< Danieli 12 >

1 “Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
Ob tistem času bo vstal Mihael, veliki princ, ki stoji za otroke tvojega ljudstva in tam bo čas stiske, tak, kakršnega ni bilo, odkar je bil tam narod, celó do tega istega časa. In ob tistem času bo tvoje ljudstvo osvobojeno, vsak, kdor bo najden zapisan v knjigi.
2 Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
Mnogi izmed teh, ki spijo v prahu zemlje, se bodo zbudili, nekateri za večno življenje, nekateri pa za sramoto in večno zaničevanje.
3 Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
Tisti, ki so modri, bodo svetili kakor sijaj nebesnega svoda in tisti, ki mnoge obračajo k pravičnosti, [bodo] kakor zvezde na veke vekov.
4 Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
Toda ti, oh Daniel, zakleni besede in zapečati knjigo, celó do časa konca. Mnogi bodo tekali sem ter tja in spoznanje se bo povečalo.«
5 Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
Potem sem jaz, Daniel, pogledal in glej tam sta stala druga dva, eden na tej strani rečnega brega, drugi pa na drugi strani rečnega brega.
6 Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
In eden je rekel možu, oblečenemu v lan, ki je bil na vodah reke: »Doklej bo to do konca teh čudežev?«
7 Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
Slišal sem moža, oblečenega v lan, ki je bil na vodah reke, ko je držal svojo desno roko in svojo levo roko k nebu in prisegel pri njem, ki živi na veke, da bo to za čas, [dva] časa in polovico, in ko bo dovršil, da razkropi moč svetega ljudstva, se bodo vse te stvari končale.
8 Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
Slišal sem, toda nisem razumel. Potem sem rekel: »Oh moj Gospod, kakšen bo konec teh stvari?«
9 Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
Rekel je: »Pojdi svojo pot, Daniel, kajti besede so zaklenjene in zapečatene do časa konca.
10 Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
Mnogi bodo očiščeni, pobeljeni in preizkušeni, toda zlobni bodo delali zlobno in nihče izmed zlobnih ne bo razumel, toda modri bodo razumeli.
11 “Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
Od časa, ko bo dnevno žrtvovanje odvzeto in postavljena ogabnost, ki dela opustošenje, bo tisoč dvesto devetdeset dni.
12 Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
Blagoslovljen je kdor čaka in prihaja k tisoč tristo petintridesetim dnem.
13 “Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”
Toda ti pojdi svojo pot, dokler ne bo konec, kajti počival boš in stal v svojem deležu ob koncu dni.«

< Danieli 12 >