tah dikpo. Te dongah ram ngawncawn te a ning la om vetih a ngawncawn tah a poo la om ni.
43 Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
Na hmuh bangla thi neh laicang dikpo a thoek dongah hlang kah tiingan thoek uh ni. Tedae neh thi neh dikpo a thoek thai pawt bangla he neh ke khaw aka pitpom uh la om mahpawh.
44 “Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
Vaan Pathen loh manghai rhoek te amamih tue vaengah a pai sak vetih a ram tah kumhal due la tim mahpawh. Ram te pilnam tloe taengah a nuei la hlah mahpawh. Ram boeih he tlum cakhaw te tah kumhal duela cak ni.
45 Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
He kong dongah tlang lamkah kut neh saii mueh lungto a coe na hmuh. Te dongah thi, rhohum, dikpo, cak neh sui khaw vingving nuei. Boeilen Pathen loh tahae lamloh aka om ham te manghai taengah m'ming sak. Te dongah mang he tong tih a thuingaihnah uepom coeng,” a ti nah.
46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
Te dongah manghai Nebukhadnezzar loh a maelhmai longah buluk tih Daniel taengah bakop. Te dongah khosaa neh a hlihlim te a taengah doe ham a thui pah.
47 Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
Manghai loh Daniel te a doo tih, “Nangmih kah Pathen tah oltak pai ni. Pathen rhoek kah Pathen, manghai rhoek kah Boeipa ni. He oldung tueng hamla na noeng dongah ni oldung he nan tueng,” a ti nah.
48 Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
Te phoeiah manghai loh Daniel te a pomsang tih anih te boeilen kutdoe muep a paek. Babylon paeng pum soah anih te a boei sak tih Babylon hlang cueih boeih lakah boeilen khoboei la a khueh.
49 Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.
Daniel loh manghai taengah a bih tih Sadrakh, Meshach neh Abednego rhoek te Babylon paeng kah taemnah soah a khueh. Te vaengah Daniel tah manghai vongka ah kho a sak.